Aroma 13 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 13:1-14

Kumvera Aulamuliro

1Aliyense ayenera kumvera akulu olamulira, chifukwa palibe ulamuliro umene sunachokere kwa Mulungu. Olamulira amene alipo anayikidwa ndi Mulungu. 2Kotero kuti, iwo amene awukira ulamuliro atsutsana ndi chimene Mulungu anakhazikitsa. Ndipo amene atero adzibweretsera okha chilango. 3Pakuti olamulira saopseza amene amachita zabwino koma amene amachita zoyipa. Kodi mukufuna kukhala osaopa olamulira? Tsono chitani zoyenera ndipo adzakuyamikirani. 4Pakuti iyeyo ndi mtumiki wa Mulungu wokuchitirani zabwino. Koma ngati muchita zoyipa muchite mantha, pakuti iye ali ndi mphamvu zolangira. Iye ndi mtumiki wa Mulungu wobweretsa mkwiyo ndi kulanga onse ochita zoyipa. 5Nʼchifukwa chake ndi koyenera kugonjera olamulira, osati chifukwa choopa kulangidwa kokha komanso chifukwa cha chikumbumtima. 6Ichi nʼchifukwa chakenso inu mumapereka msonkho. Pakuti olamulira ndi atumiki a Mulungu amene amapereka nthawi yawo yonse kulamulira. 7Mubwezereni aliyense amene munamukongola. Ngati inu muli ndi ngongole yamsonkho, perekani msonkho kwa oyenera kuwalipira. Ngati ndi kuopa perekeni kwa oyenera kuwaopa ndipo ngati ndi ulemu kwa oyenera ulemu.

Chikondi Chimakwaniritsa Malamulo

8Musakhale ndi ngongole ndi wina aliyense kupatula ngongole ya kukondana wina ndi mnzake. Pakuti amene amakonda munthu mnzake wakwaniritsa lamulo. 9Malamulo awa: “Usachite chigololo,” “Usaphe,” “Usabe,” “Usasirire,” ndi malamulo ena onse amene alipo, akhazikika pa lamulo limodzi ili, “Konda mnansi wako monga iwe mwini.” 10Chikondi sichichitira mnzake zoyipa. Chifukwa chake chikondi ndicho chokwaniritsa lamulo.

11Ndipo chitani ichi pozindikira nthawi ino. Nthawi yafika yoti inu mudzuke kutulo, chifukwa chipulumutso chathu chili pafupi tsopano kuposa pamene tinayamba kukhulupirira. 12Usiku watsala pafupifupi kutha. Kwatsala pangʼono kucha. Tiyeni tsono tichotse ntchito zamdima ndipo tivale chovala chakuwunika. 13Tiyeni tikhale moyenera monga nthawi ya masana, osati mʼmagulu amadyerero, achiwerewere ndi kuledzera, mʼmadama ndi zonyansa komanso osati mʼmagawano ndi nsanje. 14Koma valani Ambuye Yesu Khristu ndipo musaganizire za momwe mungakwaniritsire zokhumba zachikhalidwe cha uchimo.

Thai New Contemporary Bible

โรม 13:1-14

การยอมเชื่อฟังผู้มีอำนาจปกครอง

1ทุกคนต้องยอมตนเชื่อฟังผู้มีอำนาจปกครอง เพราะไม่มีผู้ใดมีอำนาจเว้นแต่พระเจ้าได้ทรงสถาปนา ผู้มีอำนาจต่างๆ ที่มีอยู่

ล้วนได้รับการแต่งตั้งจากพระเจ้า 2ฉะนั้นผู้ที่กบฏต่อผู้มีอำนาจก็กำลังกบฏต่อผู้ที่พระเจ้าได้ทรงสถาปนา และผู้ที่ทำเช่นนั้นจะนำโทษมาสู่ตนเอง 3เพราะว่าผู้ปกครองบ้านเมืองนั้นไม่น่ากลัวสำหรับคนที่ทำถูก แต่น่ากลัวสำหรับคนที่ทำผิด ท่านอยากจะพ้นจากความกลัวผู้มีอำนาจใช่ไหม? ถ้าเช่นนั้นก็จงทำสิ่งที่ถูกต้อง แล้วเขาจะชมเชยท่าน 4เพราะเขาเป็นผู้รับใช้ของพระเจ้าเพื่อประโยชน์

สุขของท่าน แต่ถ้าท่านทำผิดก็จงกลัวเถิด เพราะเขาไม่ได้ถือดาบไว้เฉยๆ เขาเป็นผู้รับใช้ของพระเจ้า เป็นตัวแทนของพระพิโรธที่จะนำการลงโทษมาสู่ผู้กระทำผิด 5ฉะนั้นเราจึงต้องยอมเชื่อฟังผู้มีอำนาจไม่เพียงเพราะกลัวการลงโทษ แต่เพราะเห็นแก่จิตสำนึกด้วย

6และนี่คือเหตุผลที่ท่านเสียภาษี เพราะผู้มีอำนาจเป็นผู้รับใช้ของพระเจ้า ผู้ให้เวลาทั้งหมดของตนในการปกครองบ้านเมือง 7จงให้แก่ทุกคนในสิ่งที่ท่านติดค้างเขาคือ ถ้าท่านติดค้างส่วยสาอากร จงเสียส่วยสาอากร ถ้าติดค้างภาษี จงเสียภาษี ถ้าควรให้ความเคารพ จงให้ความเคารพ ถ้าควรให้เกียรติ จงให้เกียรติ

จงรักกันเพราะวันนั้นใกล้เข้ามาแล้ว

8อย่าติดค้างเป็นหนี้ใคร เว้นแต่หนี้ซึ่งไม่อาจจ่ายคืนได้หมด คือความรักที่มีต่อกันและกัน เพราะผู้ที่รักเพื่อนมนุษย์ก็ได้ปฏิบัติตามบทบัญญัติอย่างครบถ้วนแล้ว 9พระบัญญัติที่ว่า “อย่าล่วงประเวณี” “อย่าฆ่าคน” “อย่าลักขโมย” “อย่าโลภ”13:9 อพย.20:13-15,17ฉธบ.5:17-19,21 และพระบัญญัติอื่นๆ ล้วนรวมอยู่ในข้อนี้คือ “จงรักเพื่อนบ้านเหมือนรักตนเอง”13:9 ลนต.19:18 10ความรักไม่ทำร้ายเพื่อนบ้านของตน ฉะนั้นการมีความรักจึงเป็นการปฏิบัติตามบทบัญญัติอย่างครบถ้วนแล้ว

11และจงทำอย่างนี้ด้วยเข้าใจว่าปัจจุบันเป็นเวลาอะไร ถึงเวลาแล้วที่ท่านจะตื่นจากหลับเพราะบัดนี้ความรอดของเราใกล้เข้ามามากยิ่งกว่าเมื่อเราแรกเชื่อ 12กลางคืนเกือบจะจบสิ้นลง จวนจะรุ่งเช้าแล้ว ดังนั้นให้เราถอดพฤติการณ์ของความมืดออกไปและสวมยุทธภัณฑ์ของความสว่าง 13ให้เราประพฤติตนอย่างเหมาะสมเหมือนอยู่ในเวลากลางวัน ไม่เที่ยวมั่วสุม เสพสุราเมามาย ไม่ทำผิดศีลธรรมทางเพศและเสเพล ไม่แตกก๊กแตกเหล่าและอิจฉาริษยากัน 14แต่จงประดับกายด้วยองค์พระเยซูคริสต์เจ้า และอย่าคิดว่าจะสนองความปรารถนาของวิสัยบาป13:14 หรือเนื้อหนังอย่างไรดี