Aroma 13 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 13:1-14

Kumvera Aulamuliro

1Aliyense ayenera kumvera akulu olamulira, chifukwa palibe ulamuliro umene sunachokere kwa Mulungu. Olamulira amene alipo anayikidwa ndi Mulungu. 2Kotero kuti, iwo amene awukira ulamuliro atsutsana ndi chimene Mulungu anakhazikitsa. Ndipo amene atero adzibweretsera okha chilango. 3Pakuti olamulira saopseza amene amachita zabwino koma amene amachita zoyipa. Kodi mukufuna kukhala osaopa olamulira? Tsono chitani zoyenera ndipo adzakuyamikirani. 4Pakuti iyeyo ndi mtumiki wa Mulungu wokuchitirani zabwino. Koma ngati muchita zoyipa muchite mantha, pakuti iye ali ndi mphamvu zolangira. Iye ndi mtumiki wa Mulungu wobweretsa mkwiyo ndi kulanga onse ochita zoyipa. 5Nʼchifukwa chake ndi koyenera kugonjera olamulira, osati chifukwa choopa kulangidwa kokha komanso chifukwa cha chikumbumtima. 6Ichi nʼchifukwa chakenso inu mumapereka msonkho. Pakuti olamulira ndi atumiki a Mulungu amene amapereka nthawi yawo yonse kulamulira. 7Mubwezereni aliyense amene munamukongola. Ngati inu muli ndi ngongole yamsonkho, perekani msonkho kwa oyenera kuwalipira. Ngati ndi kuopa perekeni kwa oyenera kuwaopa ndipo ngati ndi ulemu kwa oyenera ulemu.

Chikondi Chimakwaniritsa Malamulo

8Musakhale ndi ngongole ndi wina aliyense kupatula ngongole ya kukondana wina ndi mnzake. Pakuti amene amakonda munthu mnzake wakwaniritsa lamulo. 9Malamulo awa: “Usachite chigololo,” “Usaphe,” “Usabe,” “Usasirire,” ndi malamulo ena onse amene alipo, akhazikika pa lamulo limodzi ili, “Konda mnansi wako monga iwe mwini.” 10Chikondi sichichitira mnzake zoyipa. Chifukwa chake chikondi ndicho chokwaniritsa lamulo.

11Ndipo chitani ichi pozindikira nthawi ino. Nthawi yafika yoti inu mudzuke kutulo, chifukwa chipulumutso chathu chili pafupi tsopano kuposa pamene tinayamba kukhulupirira. 12Usiku watsala pafupifupi kutha. Kwatsala pangʼono kucha. Tiyeni tsono tichotse ntchito zamdima ndipo tivale chovala chakuwunika. 13Tiyeni tikhale moyenera monga nthawi ya masana, osati mʼmagulu amadyerero, achiwerewere ndi kuledzera, mʼmadama ndi zonyansa komanso osati mʼmagawano ndi nsanje. 14Koma valani Ambuye Yesu Khristu ndipo musaganizire za momwe mungakwaniritsire zokhumba zachikhalidwe cha uchimo.

New Serbian Translation

Римљанима 13:1-14

Дужности према властима

1Сваки човек нека се покорава државним властима. Јер ниједна власт не постоји без Божијег допуштења; Бог је поставио постојеће власти. 2Према томе, ко се супротставља власти, противи се ономе што је Бог уредио, а који се томе противе, биће осуђени. 3Владари, наиме, не представљају страх за оне који чине добро, него за оне који чине зло. Ако не желиш да се бојиш власти, чини добро, па ће те власт похвалити. 4Јер, власт служи Богу за твоје добро. Ако чиниш зло, бој се, јер власт не носи мач без разлога. Она је Божији слуга, извршилац казне над оним који чини зло. 5Стога се треба покоравати властима, не само да би се избегла казна, него и ради савести. 6Због тога и плаћате порезе, јер они који раде на томе, Божије су слуге. 7Плаћајте свакоме што дугујете: порез ономе коме дугујете порез, царину ономе коме дугујете царину; поштовање ономе коме дугујете поштовање, и част ономе коме дугујете част. 8Никоме ништа не дугујте, осим да волите једни друге. Јер онај који воли другога, испунио је Божији Закон. 9Наиме, заповести: „Не чини прељубе, не убиј, не укради, не пожели туђе“, и било која друга, своде се на ову једну: „Воли ближњега свога као самога себе.“ 10Љубав не наноси зло ближњему. Према томе, љубав је испуњење Закона.

11Чините ово, јер знате у каквом времену живимо. Дошао је час да се пробудите из сна, јер сад нам је спасење ближе него онда када смо узверовали. 12Ноћ је на измаку, а дан се назире. Стога, одбацимо од себе дела која припадају тами и опашимо се оружјем светлости. 13Живимо како приличи животу по дану, не у банчењима и пијанкама, не у разврату и похотама, не у свађи и зависти, 14него обуците се у Господа Исуса Христа. И не удовољавајте пожудама бринући се за тело.