Aroma 8 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 8:1-39

Moyo Watsopano mwa Khristu

1Choncho, tsopano amene ali mwa Khristu Yesu alibe mlandu owatsutsa 2chifukwa mwa Khristu Yesu, lamulo la Mzimu Woyera amene amapereka moyo, lawamasula ku lamulo la tchimo ndi la imfa. 3Pakuti zimene Malamulo sanathe kuzichita, popeza anali ofowoka chifukwa cha khalidwe lathu la uchimo, Mulungu anazichita potumiza Mwana wake mʼchifanizo cha munthu ochimwa kuti akhale nsembe yauchimo. Ndipo Iye anagonjetsa tchimo mʼthupi la munthu, 4ndi cholinga chakuti chilungamo chofunikira cha lamulo chikwaniritsidwe kwathunthu mwa ife amene sitikhala monga mwachikhalidwe chathu cha uchimo koma mwa Mzimu.

5Pakuti anthu amene amakhala monga mwa makhalidwe oyipa a thupi amayika malingaliro awo pa zinthu zathupi. Koma amene amakhala monga mwa Mzimu amayika malingaliro awo pa zinthu za Mzimu. 6Kuyika mtima pa zathupi ndi imfa koma kuyika mtima pa za Mzimu ndi moyo ndi mtendere. 7Pakuti mtima umene wakhazikika pa zathupi ndi wodana ndi Mulungu. Sunagonjere lamulo la Mulungu ndipo sungathe kutero. 8Ndipo anthu amene amalamulidwa ndi khalidwe lauchimo sangathe kukondweretsa Mulungu.

9Koma inu simulamulidwanso ndi khalidwe lanu lauchimo koma ndi Mzimu ngati Mzimu wa Mulungu akhaladi mwa inu. Koma ngati munthu aliyense alibe Mzimu wa Khristu, iyeyu si wa Khristu. 10Ndipo ngati Khristu ali mwa inu, thupi lanu ndi lakufa chifukwa cha uchimo, koma mzimu wanu ndi wamoyo chifukwa cha chilungamo. 11Ndipo ngati Mzimu wa Mulungu amene anaukitsa Yesu kwa akufa akhala mwa inu, Iyeyo amene anaukitsa Khristu kwa akufa adzapatsanso moyo matupi anu amene amafa kudzera mwa Mzimu wake amene amakhala mwa inu.

12Kotero abale, ife tili ndi zoti tikwaniritse, koma osati za khalidwe lathu lauchimo, kumachita zofuna zake. 13Pakuti ngati inu mukhala monga mwa khalidwe lauchimo, mudzafa. Koma ngati mwa Mzimu mupha ntchito zoyipa zathupi, mudzakhala ndi moyo. 14Onse amene amatsogozedwa ndi Mzimu wa Mulungu ndi ana a Mulungu. 15Mzimu amene inu munalandira samakusandutsani akapolo, kuti muzikhalanso amantha, koma Mzimu amakusandutsani ana. Ndipo mwa Iye ife timafuwula kuti, “Abba, Atate.” 16Mzimu mwini amavomerezana ndi mzimu wathu kuti ife ndife ana a Mulungu. 17Tsono ngati tili ana ake, ndiye kuti ndife olowa mʼmalo a Mulungu ndi olowa mʼmalo pamodzi ndi Khristu. Ngati ife timva zowawa pamodzi ndi Khristu, tidzalandiranso ndi ulemerero womwe pamodzi naye.

Ulemerero wa Mʼtsogolo

18Ine ndiganiza kuti masautso amene tikuwamva nthawi ino, sakufanana ndi ulemerero umene udzaonetsedwa mwa ife. 19Pakuti chilengedwe chikudikira ndi chiyembekezo kuonetsedwa poyera kwa ana a Mulungu. 20Pakuti chilengedwe sichinasankhe kugonjera zopanda pake, koma mwachifuniro cha Iye amene analola kuti chigonjere. Koma chili ndi chiyembekezo 21chakuti chidzamasulidwa ku ukapolo wa chivundi ndi kulandiranso ufulu ndi ulemerero wa ana a Mulungu.

22Ife tikudziwa kuti chilengedwe chonse chakhala chikubuwula ndi ululu ngati ululu wa nthawi yobereka mwana mpaka tsopano lino. 23Si zokhazo ayi, ngakhale ife tomwe, amene tili ndi zipatso zoyamba za Mzimu, tikubuwulira mʼkati mwathu pomwe tikudikira mwachidwi kusankhidwa kwathu ngati ana, kuwomboledwa kwa matupi athu. 24Pakuti ife tinapulumutsidwa mʼchiyembekezo ichi. Koma chiyembekezo chimene chimaoneka si chiyembekezo ayi. Kodi ndani amene amayembekezera chimene ali nacho kale? 25Koma ngati ife tiyembekeza chimene tikanalibe, ndiye kuti tikuyembekeza modekha mtima.

26Momwemonso, Mzimu amatithandiza ife mʼkufowoka kwathu. Ife sitidziwa momwe tiyenera kupempherera koma Mzimu mwini amatipempherera mobuwula ndi mawu osafotokozedwa. 27Koma Iye amene amasanthula mitima yathu amadziwa maganizo a Mzimu, chifukwa Mzimu amapempherera oyera mtima molingana ndi chifuniro cha Mulungu.

Oposa Agonjetsi

28Ndipo ife tikudziwa kuti zinthu zonse zimathandizana kuwachitira ubwino amene amakonda Mulungu, amene anayitanidwa monga mwa cholinga chake. 29Pakuti amene Mulungu anawadziwiratu, anawasankhiratunso kuti akonzedwe mʼchifanizo cha Mwana wake, kuti Iye akhale Mwana woyamba kubadwa mwa abale ambiri. 30Iwo amene anawasankhiratu, anawayitananso. Amene Iye anawayitana anawalungamitsanso ndipo amene anawalungamitsa anawapatsanso ulemerero.

31Nanga tsono tidzanena chiyani pa izi? Ngati Mulungu ali mbali yathu, adzatitsutsa ife ndani? 32Iye amene sanatimane Mwana wake wa Iye yekha, koma anamupereka chifukwa cha ife tonse. Iye adzalekeranjinso pamodzi naye kutipatsa ife zinthu zonse mwaulere? 33Ndani amene adzabweretsa mlandu kutsutsa amene Mulungu anawasankha? Ndi Mulungu amene amalungamitsa. 34Ndani amene angatipeze ife olakwa? Palibe. Khristu Yesu amene anafa, kuposera pamenepo, amene anaukitsidwa ndi moyo, amene ali kudzanja lamanja la Mulungu ndiye amene akutipempherera. 35Ndani amene adzatilekanitsa ife ndi chikondi cha Khristu? Kodi ndi masautso, kapena zowawa, kapena mazunzo, kapena njala, kapena umaliseche, kapena choopsa, kapena lupanga? 36Monga kwalembedwa:

“Chifukwa cha inu, ife tikuphedwa tsiku lonse:

ife tikutengedwa ngati nkhosa zoti zikaphedwe.”

37Ayi, mu zonsezi ife ndife oposa agonjetsi mwa Iye amene anatikonda. 38Pakuti ine ndatsimikiza ndi mtima wonse kuti ngakhale imfa, kapena moyo, ngakhale angelo, kapena ziwanda, ngakhale zinthu zilipo, kapena zili mʼtsogolo, kapena mphamvu zina, 39ngakhale kutalika, kapena kuya, kapena chilichonse mʼchilengedwe chonse, sizingathe kutisiyanitsa ndi chikondi cha Mulungu chimene chili mwa Khristu Yesu Ambuye athu.

New Russian Translation

Римлянам 8:1-39

Жизнь в Духе

1Теперь тем, кто находится в единении со Христом Иисусом, нет никакого осуждения, 2потому что Закон Духа, дающего жизнь через Иисуса Христа, освободил тебя от закона греха и смерти. 3То, что не в силах был сделать Закон, не способный перебороть нашу греховную природу8:3 Нашу греховную природу – букв.: «нашу плоть»., сделал Бог. Он послал Своего Сына в теле, подобном греховному человеческому телу, и осудил грех, сделав Его тело жертвой за наши грехи. 4Он сделал это для того, чтобы справедливые требования Закона были исполнены в нас, живущих не по греховной природе8:4 Букв.: «по плоти». Так же и в других местах этой книги., а по Духу.

5Живущие по греховной природе думают о том, чего хочет эта природа, а живущие по Духу – о том, чего желает Дух. 6Мысли, исходящие от греховной природы, ведут к смерти, а мысли, исходящие от Духа, – к жизни и миру. 7Греховный образ мыслей враждебен Богу. Он не подчиняется Божьему Закону, да и не может подчиняться. 8Поэтому живущие под властью греховной природы не могут угодить Богу.

9Но если Дух Божий живет в вас, то вы уже находитесь не под властью греховной природы, а под властью Духа. А в ком нет Духа Христа, тот и не принадлежит Ему. 10Если же в вас живет Христос, то ваше тело мертво8:10 Или: «смертно». вследствие греха, а Дух – это ваша жизнь8:10 См. 1 Кор. 6:17-19; или: «дает вам жизнь». для праведности8:10 Или: «а дух жив благодаря праведности».. 11Если в вас живет Дух Того, Кто воскресил Иисуса из мертвых, то Воскресивший из мертвых Иисуса оживит Духом Своим, живущим в вас, и ваши смертные тела.

12Поэтому, братья, мы не должники греховной природы, чтобы жить так, как она нам диктует. 13Если вы живете так, как вам диктует греховная природа, вы погибнете. Если же вы Духом умерщвляете ее действия, то будете жить. 14Потому что все, кем руководит Дух Божий, являются сыновьями Божьими. 15Вы получили не дух рабства, чтобы опять жить в страхе, а Духа усыновления, Которым мы и обращаемся к Богу: «Абба!8:15 Это ласкательное обращение к отцу на арамейском языке. Отец!» 16Дух Божий свидетельствует вместе с нашим духом8:16 Или: «свидетельствует нашему духу». о том, что мы дети Божьи. 17А если мы Его дети, то и наследники. Наследники Божьи и сонаследники Христу. Ведь если мы страдаем вместе с Ним, то вместе с Ним и будем прославлены.

Будущая слава

18Я считаю, что наши нынешние страдания ничего не значат в сравнении с той славой, которая ожидает нас в будущем. 19Ведь все творение с нетерпением ожидает откровения сыновей Божьих. 20Потому что творение было подчинено бессмысленности существования не по своей воле, а по воле Того, Кто подчинил его8:20 См. Быт. 3:14-19.. Но у творения есть надежда на 21освобождение от власти тления, чтобы обрести ту же славную свободу, что и дети Божьи.

22Мы знаем, что все творение до сих пор стонет и мучается, как женщина при родах8:22 Ср. Мат. 24:8 и сноску на этот стих., 23и не только оно, но и мы, получившие Духа как залог того, что нас ожидает8:23 Букв.: «первые плоды Духа»., тоже внутренне стонем, с нетерпением ожидая полного усыновления – искупления наших тел. 24В этой надежде мы и спасены. Но надежда не бывает направлена на то, что уже видимо; если что-то уже видимо, то на что же надеяться? 25Мы надеемся на то, чего не видим, и терпеливо этого ожидаем.

26Также и Дух помогает нам при всей нашей слабости. Мы не знаем даже, о чем нам следует молиться, но Дух Сам ходатайствует за нас вздохами, которые не могут быть выражены словами. 27Тот, Кто исследует сердца, знает мысль Духа, потому что Дух ходатайствует за святых в согласии с Божьей волей.

Любовь Божья в Иисусе Христе

28Мы знаем, что Бог все обращает во благо для тех, кто любит Его и кого Он призвал по Своему замыслу. 29Потому что кого Он заранее узнал, тех и предопределил быть подобными образу8:29 Ср. Быт. 1:26-27. Своего Сына, чтобы Иисус стал Первенцем8:29 В древние времена первенец занимал самое высокое положение в семье после отца (см. Быт. 49:3) и принадлежал Богу (см. Исх. 13:2, 12-13). Таким же образом Иисус имеет уникальные отношения с Богом и занимает самое высокое положение среди верующих. среди множества братьев. 30А кого Бог предопределил, тех Он и призвал, а кого призвал, тех и оправдал, а кого оправдал, тех и прославил.

31Что же нам сказать об этом? Если Бог за нас, то кто против нас? 32Тот, Кто не пожалел Своего Сына, но отдал Его за всех нас, разве не дарует с Ним и всего остального? 33Кто будет обвинять избранных Богом? Если Бог оправдывает, 34кто может осудить? Христос Иисус, Который умер, но воскрес и сейчас находится по правую руку от Бога, ходатайствует за нас. 35Что может отлучить нас от любви Христа? Скорбь или трудности? Преследования или голод? Нагота или угроза казни? 36Написано:

«Ради Тебя убивают нас всякий день

и смотрят на нас, как на овец перед бойней»8:36 Пс. 43:23..

37Но мы одерживаем величайшую победу над всем этим благодаря Тому, Кто полюбил нас. 38И я уверен, что ни смерть, ни жизнь, ни ангелы, ни власти, ни настоящее, ни будущее, ни силы, 39ни высота, ни глубина – ничто во всем творении не может отлучить нас от любви Бога во Христе Иисусе, нашем Господе!