Aroma 15 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 15:1-33

1Ife amene tili ndi chikhulupiriro champhamvu tiziwalezera mtima anthu ofowoka, ndipo tisamadzikondweretse tokha. 2Aliyense wa ife akondweretse mnzake pomuchitira zabwino zomulimbikitsa. 3Pakuti ngakhale Khristu sanadzikondweretsa yekha koma, monga kwalembedwa kuti, “Chipongwe cha anthu okunyozani chinagwera Ine.” 4Pakuti zilizonse zimene zinalembedwa kale zinalembedwa kuti zitiphunzitse ife. Malembawo amatilimbikitsa kupirira kuti tikhale ndi chiyembekezo.

5Mulungu amene amapereka kupirira ndi chilimbikitso akupatseni maganizo amodzi pakati panu monga inu mukutsatira Khristu Yesu, 6kotero kuti ndi mtima umodzi ndi movomerezana mulemekeze Mulungu ndi Atate a Ambuye athu Yesu Khristu.

7Tsopano landiranani wina ndi mnzake, monganso Khristu anakulandirani inu, ndi cholinga choti Mulungu alemekezeke. 8Chifukwa kunena zoona, Khristu wasanduka mtumiki wa Ayuda, kuonetsa kuti Mulungu ndi wokhulupirika pa malonjezo amene anachita kwa makolo awo 9kuti a mitundu ina atamande Mulungu chifukwa cha chifundo chake. Monga kwalembedwa kuti,

“Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa a mitundu;

ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.”

10Akutinso,

“Kondwerani inu anthu a mitundu ina pamodzi ndi anthu ake.”

11Ndipo akutinso,

“Tamandani Ambuye, inu nonse a mitundu ina,

ndi kuyimba zotamanda Iye, inu anthu onse.”

12Ndiponso Yesaya akuti,

“Muzu wa Yese udzaphuka,

wina amene adzauka kulamulira anthu a mitundu ina;

mwa Iye mudzakhala chiyembekezo cha a mitundu ina.”

13Mulungu amene amatipatsa chiyembekezo adzaze mitima yanu ndi chimwemwe ndi mtendere pamene mukumudalira Iye, kuti chiyembekezo chanu chisefukire mwamphamvu ya Mzimu Woyera.

Paulo Mtumwi wa Anthu a Mitundu Ina

14Abale anga, ine mwini ndikutsimikiza kuti inuyo ndinu abwino, odzaza ndi chidziwitso ndi okhoza kulangizana wina ndi mnzake. 15Ine ndakulemberani inu molimba mtima pa fundo zina, kukhala ngati kukukumbutsaninso za zimenezo, chifukwa cha chisomo chimene Mulungu anandipatsa ine 16kukhala mtumiki wa Khristu Yesu wa a mitundu ina ndi udindo wa wansembe, kulalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu, kuti a mitundu ina akhale nsembe yolandiridwa kwa Mulungu, yopatsidwa ndi Mzimu Woyera.

17Choncho, ine ndikunyadira mwa Khristu Yesu potumikira Mulungu wanga. 18Ine sindidzayesera kuyankhula za kanthu kalikonse koma zimene Khristu wazichita kudzera mwa ine zotsogolera a mitundu ina kuti amvere Mulungu mwa zimene ndinanena ndi kuzichita 19mwamphamvu ya zizindikiro ndi zodabwitsa kudzera mwamphamvu ya Mzimu Woyera. Choncho kuchokera ku Yerusalemu ndi kuzungulira ku Iluriko, ine ndalalikira kwathunthu Uthenga Wabwino wa Khristu. 20Chakhala chilakolako changa nthawi zonse kuti ndilalikire Uthenga Wabwino kumene Khristu sadziwika, kuti ine ndisamange pa maziko a wina wake. 21Koma monga kwalembedwa kuti,

“Iwo amene sanawuzidwe za Iye adzaona,

ndi iwo amene sanamve adzazindikira.”

22Ichi nʼchifukwa chake ine ndakhala ndikuletsedwa kawirikawiri kubwera kwa inu.

Paulo Akonza Zopita ku Roma

23Koma tsopano popeza kulibenso malo anga woti ndigwire ntchito mʼmadera awa, ndakhala ndikufuna kukuonani kwa zaka zambiri. 24Ine ndikukonza kuti nditero pamene ndipita ku Spaniya. Ine ndikuyembekeza kudzakuchezerani pamene ndikudutsa ndi kuti inu mudzathandize popitiriza ulendo wanga, nditasangalala ndi kukhala nanu kwa kanthawi. 25Koma tsopano, ine ndili pa ulendo wopita ku Yerusalemu potumikira oyera mtima akumeneko. 26Pakuti kunakomera a ku Makedoniya ndi a ku Akaya kupereka thandizo kwa osauka pakati pa oyera mtima mu Yerusalemu. 27Iwo chinawakomera kuchita ichi, ndipo ndithu anali ndi ngongole kwa iwo. Pakuti ngati a mitundu ina anagawana ndi Ayuda madalitso auzimu, iwo ali ndi ngongole kwa Ayuda kuti agawane nawo madalitso awo a ku thupi. 28Tsono ine nditamaliza ntchito iyi ndi kutsimikiza kuti alandira chipatsochi, ndidzadzera kwanuko kudzakuchezerani pa ulendo wanga popita ku Spaniya. 29Ine ndikudziwa kuti pamene ndidzabwera kwa inu, ndidzafika ndili wodzaza ndi madalitso a Khristu.

30Abale, ine ndikukupemphani, mwa Ambuye athu Yesu Khristu ndi mwachikondi cha Mzimu, kuti mukhale nane pa kulimbika kwanga pondipempherera kwa Mulungu. 31Pempherani kuti ine ndilanditsidwe kwa osakhulupirira a ku Yudeya ndi kuti utumiki wanga mu Yerusalemu ukhale ovomerezeka ndi oyera mtima. 32Kuti mwachifuniro cha Mulungu ndibwere kwa inu ndi chimwemwe kuti ndidzapumule pamodzi ndi inu. 33Mulungu wamtendere akhale ndi inu nonse. Ameni.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

羅馬書 15:1-33

我為人人

1我們堅強的人要扶助軟弱的人,分擔他們的重擔,不該只顧自己的喜好。 2我們每個人都應該為他人著想,建造他人的生命。 3因為基督並沒有專顧自己,正如聖經上說:「辱駡你之人的辱駡都落在我身上。」 4從前寫在聖經上的話都是為了教導我們,使我們靠著忍耐和聖經的鼓勵而有盼望。 5但願賜忍耐和鼓勵的上帝給你們合一的心去效法基督耶穌的榜樣, 6使你們一起同聲頌贊上帝——我們主耶穌基督的父。

7所以,你們應該像基督接納你們一樣彼此接納,使上帝得榮耀。 8你們要知道,基督為了上帝的真理成為猶太15·8 猶太」希臘文是「受割禮之人」。的僕人,好實現上帝對猶太人祖先們的應許, 9使外族人也因祂的憐憫而將榮耀歸給上帝。正如聖經上說:

「因此,我要在列邦中讚美你,

歌頌你的名。」

10又說:

「外族人啊,

你們當與主的子民一同歡樂。」

11又說:

「萬邦啊,你們當讚美主!

萬民啊,你們當頌讚祂!」

12以賽亞先知也說:

「將來耶西的根要興起,

祂要統治外族,

外族人都要仰望祂。」

13願使人有盼望的上帝,因為你們信祂,將諸般的喜樂和平安充滿你們的心,使你們藉著聖靈的能力充滿盼望!

福音特使

14弟兄姊妹,我知道你們充滿良善,知識全備,能彼此勸導。 15但我仍放膽寫信提醒你們幾件事,因為我蒙上帝賜恩, 16在外族人中作基督耶穌的僕人和上帝福音的祭司,好叫外族人藉著聖靈得以聖潔,可以作上帝喜悅的祭物。 17因此,我在基督耶穌裡以事奉上帝為榮。 18-19別的事我不敢提,只有一件是我津津樂道的,就是基督藉著我的言語行為,用神蹟奇事和聖靈的大能叫外族人順服,使我把基督的福音從耶路撒冷一路傳到了以利哩古。 20我立志只去從未聽過基督之名的地方傳福音,免得我建造在別人的根基上。 21正如聖經上說:「對祂毫無所聞的,將要看見;未曾聽過的,將要明白。」

保羅計劃去羅馬

22因此,我一直受到攔阻,不能到你們那裡。 23但如今福音傳遍了這一帶,況且我幾年來一直盼望去你們那裡, 24所以我想去西班牙的途中路過你們那裡,稍作停留,享受與你們的相聚之樂,然後由你們資助我上路。 25但現在我要去耶路撒冷服侍當地的聖徒, 26因為馬其頓亞該亞的教會欣然捐出了財物給耶路撒冷的窮困聖徒。 27這固然是他們慷慨解囊,但也可以說是他們該還的債。外族人既然分享了猶太聖徒屬靈的福分,現在以物質報答他們也是應該的。 28等我辦完這件事,將捐款交付他們之後,我就會途經你們那裡去西班牙29我知道我去的時候,必會把基督豐盛的祝福帶給你們。

30弟兄姊妹,我藉著我們主耶穌基督和聖靈所賜的愛心,懇求你們與我一同竭力禱告,為我祈求上帝, 31使我脫離猶太地區不信之人的迫害,叫耶路撒冷的聖徒樂意接受我帶去的捐款, 32並使我按照上帝的旨意歡然去與你們相聚,一同重新得力。

33願賜平安的上帝常與你們同在。阿們!