Aroma 14 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 14:1-23

Ofowoka ndi Amphamvu

1Mulandire amene ndi ofowoka mʼchikhulupiriro, osatsutsana naye pa maganizo ake. 2Chikhulupiriro cha munthu wina chimamulola kudya china chilichonse koma munthu wina, amene chikhulupiriro chake ndi chofowoka, amangodya zamasamba zokha. 3Munthu amene amadya chilichonse sayenera kunyoza amene satero, ndipo munthu amene samadya chilichonse asaweruze munthu amene amatero, pakuti Mulungu anamulandira. 4Kodi ndiwe ndani kuti uweruze wantchito wamwini? Mbuye wake yekha ndiye aweruze ngati iye wakhoza kapena walephera pa ntchito yake. Ndipo adzakhoza popeza kuti Mbuye wake angathe kumukhozetsa.

5Munthu wina amayesa tsiku limodzi lopatulika kuposa lina. Munthu wina amayesa masiku onse ofanana. Aliyense akhale otsimikiza mʼmaganizo ake. 6Iye amene amaganiza kuti tsiku limodzi ndi lopambana, amatero kwa Ambuye. Iye amene amadya nyama, amadya mwa Ambuye pakuti amayamika Mulungu. Ndipo iye amene sadya, amatero kwa Ambuye ndi kuyamika Mulungu. 7Pakuti palibe wina wa ife amene amakhala moyo pa yekha ndiponso palibe wina wa ife amene amafa pa yekha. 8Ngati ife tikhala ndi moyo, ife tikhala ndi moyo kwa Ambuye. Ndipo ngati ife tifa, tifa kwa Ambuye. Choncho, ngati tikhala ndi moyo kapena kufa, ndife ake a Ambuye.

9Pa chifukwa ichi, Khristu anafa ndi kuukanso kotero kuti Iye akhale ndi Ambuye wa akufa ndi amoyo. 10Tsono nʼchifukwa chiyani iwe ukuweruza mʼbale wako? Kapena nʼchifukwa chiyani ukumunyoza mʼbale wako? Pakuti ife tonse tidzayima pa mpando wakuweruza wa Mulungu. 11Kwalembedwa, akutero Ambuye,

“Pamene Ine ndili ndi moyo,

aliyense adzandigwadira

ndipo lilime lililonse lidzavomereza Mulungu.”

12Choncho tsopano, aliyense wa ife adzafotokoza yekha kwa Mulungu.

13Motero, tiyeni tisiye kuweruzana wina ndi mnzake. Mʼmalo mwake, tsimikizani mʼmaganizo anu kuti musayike chokhumudwitsa kapena chotchinga mʼnjira ya mʼbale wanu. 14Monga mmodzi amene ndili mwa Ambuye Yesu, ndine wotsimikiza mtima kuti palibe chakudya chimene pachokha ndi chodetsedwa. Koma ngati wina atenga china chake kukhala chodetsedwa, kwa iyeyo ndi chodetsedwa. 15Ngati mʼbale wako akuvutika chifukwa cha chimene umadya, iwe sukuchitanso mwachikondi. Usamuwononge mʼbale wako amene Khristu anamufera chifukwa cha chakudya chakocho. 16Musalole kuti chimene muchiyesa chabwino achinene ngati choyipa. 17Pakuti Ufumu wa Mulungu si nkhani yakudya ndi kumwa, koma chilungamo, mtendere ndi chimwemwe mwa Mzimu Woyera. 18Nʼchifukwa chake aliyense amene atumikira Khristu mʼnjira iyi akondweretsa Mulungu ndi kuvomerezedwa ndi anthu.

19Tsono tiyeni tiyesetse kuchita zimene zidzabweretsa mtendere ndi kulimbikitsana mwachikondi. 20Musawononge ntchito ya Mulungu chifukwa cha chakudya. Chakudya chonse ndi choyera, koma munthu amalakwa ngati adya chilichonse chimene chimakhumudwitsa wina. 21Nʼkwabwino kusadya kapena kumwa vinyo kapena kuchita chilichonse chimene chidzachititsa mʼbale wako kugwa.

22Tsono zimene ukukhulupirira pa zinthu izi zikhale pakati pa iwe ndi Mulungu. Wodala munthu amene sadzitsutsa yekha pa zimene amazivomereza. 23Koma munthu amene akukayika atsutsidwa ngati adya, chifukwa kudya kwake si kwa chikhulupiriro; ndipo chilichonse chosachokera mʼchikhulupiriro ndi tchimo.

Slovo na cestu

Římanům 14:1-23

„Slabí“ a „silní“ věřící

1Lidi, kteří mají příliš úzkostlivou víru, přijímejte mezi sebe, ale ne proto, abyste kritizovali a vyvraceli jejich názory. 2Jeden je přesvědčený, že je nutno dodržovat celou řadu náboženských zákazů a příkazů, například nejí jídla, která pokládá za nečistá. 3Jiný naopak věří, že na tom tolik nezáleží, že může jíst všechno. Kdo jí všechno, ať se nedívá spatra na toho, kdo třeba nejí vůbec maso. A kdo nepožívá maso, ať nekritizuje toho, kdo ho jí bez zábran: vždyť také on byl přijat Bohem. 4Jakým právem chceš odsuzovat toho, jehož pánem nejsi ty, ale Bůh? Je jen Boží záležitostí, zda člověk stojí nebo padá – a i v pádu ho Bůh dokáže zadržet.

5-6Někdo zase činí rozdíl mezi dny v týdnu, zatímco pro jiného je den jako den. Důležité je, aby v těchto věcech každý jednal podle svého přesvědčení a s touhou oslavit Boha. 7-8Vždyť nikdo z nás nežije ani neumírá jen pro sebe. 9Proto Kristus zemřel a zase vstal, aby si podmanil vše živé i mrtvé. Tak tedy v životě i ve smrti náležíme jemu. 10Proč tedy odsuzovat bratra a pohrdat jím? Všichni se přece budeme muset postavit před Boží soud. 11Vždyť je psáno:

„Každé koleno přede mnou poklekne,

každý jazyk mě bude velebit.“

12Každý sám za sebe bude skládat účty Bohu.

Ohleduplnost – základ pokojného soužití

13Nechte už tedy vzájemného kritizování; raději se mějte na pozoru, aby váš bratr neklopýtl a nepadl vaší vinou. 14-16Vím a jsem o tom plně přesvědčen – tak mi to dal poznat Ježíš, že nic není nečisté samo o sobě. Nečistými se stávají věci jen tomu, kdo je za nečisté považuje. Ale rozhodujícím hlediskem ať je vždy láska. I když nám svědomí v tom či onom nebrání, důležitější je nepohoršit bratra. Co samo o sobě ještě není špatné, může vyvolat špatnou odezvu. 17V Božím království nejde přece o jídlo a pití, ale o spravedlnost, pokoj a radost, jak je dává Duch svatý. 18Kdo v tomto duchu slouží Kristu, líbí se Bohu a váží si ho i lidé. 19Usilujme tedy především o to, co slouží všem k pokoji a ke vzájemnému duchovnímu prospěchu. 20Nepoškozujme Boží dílo kvůli podružnostem a vyhýbejme se všemu, co by mohlo oslabit víru bratra. 21Je lepší odepřít si, co vadí mému bratru, než někoho zranit. 22-23Své přesvědčení však nezrazujme; Bůh o něm ví. Budeme šťastni a bez výčitek, když uposlechneme hlas svého svědomí. Neřídit se jím a zapřít své přesvědčení je hřích.