Aroma 6 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 6:1-23

Kufa ku Tchimo, Kukhala ndi Moyo mwa Khristu

1Nanga tinene chiyani? Kodi tipitirire kuchimwa kuti chisomo chichulukebe? 2Ayi. Mʼnjira iliyonse! Popeza tinafa ku tchimo, nanga tidzapitirira bwanji kukhalabe mʼmenemo? 3Kodi simukudziwa kuti tonse amene tinabatizidwa mwa Khristu Yesu tinabatizidwa mu imfa yake? 4Chifukwa chake ife tinayikidwa mʼmanda pamodzi ndi Iye mwa ubatizo. Tinalowa mu imfa ndi cholinga choti monga momwe Khristu anaukitsidwa kwa akufa ndi ulemerero wa Atate, ifenso tikakhale mʼmoyo watsopano.

5Pakuti ngati ife tinakhala amodzi ndi Iye mu imfa yake, tidzakhalanso ndithu amodzi ndi Iye mu kuuka kwake. 6Ife tikudziwa kuti umunthu wathu wakale unapachikidwa pamodzi ndi Iye kuti thupi la uchimo likhale lopanda mphamvu ndi kuti tisakakhalenso akapolo a tchimo 7chifukwa aliyense amene anafa anamasuka ku tchimo.

8Koma ngati tinafa pamodzi ndi Khristu, tikhulupirira kuti tidzakhalanso ndi moyo pamodzi ndi Iye. 9Pakuti tikudziwa kuti popeza Khristu anaukitsidwa kwa akufa, Iye sangafenso. Imfa ilibenso mphamvu pa Iye. 10Imfa imene Iye anafa, anafa ku tchimo kamodzi kokha, koma moyo umene akhala ndi wa kwa Mulungu.

11Kotero inunso, mudzione nokha ngati akufa ku tchimo koma a moyo kwa Mulungu mwa Khristu Yesu. 12Nʼchifukwa chake, musalole tchimo lilamulire matupi anu amene anafa kuti mumvere zilakolako zonyansa. 13Musapereke ziwalo zathupi lanu ku tchimo, ngati zipangizo zamakhalidwe oyipa. Mʼmalo mwake, mudzipereke kwa Mulungu, ngati amene achoka ku imfa kupita ku moyo. Ndipo mupereke ziwalo zathupi lanu ngati zipangizo zachilungamo. 14Tchimo silidzakhalanso ndi mphamvu pa inu, chifukwa Malamulo sakulamulira moyo wanu koma chisomo.

Ife Ndife Akapolo a Mulungu

15Nʼchiyani tsono? Kodi tidzichimwa chifukwa sitikulamulidwa ndi Malamulo koma chisomo? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! 16Kodi inu simudziwa kuti pamene mudzipereka kwa wina wake, kumumvera ngati akapolo, ndinu akapolo a amene mumumvera? Ngati ndinu akapolo a tchimo mudzafa. Koma ngati ndinu akapolo akumvera, mudzakhala olungama pamaso pake. 17Koma ayamikidwe Mulungu pakuti ngakhale munali akapolo a tchimo, munamvera ndi mtima wonse chiphunzitso chimene munalandira. 18Inu munamasulidwa ku tchimo ndipo tsopano mwasanduka akapolo achilungamo.

19Ine ndikufanizira zinthu za tsiku ndi tsiku chifukwa chikhalidwe chanu nʼchofowoka. Monga momwe munkapereka ziwalo za matupi kukhala akapolo a zonyansa ndi makhalidwe oyipa, zimene zimanka zichulukirabe, choncho tsopano dziperekeni ziwalozo kuti zikhale akapolo achilungamo ndi a kuyera mtima. 20Pomwe munali akapolo atchimo, simunkalabadira za chilungamo. 21Kodi munapeza phindu lanji pochita zinthu zimenezi, zomwe tsopano mukuchita nazo manyazi? Zinthu zimenezo zotsatira zake ndi imfa! 22Koma tsopano pakuti inu mwamasulidwa ku tchimo ndipo mwasanduka akapolo a Mulungu, phindu lomwe mulipeza ndi kuyera mtima ndipo chotsatira chake ndi moyo wosatha. 23Pakuti malipiro a tchimo ndi imfa, koma mphatso yaulere imene Mulungu amapereka ndi moyo wosatha mwa Khristu Yesu Ambuye athu.

Słowo Życia

Rzymian 6:1-23

Martwi dla grzechu, ożywieni dla Chrystusa

1Czy wobec tego mamy nadal grzeszyć, aby łaska stała się bardziej widoczna? 2Oczywiście, że nie! Skoro umarliśmy dla grzechu, to jak możemy nadal w nim żyć? 3Czy nie rozumiecie tego, że gdy przyjmując chrzest utożsamiliśmy się z Chrystusem Jezusem, zjednoczyliśmy się z Nim również w Jego śmierci? 4Przez chrzest zostaliśmy razem z Nim pogrzebani, zanurzając się w Jego śmierci. A skoro Bóg Ojciec swoją potężną mocą wzbudził Jezusa do życia, to również my powinniśmy żyć nowym życiem.

5Skoro zostaliśmy złączeni z Jezusem w śmierci, to będziemy z Nim złączeni również w zmartwychwstaniu. 6Pamiętajmy o tym, że nasze dawne życie zostało wraz z Jezusem przybite do krzyża, a nasza grzeszna natura została obezwładniona, abyśmy już nie służyli grzechowi. 7Kto umiera, staje się wolny od grzechu. 8Skoro więc umarliśmy z Chrystusem, to wierzymy, że razem z Nim będziemy żyli. 9Wiemy bowiem, że Jezus, powstawszy z martwych, już nigdy nie umrze—śmierć nie ma nad Nim żadnej władzy. 10Umarł tylko raz, aby pokonać grzech, a teraz żyje dla Boga.

11Dlatego wy również uważajcie siebie za martwych dla grzechu, a żyjących dla Boga, dzięki Chrystusowi Jezusowi. 12Niech więc grzech nie panuje już nad waszym doczesnym ciałem—nie poddawajcie się grzesznym pragnieniom! 13Nie czyńcie z żadnej części ciała narzędzia grzechu, lecz całkowicie powierzcie się Bogu! Byliście martwi, a ożyliście, więc niech całe wasze ciało będzie teraz narzędziem działania Boga. 14Grzech nie musi być już dłużej waszym władcą, gdyż nie podlegacie przepisom Prawa Mojżesza, lecz Bożej łasce.

Niewolnicy prawości

15Czy zatem możemy swobodnie grzeszyć, dlatego że nie podlegamy Prawu, ale łasce? W żadnym wypadku! 16Czy nie wiecie, że jesteście zależni od tego, komu służycie? Albo wybieracie grzech i śmierć, albo posłuszeństwo i prawość. 17Dziękuję Bogu za to, że chociaż kiedyś byliście niewolnikami grzechu, całym sercem przyjęliście przekazaną wam Bożą naukę. 18I zostaliście uwolnieni spod władzy grzechu, aby teraz być niewolnikami prawości. 19Pozwólcie, że tak to wyjaśnię: Kiedyś różne części ciała traktowaliście jak niewolników spełniających wasze grzeszne pragnienia. Teraz jednak wykorzystujcie je jako niewolników wykonujących to, co słuszne i święte.

20Będąc w niewoli zła, nie musieliście postępować w sposób dobry i prawy. 21Ale jaki był skutek waszych czynów, których teraz tak się wstydzicie? Wieczna śmierć! 22Jako uwolnieni spod władzy grzechu jesteście poddanymi Boga, a to doprowadzi was do świętości i wiecznego życia. 23Zapłatą za grzech jest śmierć, ale Bóg darował nam życie wieczne w Jezusie Chrystusie, naszym Panu!