Aroma 16 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 16:1-27

Mawu Olawirana

1Ine ndikupereka kwa inu mlongo wathu Febe, mtumiki wa mpingo wa ku Kenkreya. 2Ine ndikukupemphani kuti mumulandire mwa Ambuye mʼnjira yoyenera oyera mtima ndi kumupatsa thandizo lililonse limene akulifuna kuchokera kwa inu, pakuti iye wakhala thandizo lalikulu kwa anthu ambiri kuphatikiza ine.

3Perekani moni kwa Prisila ndi Akura, atumiki anzanga mwa Khristu Yesu. 4Iwo anapereka miyoyo yawo chifukwa cha ine. Osati ine ndekha komanso mipingo yonse ya a mitundu ina ikuyamika.

5Perekaninso moni kwa mpingo umene umasonkhana mʼnyumba mwawo.

Perekani moni kwa mʼbale wanga wokondedwa Epeneto, amene ndi woyamba kukhulupirira Khristu mʼchigawo cha Asiya.

6Perekani moni kwa Mariya, amene wakhala akukugwirirani ntchito kwambiri.

7Perekani moni kwa Androniko ndi Yuniya abale anga amene anali mʼndende pamodzi ndi ine. Iwo amadziwika ndi atumwi, ndipo iwo anali mwa Khristu ine ndisanakhale.

8Perekani moni kwa Ampliato, amene ine ndimamukonda mwa Ambuye.

9Perekani moni kwa Urbano, mtumiki mnzathu mwa Khristu ndi wokondedwa wanga Staku.

10Perekani moni kwa Apele, woyesedwa ndi wovomerezeka mwa Khristu.

Perekani moni kwa a mʼbanja la Aristobulo.

11Perekani moni kwa Herodiona, mʼbale wanga.

Perekani moni kwa a mʼbanja la Narkiso amene ali mwa Ambuye.

12Perekani moni kwa Trufena ndi Trufosa, amayi aja amene amagwira ntchito ya Ambuye molimbika.

Perekani moni kwa mnzanga wokondedwa Persida, mayi winanso amene wagwira ntchito kwambiri mwa Ambuye.

13Perekani moni kwa Rufo, wosankhidwa mwa Ambuye, ndi amayi ake, amene akhala amayi anganso.

14Perekani moni kwa Asunkrito, Felego, Herima, Patroba, Herima ndi abale amene ali nawo pamodzi.

15Perekani moni kwa Filologo, Yuliya, Neriya ndi mlongo wake, ndi Olumpa ndi oyera mtima onse amene ali nawo pamodzi.

16Mupatsane moni wina ndi mnzake mwachikondi choona.

Mipingo yonse ya Khristu ikupereka moni.

17Abale, ine ndikukupemphani kuti musamale chifukwa cha amene ayambitsa mipatuko ndi kuyika zokhumudwitsa panjira yanu, motsutsana ndi chiphunzitso chimene mwachiphunzira. Muwapewe iwo. 18Pakuti otero sakutumikira Ambuye athu Khristu koma zilakolako zawo. Ndi mawu okoma ndi oshashalika iwo amanamiza anthu osalakwa. 19Aliyense anamva za kumvera kwanu, choncho ndine odzaza ndi chimwemwe chifukwa cha inu. Koma ine ndikufuna kuti inu mukhale anzeru pa zabwino, ndi wopanda cholakwa pa zimene zili zoyipa.

20Mulungu wamtendere adzaphwanya Satana msanga pansi pa mapazi anu.

Chisomo cha Ambuye athu Yesu chikhale ndi inu.

21Timoteyo, mtumiki mnzanga, akupereka moni. Nawonso, Lusio, Yasoni ndi Sosipatro, abale anga akutero.

22Ine Tertio, amene ndalemba kalatayi, ndi kupereka moni mwa Ambuye.

23Gayo, amene chifukwa cha chisamaliro chake, ine ndi mpingo wonse kuno tikusangalala, akupereka moni.

Erasto, amene ndi msungichuma wa mzinda wonse ndiponso mʼbale wathu Kwato, akupereka moni.

24Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale ndi inu nonse. Ameni.

25Tsopano kwa Iye amene ali ndi mphamvu yokhazikitsa monga mwa uthenga wanga wabwino ndikulalikidwa kwa Yesu Khristu, monga mwa vumbulutso lachinsinsi chobisika kwa nthawi yayitali, 26koma tsopano chavumbulutsidwa ndi kudziwika kudzera mʼMalemba a uneneri mwa lamulo la Mulungu wosatha, kuti mitundu yonse ikhulupirire ndi kumvera Iye, 27kwa Mulungu yekhayo wanzeru kukhale ulemerero kwamuyaya kudzera mwa Yesu Khristu! Ameni.

Luganda Contemporary Bible

Abaruumi 16:1-27

Okulamusa

116:1 a 2Ko 3:1 b Bik 18:18Kaakano mbanjulira Foyibe mwannyinaffe, era omuweereza w’ekkanisa16:1 Foyibe yali mudiikoni mu kkanisa eyo ey’omu Kenkereya. 216:2 Baf 2:29Mumwanirize mu Mukama waffe, nga bwe kigwanidde abatukuvu, era muyimirire naye nga mumuyamba mu nsonga yonna gye yeetaaga, kubanga naye yennyini yayamba bangi era nange kennyini.

316:3 a Bik 18:2 b nny 7, 9, 10Mundabire Pulisikira ne Akula, bwe tukola omulimu mu Kristo Yesu, 4abeewaayo wakiri okutemwako emitwe olw’obulamu bwange, era si beebaza bokka wabula n’Ekkanisa z’Abamawanga zonna.

516:5 a 1Ko 16:19; Bak 4:15; Fir 2 b 1Ko 16:15Mutuuse okulamusa kwange eri abo bonna abakuŋŋaana ng’ekkanisa mu maka gaabwe.

Mundabire mukwano gwange omwagalwa Epayineeto, kye kibala eky’olubereberye eky’omu Asiya eri Kristo.

6Mundabire Maliyamu eyabakolera ennyo.

716:7 nny 11, 21Mundabire Anduloniiko ne Yuniya ab’ekika kyange, abaasibibwa awamu nange mu kkomera, era bassibwamu nnyo ekitiibwa abatume era be bansooka okubeera mu Kristo.

8Mundabire Ampuliyaato omwagalwa wange mu Mukama waffe.

916:9 nny 3Mundabire Ulubano, mukozi munnaffe mu Kristo, n’omwagalwa waffe Sutaku.

10Mundabire Apere, asiimibwa mu Kristo.

Mundabire n’ab’omu nnyumba ya Alisutobulo.

1116:11 nny 7, 21Mundabire Kerodiyoni muganda wange.

Mundabire ab’omu nnyumba ya Nalukiso.

12Mundabire Terufayina ne Terufoosa, abaakola ennyo omulimu gwa Mukama waffe.

Mundabire Perusi omwagalwa eyakola ennyo omulimu mu Mukama waffe.

13Mundabire Luufo Mukama gwe yalonda, era ne nnyina ali nga mmange.

14Mundabire Asunkulito ne Felegoni, ne Kerume, ne Patuloba, ne Keruma era n’abooluganda abali nabo.

1516:15 a nny 2 b nny 14Mundabire Firologo ne Yuliya, ne Nerewu ne mwannyina, ne Olumpa n’abatukuvu bonna abali awamu nabo.

1616:16 1Ko 16:20; 2Ko 13:12; 1Bs 5:26Mulamusagane n’okunywegera okutukuvu.

Ekkanisa zonna eza Kristo, zibalamusizza.

Ebisembayo

1716:17 a Bag 1:8, 9; 1Ti 1:3; 6:3 b 2Bs 3:6, 14; 2Yk 10Noolwekyo mbakuutira abooluganda mwegenderezenga abo abaleeta enjawukana, n’eby’esittaza ebikontana n’okuyigiriza kwe mwayiga, era mubakubenga amabega. 1816:18 a Baf 3:19 b Bak 2:4Kubanga abantu ng’abo tebaweereza Mukama waffe Yesu, wabula embuto zaabwe. Bakozesa ebigambo ebirungi eby’okuwaanawaana nga balimbalimba emitima gy’abanafu. 1916:19 a Bar 1:8 b Mat 10:16; 1Ko 14:20Kubanga amawulire ag’okuwulira kwammwe gaabuna mu bantu bonna, kyenvudde mbasanyukira. Naye njagala mubenga bagezi mu kukola obulungi, era abalongoofu abeewala ekibi.

2016:20 a Bar 15:33 b Lub 3:15 c 1Bs 5:28Kaakano Katonda ow’emirembe ajja kubetentera Setaani wansi w’ebigere byammwe, mangu.

Ekisa kya Mukama waffe Yesu kibeerenga nammwe.

2116:21 a Bik 16:1 b Bik 13:1 c Bik 17:5 d nny 7, 11Timoseewo mukozi munnange, ne Lukiyo ne Yasooni wamu ne Sosipateri, baganda bange, babatumidde.

22Nange Terutiyo16:22 Terutiyo ye yakubanga tayipu nga Pawulo awandiika ebbaluwa ze awandiika ebbaluwa eno, mbatumidde mu Mukama waffe.

2316:23 Bik 19:22Gaayo16:23 Gaayo yandiba Gaayo ow’omu 1Ko 1:14, Pawulo gwe yabatiza ansuza, n’ekkanisa yonna babalamusizza. Mundabire Erasuto omuwanika w’ekibuga, ne Kwaluto muganda we.

24Ekisa kya Mukama waffe Yesu Kristo kibeerenga nammwe mwenna. Amiina.

Pawulo abasiibula n’okusaba

2516:25 a Bef 3:20 b Bar 2:16 c Bef 1:9; Bak 1:26, 27Kaakano eri oyo ayinza okubanyweza ng’enjiri yange n’okubuulira mu Kristo Yesu bwe biri, ng’ekyama ky’okubikkulirwa eby’ebiro eby’emirembe n’emirembe ebyasirikirwa, bwe kiri, 26kaakano nga bannabbi bwe baayogerera mu byawandiikibwa, ng’ekiragiro kya Katonda ataggwaawo bwe kiri, olw’okugonda mu kukkiriza eri Abaamawanga bonna abaamanyibwa, 2716:27 Bar 11:36Katonda omu yekka ow’amagezi, agulumizibwenga ku bwa Yesu Kristo, emirembe n’emirembe. Amiina.