Aroma 3 – CCL & NCA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 3:1-31

Kukhulupirika kwa Mulungu

1Nanga kodi pali ubwino wotani pokhala Myuda, kapena muli ubwino wanjinso mu mdulidwe? 2Ubwino wake ndi wambiri mʼnjira zonse! Choyambirira iwo anapatsidwa Mawu a Mulungu kuti awasunge.

3Nanga zili bwanji ngati ena analibe chikhulupiriro? Kodi kupanda chikhulupiriro kwawo kukanalepheretsa kukhulupirika kwa Mulungu? 4Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Mulungu akhale woona, ndi munthu aliyense akhale wonama. Monga kwalembedwa kuti,

“Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula

ndi kupambana pamene muweruza.”

5Koma ngati kuyipa mtima kwathu kuonetsa poyera kuti Mulungu ndi wolungama, ife tinganene chiyani? Kodi tinganene kuti Mulungu ndi wosalungama pamene aonetsa mkwiyo wake pa ife? (Ine ndikuyankhula monga mmene anthu ena amayankhulira). 6Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ngati zikanakhala zotero, kodi Mulungu akanaweruza bwanji dziko lapansi? 7Wina atanena kuti, “Ngati kunama kwanga kukuonetsa koposa kuti Mulungu ndi woona, ndi kuwonjezera pa ulemerero wake, nanga nʼchifukwa chiyani ndikuweruzidwa kuti ndine wochimwa?” 8Nʼchifukwa chiyani osanena kuti, monga ena amanena mosasamala kuti, “Tiyeni tichite zoyipa kuti zabwino zionekere?” Anthu onena zoterewa kulangidwa kwawo ndi koyenera.

Palibe Munthu Wolungama

9Kodi timalize bwanji? Kodi Ayuda ndife oposa anthu ena? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ife tinanena kale kuti Ayuda ndi a mitundu ina omwe ndi ochimwa. 10Monga kwalembedwa kuti,

“Palibe munthu wolungama, inde palibe ndi mmodzi yemwe.

11Palibe ndi mmodzi yemwe amene amazindikira,

palibe amene amafunafuna Mulungu.

12Onse apatukira kumbali,

onse pamodzi asanduka opandapake.

Palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita zabwino,

palibe ngakhale mmodzi.”

13“Kummero kwawo kuli ngati manda apululu;

ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.”

“Ululu wa mamba uli pa milomo yawo.”

14“Mʼkamwa mwawo ndi modzaza ndi zotemberera ndi mawu owawa.”

15“Mapazi awo afulumira kukakhetsa magazi.

16Kusakaza ndi chisoni kumaonekera mʼnjira zawo,

17ndipo njira ya mtendere sayidziwa.”

18“Saopa Mulungu ndi pangʼono pomwe.”

19Tsopano tikudziwa kuti chilichonse Malamulo amanena, amanena kwa amene amalamulidwa ndi Malamulowo, ndi cholinga chakuti aliyense asowe chonena, ndipo dziko lonse lidzayimbidwa mlandu ndi Mulungu. 20Chifukwa chake palibe mmodzi amene adzayesedwa wolungama pamaso pake chifukwa chosunga Malamulo, kuti ife timazindikira tchimo kupyolera mu Malamulo.

Kulungama Mwachikhulupiriro

21Koma tsopano chilungamo chochokera kwa Mulungu, osati chochokera ku Malamulo, chaonetsedwa. Ichi ndi chimene Malamulo ndi Aneneri amachitira umboni. 22Timakhala olungama pamaso pa Mulungu pamene takhulupirira Yesu Khristu. Mulungu amachitira zimenezi anthu onse amene akhulupirira Khristu. Palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi a mitundu ina, 23pakuti onse anachimwa naperewera pa ulemerero wa Mulungu 24ndipo onse alungamitsidwa mwaulere mwa chisomo chake chifukwa cha Khristu Yesu amene anawawombola. 25Mulungu anamupereka Iyeyu kuti pokhetsa magazi ake, akhale nsembe yokhululukira machimo. Mulungu anachita zimenezi kufuna kuonetsa chilungamo chake. Chifukwa cha kuleza mtima kwake, sanalange anthu chifukwa cha machimo amene anachita kale. 26Iye anachita izi kuti aonetse chilungamo chake lero lino. Anthu azindikire kuti Iye ndi wolungama ndipo amalungamitsa aliyense amene akhulupirira Yesu.

27Nanga tsono pamenepa munthu anganyadenso? Kunyadatu kwachotsedwa. Chifukwa cha Malamulo? Kodi Malamulo samafuna ntchito za munthu? Ayi, koma mwachikhulupiriro. 28Ife tikunenabe kuti munthu amalungamitsidwa mwachikhulupiriro osati mwakusunga Malamulo. 29Kodi Mulungu ndi Mulungu wa Ayuda okha? Kodi si Mulungu wa a mitundu inanso? Inde wa a mitundu inanso, 30popeza ndi Mulungu mmodzi yemweyo amene adzalungamitsa mwachikhulupiriro ochita mdulidwe ndi osachita mdulidwe kudzera mʼchikhulupiriro chomwecho. 31Kodi tsono ife, tikutaya Malamulo pamene tikunena kuti pafunika chikhulupiriro? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Komatu ife tikukwaniritsadi Malamulo.

New Chhattisgarhi Translation (नवां नियम छत्तीसगढ़ी)

रोमीमन 3:1-31

परमेसर बिसवासयोग्य अय

1तब यहूदी होय के का फायदा या खतना करवाय के का महत्‍व हवय? 2हर किसम ले बहुंत फायदा हवय। सबले पहिली यहूदीमन ला परमेसर के बचन सऊंपे गीस। 3यदि ओम ले कुछू झन बिसवासघाती निकरिन, त का होईस? का ओमन के बिसवासघाती होय ले परमेसर ह बिसवास के लइक नइं रहय? 4बिलकुल ही नइं! परमेसर ह सच्‍चा अऊ जम्मो मनखेमन लबरा अंय। जइसने कि परमेसर के बचन म लिखे हवय: “ताकि तेंह अपन बात म सही साबित हो जा, अऊ तोर नियाय म, तोला जीत मिलय।”3:4 भजन-संहिता 51:4

5पर यदि हमर अधरम ह परमेसर के धरमीपन ला जादा साफ-साफ देखाथे, त हमन का कहन? का ए कहन, कि परमेसर ह हमर ऊपर कोरोध करके अनियाय करथे? (मेंह एला मनखे के सोच के मुताबिक कहत हंव।) 6बिलकुल ही नइं! यदि परमेसर ह अनियायी होतिस, त ओह संसार के नियाय कइसने कर सकही? 7यदि मोर लबारी के कारन परमेसर के सच्‍चई अऊ महिमा ह बढ़थे, त फेर मेंह काबर एक पापी के सहीं दोसी ठहिराय जावत हंव? 8“तब आवव, हमन बुरई करन कि भलई होवय” – जइसने कि कुछू मनखेमन हमर ऊपर दोस लगाके कहिथें कि हमन अइसने कहिथन। अइसने मनखेमन ला दोसी ठहिराय जाना उचित अय।

कोनो मनखे धरमी नो हंय

9त फेर हमन का कहन? का हम यहूदीमन आने मन ले बने हवन? बिलकुल नइं! काबरकि हमन पहिली ए दोस लगा चुके हवन कि यहूदी अऊ आनजात जम्मो मनखे मन पाप के अधीन हवंय। 10जइसने कि परमेसर के बचन म लिखे हवय:

“कोनो धरमी नो हंय, एको झन घलो नइं।

11कोनो नइं समझंय, कोनो परमेसर के खोज नइं करंय।

12जम्मो झन भटक गे हवंय

अऊ एक संग ओमन बेकार हो गे हवंय।

कोनो भलई नइं करंय,

एको झन घलो नइं।”3:12 भजन-संहिता 14:1-3; 53:1-3; सभो 7:20

13“ओमन के टोंटा ह खुले कबर अय,

ओमन के जीभ ह छल कपट के बात करथे।”3:13 भजन-संहिता 5:9

“ओमन के होंठ म करैत सांप के जहर हवय।”3:13 भजन-संहिता 140:3

14“ओमन के मुहूं ह सराप अऊ करूपन ले भरे हवय।”

15“ओमन के गोड़ ह लहू बोहाय बर तेज भागथे,

16ओमन के डहार म नास अऊ दुरगती हवय,

17अऊ ओमन सांति के रसता ला नइं जानंय।”3:17 यसायाह 59:7-8

18“ओमन के आंखी के आघू म परमेसर के डर नइं अय।”3:18 भजन-संहिता 36:1

19हमन जानत हवन कि मूसा के कानून ह जऊन कुछू कहिथे, ओह ओमन ला कहिथे जऊन मन कानून के अधीन हवंय, ताकि हर एक के मुहूं ह बंद हो जावय अऊ जम्मो संसार ह परमेसर के दंड के अधीन रहय। 20एकरसेति मूसा के कानून ला माने के दुवारा कोनो परमेसर के नजर म धरमी नइं ठहिरंय, पर कानून के जरिये मनखे ह पाप के पहिचान करथे।

बिसवास के दुवारा धरमीपन

21पर अब परमेसर ह परगट करे हवय कि मनखेमन ओकर नजर म बिगर कानून के कइसने धरमी हो सकथें; एकर गवाही, मूसा के कानून अऊ अगमजानीमन देथें। 22परमेसर के ए धरमीपन ओ जम्मो झन ऊपर यीसू मसीह म बिसवास के दुवारा आथे, जऊन मन ओकर ऊपर बिसवास करथें। एम कुछू भेदभाव नइं ए। 23काबरकि जम्मो झन पाप करे हवंय अऊ ओमन परमेसर के महिमा ले अलग हवंय, 24अऊ परमेसर ह सेंतमेंत म अपन अनुग्रह ले मनखेमन ला धरमी ठहिराईस अऊ ओमन ला पाप ले मुक्ति दीस, अऊ पाप ले ए मुक्ति ह मसीह यीसू के दुवारा आईस। 25परमेसर ह यीसू ला एक बलिदान के रूप म दे दीस, जऊन ह अपन लहू बहाय के दुवारा पाप के पछताप करिस अऊ जऊन ह ए बात ला बिसवास करथे, ओकर पाप ह छेमा होथे। ए किसम ले परमेसर ह अपन धरमीपन ला देखाईस, काबरकि अपन धीरज धरे के कारन, परमेसर ह ओ पापमन के दंड नइं दीस, जऊन ला पहिली जुग म करे गे रिहिस। 26परमेसर ह ए काम ला एकरसेति करिस, ताकि ए समय म, ए साबित हो जावय कि ओह धरमी अय अऊ ओह ओ मनखे ला सही ठहिराथे, जऊन ह यीसू ऊपर बिसवास करथे।

27तब हमर घमंड करई कहां रिहिस? एकर बर तो जगह नइं ए। कोन नियम के आधार म? का कानून ला माने के आधार म? नइं, पर बिसवास के आधार म। 28काबरकि हमन ए मानथन कि मनखे ह कानून ला माने के दुवारा नइं, पर मसीह यीसू म बिसवास करे के दुवारा सही ठहिरथे। 29का परमेसर ह सिरिप यहूदीमन के परमेसर अय? का ओह आनजातमन के घलो परमेसर नो हय? हव, ओह आनजातमन के घलो परमेसर अय। 30जब सिरिप एक परमेसर हवय, जऊन ह खतना करइयामन (यहूदीमन) ला बिसवास के दुवारा अऊ बिगर खतना करइयामन (आनजातमन) ला घलो ओहीच बिसवास के दुवारा सही ठहिराही, 31त का हमन ए बिसवास के दुवारा कानून ला बेकार कर देवन? बिलकुल नइं! पर, हमन कानून ला बनाय रखथन।