Aroma 13 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 13:1-14

Kumvera Aulamuliro

1Aliyense ayenera kumvera akulu olamulira, chifukwa palibe ulamuliro umene sunachokere kwa Mulungu. Olamulira amene alipo anayikidwa ndi Mulungu. 2Kotero kuti, iwo amene awukira ulamuliro atsutsana ndi chimene Mulungu anakhazikitsa. Ndipo amene atero adzibweretsera okha chilango. 3Pakuti olamulira saopseza amene amachita zabwino koma amene amachita zoyipa. Kodi mukufuna kukhala osaopa olamulira? Tsono chitani zoyenera ndipo adzakuyamikirani. 4Pakuti iyeyo ndi mtumiki wa Mulungu wokuchitirani zabwino. Koma ngati muchita zoyipa muchite mantha, pakuti iye ali ndi mphamvu zolangira. Iye ndi mtumiki wa Mulungu wobweretsa mkwiyo ndi kulanga onse ochita zoyipa. 5Nʼchifukwa chake ndi koyenera kugonjera olamulira, osati chifukwa choopa kulangidwa kokha komanso chifukwa cha chikumbumtima. 6Ichi nʼchifukwa chakenso inu mumapereka msonkho. Pakuti olamulira ndi atumiki a Mulungu amene amapereka nthawi yawo yonse kulamulira. 7Mubwezereni aliyense amene munamukongola. Ngati inu muli ndi ngongole yamsonkho, perekani msonkho kwa oyenera kuwalipira. Ngati ndi kuopa perekeni kwa oyenera kuwaopa ndipo ngati ndi ulemu kwa oyenera ulemu.

Chikondi Chimakwaniritsa Malamulo

8Musakhale ndi ngongole ndi wina aliyense kupatula ngongole ya kukondana wina ndi mnzake. Pakuti amene amakonda munthu mnzake wakwaniritsa lamulo. 9Malamulo awa: “Usachite chigololo,” “Usaphe,” “Usabe,” “Usasirire,” ndi malamulo ena onse amene alipo, akhazikika pa lamulo limodzi ili, “Konda mnansi wako monga iwe mwini.” 10Chikondi sichichitira mnzake zoyipa. Chifukwa chake chikondi ndicho chokwaniritsa lamulo.

11Ndipo chitani ichi pozindikira nthawi ino. Nthawi yafika yoti inu mudzuke kutulo, chifukwa chipulumutso chathu chili pafupi tsopano kuposa pamene tinayamba kukhulupirira. 12Usiku watsala pafupifupi kutha. Kwatsala pangʼono kucha. Tiyeni tsono tichotse ntchito zamdima ndipo tivale chovala chakuwunika. 13Tiyeni tikhale moyenera monga nthawi ya masana, osati mʼmagulu amadyerero, achiwerewere ndi kuledzera, mʼmadama ndi zonyansa komanso osati mʼmagawano ndi nsanje. 14Koma valani Ambuye Yesu Khristu ndipo musaganizire za momwe mungakwaniritsire zokhumba zachikhalidwe cha uchimo.

Священное Писание

Римлянам 13:1-14

О власти

1Каждый человек должен подчиняться существующей власти, потому что нет власти не от Всевышнего. Все существующие власти установлены Всевышним. 2Следовательно, тот, кто восстаёт против власти, – восстаёт против установленного Всевышним, и кто так поступает, тот сам на себя навлекает суд. 3Правители страшны не тем, кто делает добро, а тем, кто делает зло. Если хочешь жить без страха перед властью, делай добро и получишь от неё похвалу. 4Представитель власти на службе у Всевышнего для твоего блага. Если же ты делаешь зло, то берегись, он не напрасно носит меч. Он – слуга Всевышнего, орудие Его гнева, направленное на того, кто делает зло. 5Так что необходимо подчиняться власти не только из страха перед наказанием, но и по совести.

6Вы и налоги платите потому, что стоящие у власти – слуги Всевышнего, посвящающие себя своему делу. 7Так что отдавайте всем то, что им надлежит: кому налог – налог, кому пошлину – пошлину, кому уважение – уважение, кому честь – честь.

О братской любви

8Не оставайтесь в долгу ни у кого ни в чём, кроме долга любви друг к другу, потому что любящий ближнего исполнил Закон. 9Вот в чём суть повелений Закона: «Не нарушай супружескую верность», «не убивай», «не кради», «не пожелай чужого»13:9 Исх. 20:13-15, 17; Втор. 5:17-19, 21., и суть любого другого повеления одна – «люби ближнего твоего, как самого себя»13:9 Лев. 19:18.. 10Любовь не причиняет зла ближнему, поэтому любовь и есть исполнение Закона.

Приближение последнего дня

11Вы ведь знаете, какое сейчас время, что настал час пробудиться вам ото сна, потому что наше спасение сейчас гораздо ближе, чем оно было тогда, когда мы только уверовали. 12Ночь приближается к концу, и наступает день. Так давайте же оставим дела тьмы и наденем доспехи света. 13Будем жить достойно, как при свете дня, не предаваясь оргиям, пьянству, разврату, распущенности, вражде и зависти. 14Пусть лучше Повелитель Иса Масих станет вашими доспехами. И не думайте об угождении своей греховной природе и её желаниям.