Aroma 2 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 2:1-29

Kuweruza Kolungama kwa Mulungu

1Choncho, iwe amene umaweruza munthu wina, ulibe pokanira pakuti nthawi iliyonse pamene uweruza wina ukudzitsutsa wekha chifukwa iwe amene umaweruzawe umachitanso zinthu zomwezo. 2Tsopano ife tikudziwa kuti chiweruzo cha Mulungu, chotsutsa amene amachita zinthu zotere, nʼchokhazikika pa choonadi. 3Kodi ukuganiza kuti udzathawa chiweruzo cha Mulungu iwe munthu wamba, pamene uweruza ena, iwe ndi kumachitanso zomwezo? 4Kodi kapena ukupeputsa kukoma mtima kwa Mulungu, kuleza mtima kwake ndi kupirira kwake? Kodi sukuzindikira kuti kukoma mtima kwakeko, nʼkofuna kuti iweyo ulape machimo ako?

5Koma pakuti ndiwe wosamvera ndi wa mtima wosafuna kulapa, ukudzisungira chilango pa tsiku la mkwiyo wa Mulungu, pamene chiweruzo cholungama cha Mulungu chidzaonetsedwa. 6Mulungu adzabwezera aliyense molingana ndi ntchito zake. 7Iye adzapereka moyo wosatha kwa amene amafunafuna ulemerero, ulemu ndi moyo pochita ntchito zabwino mopirira. 8Koma Mulungu adzakhuthulira mkwiyo ndi ukali wake pa amene amachita zofuna zawo ndi kukana choonadi nʼkumatsatira zoyipa. 9Masautso ndi zowawa zidzagwera munthu aliyense amene amachita zonyansa, kuyambira Myuda kenaka anthu a mitundu ina. 10Koma ulemerero, ulemu ndi mtendere zidzakhala kwa aliyense amene amachita zabwino, kuyambira Myuda kenaka anthu a mitundu ina. 11Pajatu Mulungu alibe tsankho.

12Onse amene amachimwa osadziwa Malamulo, adzawonongeka ngakhale kuti sadziwa Malamulowo. Ndipo onse amene amachimwa akudziwa Malamulo adzaweruzidwa potsata Malamulowo. 13Pakuti si amene amangomva Malamulo amene amakhala wolungama pamaso pa Mulungu, koma ndi okhawo amene amachita zili mʼMalamulomo amene adzatchedwa olungama. 14Ndithu, pamene a mitundu ina, amene alibe Malamulo, koma mwachikhalidwe chawo amachita zimene zili mʼMalamulo, iwowo ndi Malamulo pa iwo okha, ngakhale kuti alibe Malamulowo. 15Ntchito zawo zimaonetsa kuti Malamulowo alembedwa mʼmitima mwawo. Chikumbumtima chawonso chimawachitira umboni pakuti maganizo awo amawatsutsa kapena kuwavomereza. 16Izi zidzachitika pa tsiku limene Mulungu adzaweruza zinsinsi za anthu kudzera mwa Yesu Khristu, monga momwe Uthenga wanga Wabwino unenera.

Ayuda ndi Malamulo

17Koma iweyo, amene umadzitcha kuti ndiwe Myuda, umadalira Malamulo, ndipo umanyadira ubale wako ndi Mulungu, 18ngati umadziwa chifuniro chake, ndi kudziwa zoyenera kuchita chifukwa unaphunzitsidwa ndi Malamulo; 19ngati umadziwadi kuti ndiwe mtsogoleri wa osaona, nyale yowunikira amene ali mu mdima, 20mlangizi wa anthu opusa, mphunzitsi wa makanda, chifukwa umadziwa kuti mʼMalamulo uli nayo nzeru yonse ndi choonadi, 21tsono, iwe amene umaphunzitsa ena, sudziphunzitsa wekha kodi? Kodi iwe amene umalalikira kuti anthu asabe, umabanso? 22Kodi iwe amene umanena kuti anthu asachite chigololo, umachitanso chigololo? Kodi iwe amene umanyasidwa ndi mafano, umalandanso za mʼnyumba zopembedzera mafanowo? 23Kodi iwe amene umadzitama ndi Malamulo, umamuchititsa manyazi Mulungu posamvera Malamulowo? 24Monga kwalembedwa, “Dzina la Mulungu likuchitidwa chipongwe pakati pa a mitundu ina chifukwa cha inu.”

25Mdulidwe umakhala ndi phindu ngati usunga Malamulo, koma ngati sumvera Malamulo, iweyo umakhala ngati kuti sunachite mdulidwe. 26Ngati amene sanachite mdulidwe achita zomwe zili mʼMalamulo, kodi sadzatengedwa ngati ochita mdulidwe? 27Munthu amene sanachite mdulidwe mʼthupi koma amamvera Malamulo adzakutsutsa iwe wosamvera Malamulowe, ngakhale kuti uli nawo Malamulo olembedwawo.

28Myuda weniweni si amene angooneka ngati Myuda pamaso pa anthu, ndipo mdulidwe weniweni si umene umangochitika mʼthupi pamaso pa anthu. 29Ayi, Myuda weniweni ndi amene ali Myuda mu mtima mwake, ndipo mdulidwe weniweni ndi wa mtima, wochitika ndi Mzimu, osati ndi malamulo olembedwa. Woyamikira munthu wotere ndi Mulungu, osati anthu ayi.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Римлянам 2:1-29

Праведный Суд Всевышнего

1Поэтому нет тебе извинения, судящий другого, кто бы ты ни был! Осуждая других, ты тем самым осуждаешь и себя, потому что ты, судящий, сам делаешь то же. 2Мы знаем, что тех, кто так поступает, ждёт Суд Всевышнего, и Суд этот справедлив. 3Так неужели же ты надеешься избежать Суда Всевышнего, осуждая других за то, что делаешь сам? 4Или ты пренебрегаешь великой добротой Всевышнего, Его снисходительностью и долготерпением, не понимая, что доброта Всевышнего ведёт тебя к покаянию? 5Своим упрямством и нераскаявшимся сердцем ты сам накапливаешь гнев, который обрушится на тебя в день гнева Всевышнего, когда свершится Его праведный Суд. 6Всевышний воздаст каждому по его делам2:6 См. Заб. 61:13; Мудр. 24:12.. 7Тем, кто, постоянно творя добро, ищет у Всевышнего славы, чести и бессмертия, Он даст вечную жизнь. 8Но кто ищет своего, кто отвергает истину и следует злу, того ждут гнев и ярость. 9Каждого, делающего зло, ожидают горе и беда, во-первых, иудеев, потом и других. 10А каждого, делающего добро, ждут слава, честь и мир, во-первых, иудеев, потом и других, 11потому что Всевышний не отдаёт предпочтения никому.

12Кто грешит, не имея изложенного в Тавроте Закона, тот вне Закона и погибнет, а кто грешит, зная этот Закон, тот по Закону и будет судим. 13(Всевышний признаёт праведными не тех, кто слушает Закон, а тех, кто его исполняет. 14Да, язычники не имеют Закона, но когда они интуитивно делают то, чего требует Закон, они этим показывают, что им и без изложенного в Тавроте Закона известно, что они должны делать, а что нет. 15Они показывают тем самым, что требования Закона записаны у них в сердце2:15 См. Иер. 31:32-33., и об этом свидетельствуют их совесть и мысли, то оправдывающие их, то обвиняющие.) 16Так будет в тот день, когда Всевышний через Исо Масеха будет судить все тайные дела и мысли людей в согласии с Радостной Вестью, которую я возвещаю.

Иудеи и Закон

17Вот ты называешь себя иудеем, полагаешься на Закон и хвалишься тем, что близок к Всевышнему; 18ты знаешь Его волю и можешь определить согласно Закону, что хорошо, а что нет. 19Ты считаешь, что ты поводырь слепым и свет для тех, кто заблудился во тьме, 20что ты наставник глупцов и учитель невежд, потому что обладаешь Законом – воплощением знания и истины. 21Тогда почему же ты, уча других, не научишь в первую очередь самого себя? Ты проповедуешь против воровства2:21 См. Исх. 20:15; Втор. 5:19., а сам крадёшь; 22ты порицаешь супружескую неверность2:22 См. Исх. 20:14; Втор. 5:18., а сам изменяешь супруге; ты ненавидишь идолов, а сам обкрадываешь языческие храмы; 23ты гордишься Законом, а бесчестишь Всевышнего, нарушая Закон. 24Написано: «Из-за вас бесчестится имя Всевышнего среди язычников»2:24 Ис. 52:5; см. также Езек. 36:20-23..

25В обрезании2:25 Обряд обрезания был установлен Всевышним как знак священного соглашения с Иброхимом и его потомками (см. Нач. 17:9-14). есть польза тогда, когда ты соблюдаешь Закон, но если ты Закон нарушаешь, то в твоём обрезании нет смысла. 26Ведь если язычники соблюдают Закон, то разве они не будут считаться обрезанными? 27И тот, кто лишён телесного обрезания, но исполняет Закон, осудит тебя, обрезанного и имеющего писаный Закон, но не исполняющего его. 28Ведь иудей не тот, кто выглядит иудеем, и настоящее обрезание – не то, которое на теле. 29Нет, настоящий иудей – это тот, кто внутренне таков, и обрезание – это обрезание сердца по духу2:29 Или: «обрезание сердца, сделанное Духом»., а не по букве Закона. Такому человеку похвала не от людей, а от Всевышнего.