Aroma 3 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 3:1-31

Kukhulupirika kwa Mulungu

1Nanga kodi pali ubwino wotani pokhala Myuda, kapena muli ubwino wanjinso mu mdulidwe? 2Ubwino wake ndi wambiri mʼnjira zonse! Choyambirira iwo anapatsidwa Mawu a Mulungu kuti awasunge.

3Nanga zili bwanji ngati ena analibe chikhulupiriro? Kodi kupanda chikhulupiriro kwawo kukanalepheretsa kukhulupirika kwa Mulungu? 4Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Mulungu akhale woona, ndi munthu aliyense akhale wonama. Monga kwalembedwa kuti,

“Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula

ndi kupambana pamene muweruza.”

5Koma ngati kuyipa mtima kwathu kuonetsa poyera kuti Mulungu ndi wolungama, ife tinganene chiyani? Kodi tinganene kuti Mulungu ndi wosalungama pamene aonetsa mkwiyo wake pa ife? (Ine ndikuyankhula monga mmene anthu ena amayankhulira). 6Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ngati zikanakhala zotero, kodi Mulungu akanaweruza bwanji dziko lapansi? 7Wina atanena kuti, “Ngati kunama kwanga kukuonetsa koposa kuti Mulungu ndi woona, ndi kuwonjezera pa ulemerero wake, nanga nʼchifukwa chiyani ndikuweruzidwa kuti ndine wochimwa?” 8Nʼchifukwa chiyani osanena kuti, monga ena amanena mosasamala kuti, “Tiyeni tichite zoyipa kuti zabwino zionekere?” Anthu onena zoterewa kulangidwa kwawo ndi koyenera.

Palibe Munthu Wolungama

9Kodi timalize bwanji? Kodi Ayuda ndife oposa anthu ena? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ife tinanena kale kuti Ayuda ndi a mitundu ina omwe ndi ochimwa. 10Monga kwalembedwa kuti,

“Palibe munthu wolungama, inde palibe ndi mmodzi yemwe.

11Palibe ndi mmodzi yemwe amene amazindikira,

palibe amene amafunafuna Mulungu.

12Onse apatukira kumbali,

onse pamodzi asanduka opandapake.

Palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita zabwino,

palibe ngakhale mmodzi.”

13“Kummero kwawo kuli ngati manda apululu;

ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.”

“Ululu wa mamba uli pa milomo yawo.”

14“Mʼkamwa mwawo ndi modzaza ndi zotemberera ndi mawu owawa.”

15“Mapazi awo afulumira kukakhetsa magazi.

16Kusakaza ndi chisoni kumaonekera mʼnjira zawo,

17ndipo njira ya mtendere sayidziwa.”

18“Saopa Mulungu ndi pangʼono pomwe.”

19Tsopano tikudziwa kuti chilichonse Malamulo amanena, amanena kwa amene amalamulidwa ndi Malamulowo, ndi cholinga chakuti aliyense asowe chonena, ndipo dziko lonse lidzayimbidwa mlandu ndi Mulungu. 20Chifukwa chake palibe mmodzi amene adzayesedwa wolungama pamaso pake chifukwa chosunga Malamulo, kuti ife timazindikira tchimo kupyolera mu Malamulo.

Kulungama Mwachikhulupiriro

21Koma tsopano chilungamo chochokera kwa Mulungu, osati chochokera ku Malamulo, chaonetsedwa. Ichi ndi chimene Malamulo ndi Aneneri amachitira umboni. 22Timakhala olungama pamaso pa Mulungu pamene takhulupirira Yesu Khristu. Mulungu amachitira zimenezi anthu onse amene akhulupirira Khristu. Palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi a mitundu ina, 23pakuti onse anachimwa naperewera pa ulemerero wa Mulungu 24ndipo onse alungamitsidwa mwaulere mwa chisomo chake chifukwa cha Khristu Yesu amene anawawombola. 25Mulungu anamupereka Iyeyu kuti pokhetsa magazi ake, akhale nsembe yokhululukira machimo. Mulungu anachita zimenezi kufuna kuonetsa chilungamo chake. Chifukwa cha kuleza mtima kwake, sanalange anthu chifukwa cha machimo amene anachita kale. 26Iye anachita izi kuti aonetse chilungamo chake lero lino. Anthu azindikire kuti Iye ndi wolungama ndipo amalungamitsa aliyense amene akhulupirira Yesu.

27Nanga tsono pamenepa munthu anganyadenso? Kunyadatu kwachotsedwa. Chifukwa cha Malamulo? Kodi Malamulo samafuna ntchito za munthu? Ayi, koma mwachikhulupiriro. 28Ife tikunenabe kuti munthu amalungamitsidwa mwachikhulupiriro osati mwakusunga Malamulo. 29Kodi Mulungu ndi Mulungu wa Ayuda okha? Kodi si Mulungu wa a mitundu inanso? Inde wa a mitundu inanso, 30popeza ndi Mulungu mmodzi yemweyo amene adzalungamitsa mwachikhulupiriro ochita mdulidwe ndi osachita mdulidwe kudzera mʼchikhulupiriro chomwecho. 31Kodi tsono ife, tikutaya Malamulo pamene tikunena kuti pafunika chikhulupiriro? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Komatu ife tikukwaniritsadi Malamulo.

Slovo na cestu

Římanům 3:1-31

Bůh zůstává věrný

1Přece však má židovský národ zvláštní postavení a určité výsady. Jaké? Není jich málo! 2Předně jim byla svěřena Boží slova.

3A co když jim někteří neuvěřili – můžete namítnout. A já se ptám: Myslíte, že Bůh jen pro jejich nedůvěru nedostojí svému slovu? 4Ale kdepak! Právě na tom ukáže, jak dovede být věrný i tehdy, když mu člověk nevěří. Tak to stojí i v Písmu:

„Každý uzná, že čestně dodržíš to,

co jsi slíbil, a jako vítěz vyjdeš z každého obvinění.“

5Někdo však může namítnout: „Jestliže naše špatnost dává vyniknout Boží spravedlnosti, snad by nás Bůh neměl za ni trestat.“ 6Jaký smysl by potom měl Boží soud? 7To bychom mohli rovnou nabádat ke zlu, aby se dobro vedle něj tím víc zaskvělo. 8Někteří lidé to opravdu dělají, ale my ne, i když nás z toho obviňují. Takoví hříšníci budou plným právem odsouzeni. 9Napsal jsem vám již, že židovský národ má určité přednosti. To však neznamená, že židé jsou před Bohem lepší než ostatní. O všech lidech je v Žalmech napsáno:

10„Nikdo na světě není spravedlivý, ani jediný.

11Nikdo není moudrý, nikdo Boha nehledá.

12Všichni úplně zabloudili, jejich život ztratil smysl.

Opuštěná je cesta dobra, nikdo po ní nekráčí.

13-14Jejich hrdlo – otevřený hrob;

jazyk – nástroj lsti a podvodu;

rty – schránky jedu,

uštknou tě jako had.

15K prolití krve je nemusíš pobízet,

16zkáza a bída jsou jejich průvodci,

17cestu k pokoji však neznají,

18ani úctu před Bohem.“

19Víme však, že ustanovení zákona jsou závazná pro všechny, kterým byla určena. Každý tu musí uznat, že před Bohem je vinen, 20neboť sebeupřímnější snahou dodržovat zákon si nikdo před Bohem nedobude postavení bezúhonného; zákon naši vinu pouze blíže určuje a usvědčuje nás z ní.

Spravedlnost před Bohem

21Dnes však už známe jinou cestu k věčnému životu než spoléhání se na vlastní dodržování Božích zákonů. Už Mojžíš a proroci o ní mluvili, 22-23ale teprve Kristem ji Bůh otevřel. On sám, jak odpovídá jeho povaze, rozhodl se dát novou příležitost lidem, kteří svými vinami ztratili podíl na Boží slávě: odevzdat život do všech důsledků Kristu.

24Jaká to milost, že nic jiného není člověku zapotřebí. Kristus – toť svrchovaný důkaz Boží shovívavosti k nám. 25-26Jeho krev prolitá na popravišti je pečetí smíření Boha se světem. Až dosud Bůh trest za naše viny pouze s nekonečnou trpělivostí odkládal; nyní je však vložil na Ježíše Krista, který pro ně zemřel. A tak jsou nám definitivně odpuštěny; odpuštěny všem, kdo tuto Boží nabídku smíření přijali. Tak Bůh z hříšných dělá opět bezúhonné, aniž sám cokoliv slevuje ze své spravedlnosti.

27Čím se tedy můžeme před Bohem chlubit? Ničím! Skutky? Ty nás nespasí. Jedině víra nás může zachránit. 28Jsem přesvědčen, že nikoliv úzkostlivé dodržování všech přikázání a předpisů, ale pouze víra nás uschopní obstát před Bohem. 29Což je tu Bůh jen pro členy církve? Není snad Bohem všech lidí? To se rozumí, že je! 30Bůh je pouze jeden a bez rozdílu přijímá všechny, kdo se obrátí ke Kristu.

31Neprohlašujeme snad zákon za bezcenný tím, že stavíme víru tak vysoko? Rozhodně ne! Naopak, platnost zákona se tím jen potvrzuje.