Aroma 3 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 3:1-31

Kukhulupirika kwa Mulungu

1Nanga kodi pali ubwino wotani pokhala Myuda, kapena muli ubwino wanjinso mu mdulidwe? 2Ubwino wake ndi wambiri mʼnjira zonse! Choyambirira iwo anapatsidwa Mawu a Mulungu kuti awasunge.

3Nanga zili bwanji ngati ena analibe chikhulupiriro? Kodi kupanda chikhulupiriro kwawo kukanalepheretsa kukhulupirika kwa Mulungu? 4Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Mulungu akhale woona, ndi munthu aliyense akhale wonama. Monga kwalembedwa kuti,

“Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula

ndi kupambana pamene muweruza.”

5Koma ngati kuyipa mtima kwathu kuonetsa poyera kuti Mulungu ndi wolungama, ife tinganene chiyani? Kodi tinganene kuti Mulungu ndi wosalungama pamene aonetsa mkwiyo wake pa ife? (Ine ndikuyankhula monga mmene anthu ena amayankhulira). 6Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ngati zikanakhala zotero, kodi Mulungu akanaweruza bwanji dziko lapansi? 7Wina atanena kuti, “Ngati kunama kwanga kukuonetsa koposa kuti Mulungu ndi woona, ndi kuwonjezera pa ulemerero wake, nanga nʼchifukwa chiyani ndikuweruzidwa kuti ndine wochimwa?” 8Nʼchifukwa chiyani osanena kuti, monga ena amanena mosasamala kuti, “Tiyeni tichite zoyipa kuti zabwino zionekere?” Anthu onena zoterewa kulangidwa kwawo ndi koyenera.

Palibe Munthu Wolungama

9Kodi timalize bwanji? Kodi Ayuda ndife oposa anthu ena? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ife tinanena kale kuti Ayuda ndi a mitundu ina omwe ndi ochimwa. 10Monga kwalembedwa kuti,

“Palibe munthu wolungama, inde palibe ndi mmodzi yemwe.

11Palibe ndi mmodzi yemwe amene amazindikira,

palibe amene amafunafuna Mulungu.

12Onse apatukira kumbali,

onse pamodzi asanduka opandapake.

Palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita zabwino,

palibe ngakhale mmodzi.”

13“Kummero kwawo kuli ngati manda apululu;

ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.”

“Ululu wa mamba uli pa milomo yawo.”

14“Mʼkamwa mwawo ndi modzaza ndi zotemberera ndi mawu owawa.”

15“Mapazi awo afulumira kukakhetsa magazi.

16Kusakaza ndi chisoni kumaonekera mʼnjira zawo,

17ndipo njira ya mtendere sayidziwa.”

18“Saopa Mulungu ndi pangʼono pomwe.”

19Tsopano tikudziwa kuti chilichonse Malamulo amanena, amanena kwa amene amalamulidwa ndi Malamulowo, ndi cholinga chakuti aliyense asowe chonena, ndipo dziko lonse lidzayimbidwa mlandu ndi Mulungu. 20Chifukwa chake palibe mmodzi amene adzayesedwa wolungama pamaso pake chifukwa chosunga Malamulo, kuti ife timazindikira tchimo kupyolera mu Malamulo.

Kulungama Mwachikhulupiriro

21Koma tsopano chilungamo chochokera kwa Mulungu, osati chochokera ku Malamulo, chaonetsedwa. Ichi ndi chimene Malamulo ndi Aneneri amachitira umboni. 22Timakhala olungama pamaso pa Mulungu pamene takhulupirira Yesu Khristu. Mulungu amachitira zimenezi anthu onse amene akhulupirira Khristu. Palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi a mitundu ina, 23pakuti onse anachimwa naperewera pa ulemerero wa Mulungu 24ndipo onse alungamitsidwa mwaulere mwa chisomo chake chifukwa cha Khristu Yesu amene anawawombola. 25Mulungu anamupereka Iyeyu kuti pokhetsa magazi ake, akhale nsembe yokhululukira machimo. Mulungu anachita zimenezi kufuna kuonetsa chilungamo chake. Chifukwa cha kuleza mtima kwake, sanalange anthu chifukwa cha machimo amene anachita kale. 26Iye anachita izi kuti aonetse chilungamo chake lero lino. Anthu azindikire kuti Iye ndi wolungama ndipo amalungamitsa aliyense amene akhulupirira Yesu.

27Nanga tsono pamenepa munthu anganyadenso? Kunyadatu kwachotsedwa. Chifukwa cha Malamulo? Kodi Malamulo samafuna ntchito za munthu? Ayi, koma mwachikhulupiriro. 28Ife tikunenabe kuti munthu amalungamitsidwa mwachikhulupiriro osati mwakusunga Malamulo. 29Kodi Mulungu ndi Mulungu wa Ayuda okha? Kodi si Mulungu wa a mitundu inanso? Inde wa a mitundu inanso, 30popeza ndi Mulungu mmodzi yemweyo amene adzalungamitsa mwachikhulupiriro ochita mdulidwe ndi osachita mdulidwe kudzera mʼchikhulupiriro chomwecho. 31Kodi tsono ife, tikutaya Malamulo pamene tikunena kuti pafunika chikhulupiriro? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Komatu ife tikukwaniritsadi Malamulo.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

羅馬書 3:1-31

1那麼,猶太人有什麼長處呢?割禮有什麼價值呢? 2其實益處非常多!首先,上帝的聖言託付給了猶太人。 3雖然有些人不相信,但那有什麼關係呢?難道上帝的信實可靠會因他們的不信而化為無有嗎? 4當然不會!縱然人人都撒謊,上帝仍然真實可靠。正如聖經上說:

「你的判語證明你是公義的;

你雖被人控告,卻終必得勝。」

5我姑且用人的觀點說:「如果我們的不義可以反襯出上帝的公義,我們該做何論?上帝向我們發怒是祂不公正嗎?」 6當然不是!若是這樣,上帝怎麼能審判這世界呢? 7你們又說:「如果我們的虛謊凸顯出上帝的真實,增加祂的榮耀,為什麼祂還要把我們當作罪人審判呢?」 8為什麼你們不乾脆說:「我們作惡吧,好成就善事」?有人毀謗我們,說我們傳這種道理。這些人受審判是罪有應得!

沒有義人

9那麼,我們猶太人比別人優越嗎?絕對不是!我們已經說過,無論是猶太人還是希臘人,所有的人都身陷罪中。 10正如聖經上說:

「沒有義人,一個也沒有,

11沒有人明白,沒有人尋求上帝。

12人人偏離正路,變得毫無價值。

沒有人行善,一個也沒有。

13他們的喉嚨是敞開的墳墓,

舌頭上盡是詭詐,

嘴唇有蛇的毒液,

14滿口咒詛,言語惡毒;

15殺人流血,腳步飛快;

16所到之處,大肆毀滅;

17平安之路,他們未曾知道;

18他們眼中毫無對上帝的畏懼。」

19我們知道律法所講的都是針對律法之下的人,好叫所有的人都無話可說,使全世界都伏在上帝的審判之下。 20因為無人能夠靠遵行律法而被上帝視為義人,律法的本意是要使人知罪。

因信稱義

21但如今,上帝的義在律法以外顯明出來,有律法和眾先知做見證。 22人只要信耶穌基督,就可以被上帝稱為義人,沒有一個人例外。 23因為世人都犯了罪,虧欠上帝的榮耀, 24但蒙上帝的恩典,靠著基督耶穌的救贖,世人被無條件地稱為義人。 25上帝使基督耶穌成為贖罪祭,以便人藉著相信耶穌的寶血可以得到赦免。這是為了顯明上帝的義,因為祂用忍耐的心寬容人過去的罪, 26好在現今顯明祂的義,使人知道祂是公義的,祂也稱信耶穌的為義人。

27既然如此,我們哪裡能誇口呢?當然沒有可誇的。靠什麼方法讓人不能誇口呢?靠遵守律法嗎?不是!是靠信主的方法。 28因為我們堅信人被稱為義人是藉著信,不是靠遵行律法。 29難道上帝只是猶太人的上帝嗎?祂不也是外族人的上帝嗎?祂當然也是外族人的上帝。 30因為上帝只有一位,祂本著信稱受割禮的人為義人,也本著信稱未受割禮的人為義人。 31這麼說來,我們是藉著信心廢掉上帝的律法嗎?當然不是!我們反倒是鞏固律法。