Aroma 5 – CCL & NUB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 5:1-21

Mtendere ndi Chimwemwe

1Tsopano popeza tayesedwa olungama mwa chikhulupiriro, tili ndi mtendere ndi Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. 2Iyeyo ndiye amene anatsekulira njira mwachikhulupiriro yolowera mʼchisomo mʼmene takhazikikamo. Ndipo tikukondwerera chiyembekezo cha ulemerero wa Mulungu. 3Koma si pokhapo ayi, koma ife tikukondweranso mʼmasautso athu chifukwa tikudziwa kuti masautso amatiphunzitsa kupirira. 4Ndipo kupirira kumabweretsa makhalidwe, makhalidwe amabweretsa chiyembekezo. 5Ndipo chiyembekezo chimenechi sichitikhumudwitsa chifukwa Mulungu mwa Mzimu Woyera, amene Iye anatipatsa, wadzaza mʼmitima mwathu ndi chikondi chake.

6Pakuti pa nthawi yake, tikanali ochimwa, Khristu anatifera anthu osapembedzafe. 7Sizichitika kawirikawiri kuti munthu wina afere munthu wolungama, ngakhale kuti chifukwa cha munthu wabwino wina atha kulimba mtima kumufera. 8Koma Mulungu anaonetsa chikondi chake kwa ife chifukwa pamene tinali ochimwabe, Khristu anatifera.

9Popeza chifukwa cha magazi ake ife tapezeka olungama pamaso pa Mulungu, Iyeyo adzatipulumutsa koposa kotani ku mkwiyo wa Mulungu. 10Pakuti pamene tinali adani a Mulungu, tinayanjanitsidwa ndi Iye kudzera mu imfa ya Mwana wake. Nanga tidzapulumutsidwa bwanji kudzera mʼmoyo wake, titayanjanitsidwa naye? 11Sikuti izi zili chomwechi chabe, koma timakondweranso mwa Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. Kudzera mwa Iye, ife tsopano tayanjanitsidwa ndi Mulungu.

Imfa Kudzera mwa Adamu, Moyo Kudzera mwa Yesu

12Choncho monga momwe tchimo linalowa mʼdziko lapansi kudzera mwa munthu mmodzi, ndi imfa kudzera mu tchimo, mʼnjirayi imfa inafika kwa anthu onse pakuti onse anachimwa. 13Pakuti Malamulo asanaperekedwe, tchimo linali mʼdziko lapansi. Koma pamene palibe Malamulo, tchimo silitengedwa kukhala tchimo. 14Komabe, imfa inalamulira kuyambira nthawi ya Adamu mpaka nthawi ya Mose. Inalamulira ngakhalenso pa iwo amene sanachimwe posamvera Malamulo monga anachitira Adamu. Adamuyo amene anali chifaniziro cha wina amene ankabwera.

15Koma sitingafananitse mphatso yaulereyo ndi kuchimwa kwa anthu. Pakuti ngati anthu ambiri anafa chifukwa cha kuchimwa kwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga chisomo cha Mulungu ndi mphatso zomwe zinabwera ndi chisomo cha munthu mmodzi, Yesu Khristu, ndi kusefukira kwa ambiri! 16Ndiponso, mphatso ya Mulungu sifanana ndi zotsatira za kuchimwa kwa munthu mmodzi. Chiweruzo chinatsatira tchimo la munthu mmodzi ndi kubweretsa kutsutsidwa koma mphatso inatsatira zolakwa zambiri ndi kubweretsa kulungamitsidwa. 17Pakuti ngati, chifukwa cha kulakwa kwa munthu mmodziyo, imfa inalamulira kudzera mwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga kwa iwo amene adzalandira chisomo chochuluka ndi mphatso yachilungamo, adzalamulira mʼmoyo kudzera mwa munthu mmodzi, Yesu Khristu.

18Choncho monga tchimo limodzi linabweretsa kutsutsika pa anthu onse, chimodzimodzinso ntchito imodzi yolungama inabweretsa chilungamo kwa anthu onse ndi kuwapatsa moyo. 19Pakuti kusamvera kwa munthu mmodzi kunasandutsa anthu ambiri kukhala ochimwa, chimodzimodzinso anthu ambiri adzasanduka olungama kudzera mwa munthu mmodzinso.

20Malamulo a Mulungu anaperekedwa ndi cholinga chakuti anthu onse azindikire kuchuluka kwa machimo awo. Koma pamene machimo anachuluka, chisomo chinachuluka koposa. 21Choncho monga momwe tchimo linkalamulira anthu ndi kubweretsa imfa pa iwo, chomwecho kunali koyenera kuti chisomo chilamulire pobweretsa chilungamo kwa anthu, ndi kuwafikitsa ku moyo wosatha mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

Swedish Contemporary Bible

Romarbrevet 5:1-21

Räddade genom tron på Jesus Kristus

1När vi nu har blivit rättfärdiga inför Gud genom att tro, har vi frid med Gud genom vår Herre Jesus Kristus. 2På grund av tron på honom har vi fått tillträde till den nåd vi nu befinner oss i. Stolta och glada kan vi se fram emot Guds härlighet.

3Men inte bara det, vi är också stolta över våra lidanden, eftersom vi vet att lidandet gör oss uthålliga. 4Och uthålligheten ger fasthet och fastheten hopp. 5Och hoppet gör oss inte besvikna, för Gud har ingjutit sin kärlek i våra hjärtan genom den heliga Anden som han har gett oss.

6Medan vi fortfarande var svaga, dog Kristus vid rätt tidpunkt för de ogudaktiga. 7Annars är det väl knappt någon som skulle offra sitt liv ens för en rättfärdig – möjligen skulle någon kunna dö för en som är alltigenom god. 8Men Gud bevisade hur mycket han älskade oss genom att Kristus dog för oss medan vi fortfarande var syndare. 9När vi nu har blivit rättfärdiga genom hans blod, kan vi vara helt säkra på att han också ska rädda oss från vreden. 10Om vi då var Guds fiender men blev försonade med honom genom hans Sons död, så kan vi därför, när vi nu är försonade, också vara säkra på att vi blir räddade genom hans liv.

11Men inte nog med det, vi är stolta i Gud genom vår Herre Jesus Kristus, genom vilken vi har fått försoningen.

Adam och Kristus

12Genom en enda människa, Adam, kom synden in i världen, och genom synden döden, och så dör alla människor, eftersom alla har syndat. 13Synden fanns i världen före lagen men räknas inte när det inte finns någon lag. 14Döden härskade dock över alla människor som levde i tidsperioden mellan Adam och Mose, även över dem som inte hade syndat genom en överträdelse som Adam, han som var en förebild för honom som skulle komma. 15Men det är inte på samma sätt med nåden som med överträdelsen. För om många måste dö för en enda människas överträdelse, så är Guds nåd och nådegåvan genom en enda människa, Jesus Kristus, oändligt mycket större för många.

16Det är också stor skillnad mellan följderna av denne ende mans synd och Guds gåva. En enda mans synd ledde till en fällande dom, medan gåvan som följde efter mångas överträdelser ledde till frikännande. 17Om nämligen en enda människas överträdelse gjorde så att döden fick makten genom denne ende, så ska nu de som får den överflödande nåden och rättfärdighetens gåva i ännu högre grad få liv och makt genom en enda, Jesus Kristus.

18Om alltså en endas överträdelse ledde till en fällande dom för alla människor, har också en endas rättfärdiga handling lett till rättfärdighet och liv för alla. 19Genom att en enda människa var olydig blev alla syndare, men på samma sätt ska alla genom en enda människas lydnad bli rättfärdiga.

20Lagen kom in för att överträdelsen skulle bli större. Men där synden blev större, där ökade nåden desto mer, 21för att, så som synden härskade och förde till döden, så skulle nu nåden härska genom rättfärdigheten och genom Jesus Kristus, vår Herre, leda till evigt liv.