Aroma 5 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 5:1-21

Mtendere ndi Chimwemwe

1Tsopano popeza tayesedwa olungama mwa chikhulupiriro, tili ndi mtendere ndi Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. 2Iyeyo ndiye amene anatsekulira njira mwachikhulupiriro yolowera mʼchisomo mʼmene takhazikikamo. Ndipo tikukondwerera chiyembekezo cha ulemerero wa Mulungu. 3Koma si pokhapo ayi, koma ife tikukondweranso mʼmasautso athu chifukwa tikudziwa kuti masautso amatiphunzitsa kupirira. 4Ndipo kupirira kumabweretsa makhalidwe, makhalidwe amabweretsa chiyembekezo. 5Ndipo chiyembekezo chimenechi sichitikhumudwitsa chifukwa Mulungu mwa Mzimu Woyera, amene Iye anatipatsa, wadzaza mʼmitima mwathu ndi chikondi chake.

6Pakuti pa nthawi yake, tikanali ochimwa, Khristu anatifera anthu osapembedzafe. 7Sizichitika kawirikawiri kuti munthu wina afere munthu wolungama, ngakhale kuti chifukwa cha munthu wabwino wina atha kulimba mtima kumufera. 8Koma Mulungu anaonetsa chikondi chake kwa ife chifukwa pamene tinali ochimwabe, Khristu anatifera.

9Popeza chifukwa cha magazi ake ife tapezeka olungama pamaso pa Mulungu, Iyeyo adzatipulumutsa koposa kotani ku mkwiyo wa Mulungu. 10Pakuti pamene tinali adani a Mulungu, tinayanjanitsidwa ndi Iye kudzera mu imfa ya Mwana wake. Nanga tidzapulumutsidwa bwanji kudzera mʼmoyo wake, titayanjanitsidwa naye? 11Sikuti izi zili chomwechi chabe, koma timakondweranso mwa Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. Kudzera mwa Iye, ife tsopano tayanjanitsidwa ndi Mulungu.

Imfa Kudzera mwa Adamu, Moyo Kudzera mwa Yesu

12Choncho monga momwe tchimo linalowa mʼdziko lapansi kudzera mwa munthu mmodzi, ndi imfa kudzera mu tchimo, mʼnjirayi imfa inafika kwa anthu onse pakuti onse anachimwa. 13Pakuti Malamulo asanaperekedwe, tchimo linali mʼdziko lapansi. Koma pamene palibe Malamulo, tchimo silitengedwa kukhala tchimo. 14Komabe, imfa inalamulira kuyambira nthawi ya Adamu mpaka nthawi ya Mose. Inalamulira ngakhalenso pa iwo amene sanachimwe posamvera Malamulo monga anachitira Adamu. Adamuyo amene anali chifaniziro cha wina amene ankabwera.

15Koma sitingafananitse mphatso yaulereyo ndi kuchimwa kwa anthu. Pakuti ngati anthu ambiri anafa chifukwa cha kuchimwa kwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga chisomo cha Mulungu ndi mphatso zomwe zinabwera ndi chisomo cha munthu mmodzi, Yesu Khristu, ndi kusefukira kwa ambiri! 16Ndiponso, mphatso ya Mulungu sifanana ndi zotsatira za kuchimwa kwa munthu mmodzi. Chiweruzo chinatsatira tchimo la munthu mmodzi ndi kubweretsa kutsutsidwa koma mphatso inatsatira zolakwa zambiri ndi kubweretsa kulungamitsidwa. 17Pakuti ngati, chifukwa cha kulakwa kwa munthu mmodziyo, imfa inalamulira kudzera mwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga kwa iwo amene adzalandira chisomo chochuluka ndi mphatso yachilungamo, adzalamulira mʼmoyo kudzera mwa munthu mmodzi, Yesu Khristu.

18Choncho monga tchimo limodzi linabweretsa kutsutsika pa anthu onse, chimodzimodzinso ntchito imodzi yolungama inabweretsa chilungamo kwa anthu onse ndi kuwapatsa moyo. 19Pakuti kusamvera kwa munthu mmodzi kunasandutsa anthu ambiri kukhala ochimwa, chimodzimodzinso anthu ambiri adzasanduka olungama kudzera mwa munthu mmodzinso.

20Malamulo a Mulungu anaperekedwa ndi cholinga chakuti anthu onse azindikire kuchuluka kwa machimo awo. Koma pamene machimo anachuluka, chisomo chinachuluka koposa. 21Choncho monga momwe tchimo linkalamulira anthu ndi kubweretsa imfa pa iwo, chomwecho kunali koyenera kuti chisomo chilamulire pobweretsa chilungamo kwa anthu, ndi kuwafikitsa ku moyo wosatha mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

Bibelen på hverdagsdansk

Romerbrevet 5:1-21

Forsoning og fred med Gud

1Vi blev altså accepteret af Gud, da vi kom til tro på Jesus Kristus, vores Herre. Derfor er vi nu forsonet med Gud og har fået fred i hjertet. 2Det er også Jesus, der gennem vores tro har ført os ind i den nåde, vi nu lever i, og vi ser med glæde frem til, at vi engang skal få del i al Guds herlighed. 3Men ikke bare det. Vi glæder os endda over at blive forfulgt, for vi ved, at forfølgelserne styrker vores udholdenhed. 4Udholdenheden giver os karakterstyrke, og karakterstyrken giver os en stærk forventning om at få del i Guds herlighed engang. 5Og vi bliver ikke skuffet i vores forventning, for Gud har givet os Helligåndens kraft og fyldt vores hjerter med sin kærlighed.

6Mens vi endnu var magtesløse og ugudelige, kom Kristus i rette tid og ofrede sit liv for at redde os. 7Der er ikke mange, der vil ofre livet for at redde et medmenneske! Jo, måske hvis det er et usædvanlig godt menneske. 8Men Gud viser sin kærlighed mod os, ved at Kristus ofrede sit liv for os, mens vi stadig var syndere, 9og han har nu accepteret os på grund af Kristi stedfortrædende død. Derfor kan vi trygt regne med, at når Kristus ved sin død forsonede os med Gud, vil han også redde os på dommens dag. 10Selvom vi var fjender af Gud, blev vi alligevel forsonet med ham, fordi hans Søn døde for os. Nu, da vi er blevet Guds venner, kan vi være forvissede om, at vi vil få det evige liv, fordi Jesus lever. 11Altså er det en utrolig glæde for os, at vi er blevet forsonet med Gud gennem Jesus Kristus, vores Herre.

Adam og Kristus som modsætninger

12Det første menneske, Adam, bragte synden ind i verden, og synden førte døden med sig. Sådan fik døden magt over alle mennesker, fordi alle syndede. 13Synden var i verden, inden loven kom, men den kunne ikke udpeges, så længe der ingen lov var. 14Døden herskede derfor også i verden, før loven kom, det vil sige fra Adam til Moses. Selv de, der ikke var ulydige mod Gud på samme direkte måde som Adam, måtte dø.

Adam kan sammenlignes med Jesus i den forstand, 15-16at ét menneskes handling har fået konsekvenser for hele menneskeheden. Men hvor ét menneskes ulydighed førte til død for et utal af mennesker, bragte ét andet menneskes lydighed Guds vældige kærlighed og nåde ud til et utal af mennesker. Efter at ét menneske havde forsyndet sig, måtte Gud afsige dommen over os mennesker og erklære os skyldige. Men efter at mange mennesker havde forsyndet sig, gav Jesus Kristus frivilligt sit liv for os, og derved kunne Gud erklære os skyldfri. 17Det var ét menneskes synd, som førte til, at døden fik herredømmet over menneskene. Men det var ét menneskes gave, som fører til, at livet får herredømmet over alle, som tager imod Guds overstrømmende nåde og tilgivelse i Jesus Kristus.

18Det vil altså sige, at ét menneskes forkerte handling førte til fordømmelse og død for alle mennesker. Men det var også ét menneskes rigtige handling, der førte til frikendelse og liv for alle mennesker. 19Ét menneskes ulydighed førte til, at mange andre gjorde oprør mod Gud. Men det er også ét menneskes lydighed, der fører til, at mange andre ønsker at gøre Guds vilje.

20Da loven kom til, voksede synden. Men da synden blev større, blev Guds nåde endnu større. 21Før havde synden herredømmet, og det førte til død. Men hos dem, som har opnået Guds tilgivelse, er det nåden, som har herredømmet, og det fører til det evige liv ved Jesus Kristus, vores Herre.