Aroma 14 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 14:1-23

Ofowoka ndi Amphamvu

1Mulandire amene ndi ofowoka mʼchikhulupiriro, osatsutsana naye pa maganizo ake. 2Chikhulupiriro cha munthu wina chimamulola kudya china chilichonse koma munthu wina, amene chikhulupiriro chake ndi chofowoka, amangodya zamasamba zokha. 3Munthu amene amadya chilichonse sayenera kunyoza amene satero, ndipo munthu amene samadya chilichonse asaweruze munthu amene amatero, pakuti Mulungu anamulandira. 4Kodi ndiwe ndani kuti uweruze wantchito wamwini? Mbuye wake yekha ndiye aweruze ngati iye wakhoza kapena walephera pa ntchito yake. Ndipo adzakhoza popeza kuti Mbuye wake angathe kumukhozetsa.

5Munthu wina amayesa tsiku limodzi lopatulika kuposa lina. Munthu wina amayesa masiku onse ofanana. Aliyense akhale otsimikiza mʼmaganizo ake. 6Iye amene amaganiza kuti tsiku limodzi ndi lopambana, amatero kwa Ambuye. Iye amene amadya nyama, amadya mwa Ambuye pakuti amayamika Mulungu. Ndipo iye amene sadya, amatero kwa Ambuye ndi kuyamika Mulungu. 7Pakuti palibe wina wa ife amene amakhala moyo pa yekha ndiponso palibe wina wa ife amene amafa pa yekha. 8Ngati ife tikhala ndi moyo, ife tikhala ndi moyo kwa Ambuye. Ndipo ngati ife tifa, tifa kwa Ambuye. Choncho, ngati tikhala ndi moyo kapena kufa, ndife ake a Ambuye.

9Pa chifukwa ichi, Khristu anafa ndi kuukanso kotero kuti Iye akhale ndi Ambuye wa akufa ndi amoyo. 10Tsono nʼchifukwa chiyani iwe ukuweruza mʼbale wako? Kapena nʼchifukwa chiyani ukumunyoza mʼbale wako? Pakuti ife tonse tidzayima pa mpando wakuweruza wa Mulungu. 11Kwalembedwa, akutero Ambuye,

“Pamene Ine ndili ndi moyo,

aliyense adzandigwadira

ndipo lilime lililonse lidzavomereza Mulungu.”

12Choncho tsopano, aliyense wa ife adzafotokoza yekha kwa Mulungu.

13Motero, tiyeni tisiye kuweruzana wina ndi mnzake. Mʼmalo mwake, tsimikizani mʼmaganizo anu kuti musayike chokhumudwitsa kapena chotchinga mʼnjira ya mʼbale wanu. 14Monga mmodzi amene ndili mwa Ambuye Yesu, ndine wotsimikiza mtima kuti palibe chakudya chimene pachokha ndi chodetsedwa. Koma ngati wina atenga china chake kukhala chodetsedwa, kwa iyeyo ndi chodetsedwa. 15Ngati mʼbale wako akuvutika chifukwa cha chimene umadya, iwe sukuchitanso mwachikondi. Usamuwononge mʼbale wako amene Khristu anamufera chifukwa cha chakudya chakocho. 16Musalole kuti chimene muchiyesa chabwino achinene ngati choyipa. 17Pakuti Ufumu wa Mulungu si nkhani yakudya ndi kumwa, koma chilungamo, mtendere ndi chimwemwe mwa Mzimu Woyera. 18Nʼchifukwa chake aliyense amene atumikira Khristu mʼnjira iyi akondweretsa Mulungu ndi kuvomerezedwa ndi anthu.

19Tsono tiyeni tiyesetse kuchita zimene zidzabweretsa mtendere ndi kulimbikitsana mwachikondi. 20Musawononge ntchito ya Mulungu chifukwa cha chakudya. Chakudya chonse ndi choyera, koma munthu amalakwa ngati adya chilichonse chimene chimakhumudwitsa wina. 21Nʼkwabwino kusadya kapena kumwa vinyo kapena kuchita chilichonse chimene chidzachititsa mʼbale wako kugwa.

22Tsono zimene ukukhulupirira pa zinthu izi zikhale pakati pa iwe ndi Mulungu. Wodala munthu amene sadzitsutsa yekha pa zimene amazivomereza. 23Koma munthu amene akukayika atsutsidwa ngati adya, chifukwa kudya kwake si kwa chikhulupiriro; ndipo chilichonse chosachokera mʼchikhulupiriro ndi tchimo.

Священное Писание

Римлянам 14:1-23

Не судите

1Человека, слабого в вере, принимайте, не споря о мнениях. 2Вера одного позволяет ему есть всё, а слабый в вере ест только овощи. 3Тот, кто ест всё, не должен смотреть свысока на того, кто этого не делает, и тот, кто чего-то не ест, не должен осуждать того, кто ест, потому что Всевышний принял его. 4Кто ты такой, чтобы судить чужого слугу? Лишь его хозяин решает, справился слуга или нет. Но силою Повелителя слуга обязательно справится.

5Кто-то различает дни как более и менее важные, а для другого все дни одинаковы. Пусть каждый и дальше поступает в соответствии со своими убеждениями. 6Кто считает, что один день важнее другого, тот делает это для Повелителя. Кто ест что-либо – ест для Повелителя, потому что он при этом благодарит Всевышнего, и кто не ест этого – тоже для Повелителя не ест и благодарит Всевышнего. 7Никто из нас не живёт для себя и не умирает для себя. 8Если мы живём, то живём для Повелителя, и если умираем, то умираем тоже для Повелителя. Живём мы или умираем – мы принадлежим Ему.

9Ведь для этого и Масих умер и ожил, чтобы Ему быть Повелителем живых и мёртвых. 10Почему же ты судишь своего брата? Или ты, почему презираешь своего брата? Ведь все мы предстанем на Суд Всевышнего. 11Написано:

«Верно, как и то, что Я живу, – говорит Вечный, –

каждое колено преклонится предо Мной,

и каждый язык исповедает, что Я Бог»14:11 Ис. 49:18; 45:23..

12Каждый из нас ответит перед Всевышним сам за себя.

Не давайте повода к претыканиям

13Поэтому не будем больше судить друг друга. Лучше смотрите за собой, чтобы не делать ничего такого, из-за чего брат ваш может споткнуться и упасть. 14Моё единение с Повелителем Исой даёт мне знание и твёрдую убеждённость, что нет никакой пищи, которая была бы сама по себе нечиста14:14 Букв.: «нет ничего, что было бы нечисто само по себе»., но если человек считает что-либо нечистым, то для него оно нечисто. 15Если твой брат оскорбляется из-за пищи, которую ты ешь, то ты поступаешь не по любви. Не губи своей пищей брата, за которого умер Масих. 16Не давайте людям повода ругать то, что вы считаете позволительным. 17Царство Всевышнего заключается не в пище и питье, а в праведности, в мире и в радости, которую даёт Святой Дух. 18Кто так служит Масиху, тот доставляет радость Всевышнему и заслуживает одобрения людей.

19Будем же прилагать все усилия, чтобы делать то, что ведёт к миру и взаимному назиданию. 20Не разрушайте дела Всевышнего ради пищи. Вся пища чиста, но плохо поступает тот, кто через пищу приводит своего ближнего к падению. 21Лучше не есть мяса, не пить вина и не делать ничего, от чего твой брат спотыкается. 22Пусть твоё мнение на этот счёт будет твоим личным убеждением перед Всевышним, и счастлив тот, кто не осуждает себя за свой выбор. 23Кто ест и в то же время сомневается в правильности своего решения, уже осуждён, потому что он не поступает в соответствии со своей верой, а всё, что не по вере, – грех14:23 Некоторые рукописи помещают здесь стихи 16:25-27..