Aroma 5 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 5:1-21

Mtendere ndi Chimwemwe

1Tsopano popeza tayesedwa olungama mwa chikhulupiriro, tili ndi mtendere ndi Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. 2Iyeyo ndiye amene anatsekulira njira mwachikhulupiriro yolowera mʼchisomo mʼmene takhazikikamo. Ndipo tikukondwerera chiyembekezo cha ulemerero wa Mulungu. 3Koma si pokhapo ayi, koma ife tikukondweranso mʼmasautso athu chifukwa tikudziwa kuti masautso amatiphunzitsa kupirira. 4Ndipo kupirira kumabweretsa makhalidwe, makhalidwe amabweretsa chiyembekezo. 5Ndipo chiyembekezo chimenechi sichitikhumudwitsa chifukwa Mulungu mwa Mzimu Woyera, amene Iye anatipatsa, wadzaza mʼmitima mwathu ndi chikondi chake.

6Pakuti pa nthawi yake, tikanali ochimwa, Khristu anatifera anthu osapembedzafe. 7Sizichitika kawirikawiri kuti munthu wina afere munthu wolungama, ngakhale kuti chifukwa cha munthu wabwino wina atha kulimba mtima kumufera. 8Koma Mulungu anaonetsa chikondi chake kwa ife chifukwa pamene tinali ochimwabe, Khristu anatifera.

9Popeza chifukwa cha magazi ake ife tapezeka olungama pamaso pa Mulungu, Iyeyo adzatipulumutsa koposa kotani ku mkwiyo wa Mulungu. 10Pakuti pamene tinali adani a Mulungu, tinayanjanitsidwa ndi Iye kudzera mu imfa ya Mwana wake. Nanga tidzapulumutsidwa bwanji kudzera mʼmoyo wake, titayanjanitsidwa naye? 11Sikuti izi zili chomwechi chabe, koma timakondweranso mwa Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. Kudzera mwa Iye, ife tsopano tayanjanitsidwa ndi Mulungu.

Imfa Kudzera mwa Adamu, Moyo Kudzera mwa Yesu

12Choncho monga momwe tchimo linalowa mʼdziko lapansi kudzera mwa munthu mmodzi, ndi imfa kudzera mu tchimo, mʼnjirayi imfa inafika kwa anthu onse pakuti onse anachimwa. 13Pakuti Malamulo asanaperekedwe, tchimo linali mʼdziko lapansi. Koma pamene palibe Malamulo, tchimo silitengedwa kukhala tchimo. 14Komabe, imfa inalamulira kuyambira nthawi ya Adamu mpaka nthawi ya Mose. Inalamulira ngakhalenso pa iwo amene sanachimwe posamvera Malamulo monga anachitira Adamu. Adamuyo amene anali chifaniziro cha wina amene ankabwera.

15Koma sitingafananitse mphatso yaulereyo ndi kuchimwa kwa anthu. Pakuti ngati anthu ambiri anafa chifukwa cha kuchimwa kwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga chisomo cha Mulungu ndi mphatso zomwe zinabwera ndi chisomo cha munthu mmodzi, Yesu Khristu, ndi kusefukira kwa ambiri! 16Ndiponso, mphatso ya Mulungu sifanana ndi zotsatira za kuchimwa kwa munthu mmodzi. Chiweruzo chinatsatira tchimo la munthu mmodzi ndi kubweretsa kutsutsidwa koma mphatso inatsatira zolakwa zambiri ndi kubweretsa kulungamitsidwa. 17Pakuti ngati, chifukwa cha kulakwa kwa munthu mmodziyo, imfa inalamulira kudzera mwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga kwa iwo amene adzalandira chisomo chochuluka ndi mphatso yachilungamo, adzalamulira mʼmoyo kudzera mwa munthu mmodzi, Yesu Khristu.

18Choncho monga tchimo limodzi linabweretsa kutsutsika pa anthu onse, chimodzimodzinso ntchito imodzi yolungama inabweretsa chilungamo kwa anthu onse ndi kuwapatsa moyo. 19Pakuti kusamvera kwa munthu mmodzi kunasandutsa anthu ambiri kukhala ochimwa, chimodzimodzinso anthu ambiri adzasanduka olungama kudzera mwa munthu mmodzinso.

20Malamulo a Mulungu anaperekedwa ndi cholinga chakuti anthu onse azindikire kuchuluka kwa machimo awo. Koma pamene machimo anachuluka, chisomo chinachuluka koposa. 21Choncho monga momwe tchimo linkalamulira anthu ndi kubweretsa imfa pa iwo, chomwecho kunali koyenera kuti chisomo chilamulire pobweretsa chilungamo kwa anthu, ndi kuwafikitsa ku moyo wosatha mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

Persian Contemporary Bible

رومیان 5:1-21

رابطهٔ جديد با خدا

1پس چون بوسيلهٔ ايمان به عيسی مسيح در نظر خدا پاک و بی‌گناه محسوب شده‌ايم، از رابطهٔ مسالمت‌آميزی با خدا بهره‌مند هستيم. اين رابطه زمانی ايجاد شد كه خداوند ما عيسی مسيح جانش را روی صليب در راه ما فدا كرد. 2به سبب همين ايمان است كه عيسی مسيح ما را در چنين مقام و موقعيت عالی و ممتازی قرار داده است، مقام و موقعيتی كه اكنون نيز در آن قرار داريم؛ و با اطمينان و شادی فراوان، مشتاق هستيم به صورتی درآييم كه خدا برای ما در نظر گرفته است.

3اما نه تنها از اين بابت شاديم، بلكه وقتی با مشكلات زندگی و سختیهای روزگار نيز روبرو می‌شويم، باز خوشحال هستيم زيرا می‌دانيم اين سختیها به خير و صلاح ما هستند چون به ما می‌آموزند كه صبر و تحمل داشته باشيم. 4صبر و تحمل نيز باعث رشد و استحكام شخصيت ما می‌شود و به ما ياری می‌كند تا ايمانمان به خدا روز‌به‌روز قویتر گردد. چنين ايمانی سرانجام اميد ما را نيز نيرومند و پايدار می‌سازد، 5تا بتوانيم در برابر هر مشكلی بايستيم و اطمينان داشته باشيم كه هر پيش آمدی به خير و صلاح ماست، زيرا می‌دانيم كه خدا چقدر نسبت به ما مهربان است. ما اين محبت گرم او را در سراسر وجود خود احساس می‌كنيم، زيرا او روح‌القدس را به ما عطا فرموده تا دلهای ما را از عشق و محبتش لبريز سازد.

6پس ملاحظه می‌كنيد كه در آن هنگام كه ما درمانده و ذليل بوديم، درست در زمان مناسب، مسيح آمد و در راه ما گناهكاران جان خود را فدا كرد! 7حتی اگر ما انسانهايی خوب و پرهيزگار می‌بوديم، كمتر كسی ممكن بود حاضر شود جانش را در راه ما فدا كند، هر چند ممكن است كسی پيدا شود كه بخواهد در راه يک انسان خوب و نجيب جانش را فدا كند. 8اما ببينيد خدا چقدر ما را دوست داشت كه با وجود اينكه گناهكار بوديم، مسيح را فرستاد تا در راه ما فدا شود. 9اگر آن زمان كه گناهكار بوديم، مسيح با ريختن خون خود اين فداكاری را در حق ما كرد، حالا كه خدا ما را بی‌گناه به حساب آورده، چه كارهای بزرگتری برای ما انجام خواهد داد و ما را از خشم و غضب آيندهٔ خدا رهايی خواهد بخشيد. 10هنگامی كه دشمنان خدا بوديم، او بوسيلهٔ مرگ فرزندش ما را با خود آشتی داد؛ پس اكنون كه دوستان خدا شده‌ايم و عيسی مسيح هم در قلب ما زندگی می‌كند، چه بركات عالی و پرشكوهی به ما عطا خواهد كرد.

11حال، چقدر از رابطهٔ عالی و جديدی كه با خدا داريم، شاديم! اينها همه از بركت وجود خداوند ما عيسی مسيح است كه در راه گناهكاران، جان خود را فدا كرد تا ما را دوستان خدا سازد.

گناه حضرت آدم و بخشش عيسی مسيح

12وقتی آدم گناه كرد، گناه او تمام نسل بشر را آلوده ساخت و باعث شيوع مرگ در سراسر جهان شد. در نتيجه، همه چيز دچار فرسودگی و تباهی گشت، چون انسانها همه گناه كردند. 13(يقين داريم كه گناه آدم تمام اين مسايل را بوجود آورد، زيرا اگرچه مردم از زمان آدم تا موسی گناه می‌كردند، اما خدا در آن زمان ايشان را به سبب زير پا گذاشتن احكام خود محكوم نمی‌كرد، چون هنوز احكام و دستورات خود را به ايشان عطا نكرده بود. 14با وجود اين، آنها نيز همه مردند، اما نه به همان علتی كه آدم مرد، زيرا ايشان مانند او از ميوهٔ درخت ممنوع نخورده بودند.)

چه تفاوت بزرگی است ميان آدم و مسيح موعود كه می‌بايست ظهور كند! 15و چه فرق بزرگی است ميان گناه آدم و بخشش خدا!

آدم با گناه خود، باعث مرگ عدهٔ بسياری شد؛ اما عيسی مسيح از روی لطف خدا، سبب بخشش گناهان بسياری گشت. 16يک گناه آدم موجب شد كه عدهٔ بسياری محكوم به مرگ گردند، در حالی كه مسيح گناهان بسياری را به رايگان پاک می‌كند و باعث می‌شود خدا ايشان را «بی‌گناه» بشناسد. 17در نتيجهٔ گناه يک انسان يعنی آدم، مرگ و نابودی همه چيز را در چنگال خود گرفت؛ اما تمام كسانی كه هديهٔ خدا يعنی آمرزش و پاكی كامل از گناه را می‌پذيرند، از آن پس شريک حيات و سلطنت يک انسان ديگر يعنی عيسی مسيح می‌گردند. 18بلی، گناه آدم برای همه محكوميت به همراه آورد، ولی عمل شايسته و مقدسی كه مسيح انجام داد، همه را از محكوميت رهايی می‌دهد و به ايشان زندگی می‌بخشد. 19آدم باعث شد كه عدهٔ زيادی گناهكار شوند، اما مسيح باعث شد كه خدا بسياری را «بی‌گناه» به حساب آورد، زيرا از خدا اطاعت كرد و بر روی صليب كشته شد.

20پس ده فرمان موسی چه نقشی در نجات انسان از گناه دارد؟ ده فرمان به اين دليل عطا شد تا بر تمام مردم مسلم شود كه تا چه حد احكام خدا را زير پا گذاشته‌اند. اما هر چه بيشتر به طبيعت گناهكار خود پی می‌بريم، بيشتر لطف و بخشش بی‌پايان خدا را درک می‌كنيم. 21قبلاً گناه بر انسان حكومت می‌كرد و باعث مرگ می‌شد، اما اكنون لطف و مهربانی خدا حكومت می‌كند تا نه تنها ما را در نظر او شايسته سازد، بلكه بوسيلهٔ خداوند ما عيسی مسيح، ما را به زندگی جاويد برساند.