Aroma 3 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 3:1-31

Kukhulupirika kwa Mulungu

1Nanga kodi pali ubwino wotani pokhala Myuda, kapena muli ubwino wanjinso mu mdulidwe? 2Ubwino wake ndi wambiri mʼnjira zonse! Choyambirira iwo anapatsidwa Mawu a Mulungu kuti awasunge.

3Nanga zili bwanji ngati ena analibe chikhulupiriro? Kodi kupanda chikhulupiriro kwawo kukanalepheretsa kukhulupirika kwa Mulungu? 4Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Mulungu akhale woona, ndi munthu aliyense akhale wonama. Monga kwalembedwa kuti,

“Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula

ndi kupambana pamene muweruza.”

5Koma ngati kuyipa mtima kwathu kuonetsa poyera kuti Mulungu ndi wolungama, ife tinganene chiyani? Kodi tinganene kuti Mulungu ndi wosalungama pamene aonetsa mkwiyo wake pa ife? (Ine ndikuyankhula monga mmene anthu ena amayankhulira). 6Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ngati zikanakhala zotero, kodi Mulungu akanaweruza bwanji dziko lapansi? 7Wina atanena kuti, “Ngati kunama kwanga kukuonetsa koposa kuti Mulungu ndi woona, ndi kuwonjezera pa ulemerero wake, nanga nʼchifukwa chiyani ndikuweruzidwa kuti ndine wochimwa?” 8Nʼchifukwa chiyani osanena kuti, monga ena amanena mosasamala kuti, “Tiyeni tichite zoyipa kuti zabwino zionekere?” Anthu onena zoterewa kulangidwa kwawo ndi koyenera.

Palibe Munthu Wolungama

9Kodi timalize bwanji? Kodi Ayuda ndife oposa anthu ena? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ife tinanena kale kuti Ayuda ndi a mitundu ina omwe ndi ochimwa. 10Monga kwalembedwa kuti,

“Palibe munthu wolungama, inde palibe ndi mmodzi yemwe.

11Palibe ndi mmodzi yemwe amene amazindikira,

palibe amene amafunafuna Mulungu.

12Onse apatukira kumbali,

onse pamodzi asanduka opandapake.

Palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita zabwino,

palibe ngakhale mmodzi.”

13“Kummero kwawo kuli ngati manda apululu;

ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.”

“Ululu wa mamba uli pa milomo yawo.”

14“Mʼkamwa mwawo ndi modzaza ndi zotemberera ndi mawu owawa.”

15“Mapazi awo afulumira kukakhetsa magazi.

16Kusakaza ndi chisoni kumaonekera mʼnjira zawo,

17ndipo njira ya mtendere sayidziwa.”

18“Saopa Mulungu ndi pangʼono pomwe.”

19Tsopano tikudziwa kuti chilichonse Malamulo amanena, amanena kwa amene amalamulidwa ndi Malamulowo, ndi cholinga chakuti aliyense asowe chonena, ndipo dziko lonse lidzayimbidwa mlandu ndi Mulungu. 20Chifukwa chake palibe mmodzi amene adzayesedwa wolungama pamaso pake chifukwa chosunga Malamulo, kuti ife timazindikira tchimo kupyolera mu Malamulo.

Kulungama Mwachikhulupiriro

21Koma tsopano chilungamo chochokera kwa Mulungu, osati chochokera ku Malamulo, chaonetsedwa. Ichi ndi chimene Malamulo ndi Aneneri amachitira umboni. 22Timakhala olungama pamaso pa Mulungu pamene takhulupirira Yesu Khristu. Mulungu amachitira zimenezi anthu onse amene akhulupirira Khristu. Palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi a mitundu ina, 23pakuti onse anachimwa naperewera pa ulemerero wa Mulungu 24ndipo onse alungamitsidwa mwaulere mwa chisomo chake chifukwa cha Khristu Yesu amene anawawombola. 25Mulungu anamupereka Iyeyu kuti pokhetsa magazi ake, akhale nsembe yokhululukira machimo. Mulungu anachita zimenezi kufuna kuonetsa chilungamo chake. Chifukwa cha kuleza mtima kwake, sanalange anthu chifukwa cha machimo amene anachita kale. 26Iye anachita izi kuti aonetse chilungamo chake lero lino. Anthu azindikire kuti Iye ndi wolungama ndipo amalungamitsa aliyense amene akhulupirira Yesu.

27Nanga tsono pamenepa munthu anganyadenso? Kunyadatu kwachotsedwa. Chifukwa cha Malamulo? Kodi Malamulo samafuna ntchito za munthu? Ayi, koma mwachikhulupiriro. 28Ife tikunenabe kuti munthu amalungamitsidwa mwachikhulupiriro osati mwakusunga Malamulo. 29Kodi Mulungu ndi Mulungu wa Ayuda okha? Kodi si Mulungu wa a mitundu inanso? Inde wa a mitundu inanso, 30popeza ndi Mulungu mmodzi yemweyo amene adzalungamitsa mwachikhulupiriro ochita mdulidwe ndi osachita mdulidwe kudzera mʼchikhulupiriro chomwecho. 31Kodi tsono ife, tikutaya Malamulo pamene tikunena kuti pafunika chikhulupiriro? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Komatu ife tikukwaniritsadi Malamulo.

New Russian Translation

Римлянам 3:1-31

Долг человечества перед Богом

1В чем же тогда преимущество быть иудеем, и есть ли польза в том, чтобы быть в числе обрезанных? 2Большое преимущество во всех отношениях. Прежде всего в том, что иудеям было доверено слово Божье.

3И если некоторые из них оказались неверны Богу, то разве их неверность может уничтожить Божью верность? 4Конечно же нет! Хотя каждый человек лжив, но Бог верен, как об этом и написано:

«Чтобы Ты был оправдан в Твоих словах

и победил в суде Своем»3:4 Пс. 50:6..

5Но если наша неправедность яснее показывает праведность Божью, то значит ли это, что Бог несправедлив в Своем гневе на нас? (Я говорю по человеческому рассуждению.) 6Конечно нет. Иначе как бы Бог мог судить мир? 7Но если моя ложь делает ярче истину Божью и, таким образом, умножает Его славу, то почему же я судим как грешник? 8Может, нам нужно начать делать зло, чтобы вышло добро (а клеветники говорят, что мы так и учим)? Такие люди заслуживают осуждения.

Нет ни одного праведного

9Так что же? В лучшем ли мы, иудеи, положении, чем другие? Нет! Мы уже говорили о том, что как иудеи, так и язычники – все оказались под властью греха. 10Написано:

«Нет праведного, нет ни одного!

11Никто не понимает

и никто не ищет Бога.

12Все сбились с пути, все, как один, стали негодны,

нет делающего добро,

нет ни одного»3:10-12 Пс. 13:1-3; 52:2-4..

13«Гортань их – открытая могила,

языком своим они лгут»3:13 Пс. 5:10..

«У них на губах яд гадюки»3:13 Пс. 139:4..

14«Уста их полны проклятий и горечи»3:14 Пс. 9:28..

15«Их ноги быстры на пролитие крови;

16опустошением и горем отмечен их путь,

17им неизвестен путь к миру»3:15-17 Прит. 1:16; Ис. 59:7-8..

18«Нет Божьего страха у них в глазах»3:18 Пс. 35:2..

19Но мы знаем, что сказанное в Законе, сказано для тех, кто находится под Законом, а значит, абсолютно никто не имеет извинения, и весь мир становится виновным перед Богом. 20Никто не будет оправдан перед Ним соблюдением Закона. Через Закон приходит лишь осознание нашего греха.

Праведность по вере

21Но сейчас, независимо от Закона, Бог открывает людям ту праведность, о которой свидетельствуют Закон и пророки. 22Праведность от Бога дается через веру всем, кто верит в Иисуса Христа, потому что нет различия. 23Ведь все согрешили, и все лишились Божьей славы, 24и все получают оправдание даром, по благодати, через искупление, совершенное Иисусом Христом. 25Бог сделал Его жертвой умилостивления в крови Его для всех, кто верит. Бог пожелал проявить Свою справедливость, простив грехи, совершенные в прежние века. 26Он долго терпел, чтобы сейчас, в наше время, показать Свою праведность. Он Сам праведен и оправдывает того, кто верит в Иисуса.

27Итак, что же с нашей похвальбой? Она исключена. Какой закон это сделал? Закон дел? Нет, закон веры. 28Мы утверждаем, что человек получает оправдание верой независимо от соблюдения Закона. 29Разве Бог является только Богом иудеев? Разве Он не Бог и язычников? Конечно же, и язычников, 30потому что есть только один Бог, Который оправдает как обрезанных, так и необрезанных по их вере. 31Но это вовсе не значит, что мы верой устраняем Закон, наоборот, мы утверждаем его.