Aroma 12 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 12:1-21

Nsembe za Moyo

1Nʼchifukwa chake ine ndikukupemphani abale, mwa chifundo cha Mulungu, kuti mupereke matupi anu monga nsembe yamoyo, yopatulika ndi yokondweretsa Mulungu. Nsembeyi ndiye kupembedza kwanu kwa uzimu. 2Musafanizidwenso ndi makhalidwe a dziko lino koma musandulike pokonzanso maganizo anu. Ndipo mudzadziwa ndi kuzindikira chifuniro chabwino cha Mulungu chomwe ndi chokondweretsa ndi changwiro.

3Chifukwa cha chisomo chopatsidwa kwa ine, ndinena kwa aliyense wa inu kuti musadziyenereze nokha kuposa mmene mulili. Koma mudziganizire nokha modzichepetsa, molingana ndi muyeso wa chikhulupiriro chimene Mulungu wakupatsani. 4Pakuti monga aliyense wa ife ali ndi thupi limodzi koma ziwalo zambiri, ziwalozi sizili ndi ntchito yofanana. 5Momwemonso mwa Khristu ife amene tili ambiri tipanga thupi limodzi ndipo chiwalo chilichonse ndi cholumikizika ku chinzake. 6Ife tili ndi mphatso zosiyana, molingana ndi chisomo chopatsidwa kwa ife. Ngati mphatso ya munthu ndi kunenera, musiyeni ayigwiritse ntchito molingana ndi chikhulupiriro chake. 7Ngati ndi kutumikira, musiyeni atumikire. Ngati ndi kuphunzitsa, musiyeni aphunzitse. 8Ngati ndi kulimbikitsa, musiyeni alimbikitse. Ngati ndi kupereka kuthandiza osowa, musiyeni apereke mowolowamanja. Ngati ndi utsogoleri, musiyeni alamulire mosamala. Ngati ndi kuonetsa chifundo, musiyeni achite mosangalala.

Chikondi

9Chikondi chikhale chopanda chinyengo. Dana nacho choyipa; gwiritsitsa chabwino. 10Mukondane kwathunthu monga abale. Lemekezanani wina ndi mnzake kuposa inu eni. 11Musakhale aulesi mʼmachitidwe anu. Khalani achangu mu mzimu ndipo tumikirani Ambuye. 12Kondwerani mʼchiyembekezo, pirirani mʼmasautso ndiponso khulupirikani mʼpemphero. 13Gawanani ndi anthu a Mulungu amene ali ndi chosowa. Cherezani alendo.

14Adalitseni amene akuzunzani. Adalitseni ndipo musawatemberere. 15Kondwani pamodzi ndi amene akukondwa ndipo lirani ndi amene akulira. 16Muyanjane wina ndi mnzake. Musakhale onyada, koma lolani kuyanjana ndi anthu wamba. Musaganize kuti mumadziwa zonse.

17Musabwezere choyipa ndi choyipa kwa aliyense. Samalitsani kuchita chabwino pamaso pa aliyense. 18Ngati nʼkotheka, khalani mwamtendere ndi aliyense monga momwe mungathere. 19Okondedwa anga, musabwezere choyipa, koma lekerani Mulungu. Pakuti kwalembedwa, “Kubwezera chilango nʼkwanga. Ndidzawalanga ndine,” akutero Ambuye. 20Koma,

“Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya.

Ngati ali ndi ludzu, mupatse kanthu kakumwa.

Pochita ichi, udzamuwunjikira makala amoto pamutu pake.”

21Musagonjetsedwe ndi choyipa, koma gonjetsani choyipa pochita chabwino.

New International Version – UK

Romans 12:1-21

A living sacrifice

1Therefore, I urge you, brothers and sisters, in view of God’s mercy, to offer your bodies as a living sacrifice, holy and pleasing to God – this is your true and proper worship. 2Do not conform to the pattern of this world, but be transformed by the renewing of your mind. Then you will be able to test and approve what God’s will is – his good, pleasing and perfect will.

Humble service in the body of Christ

3For by the grace given me I say to every one of you: do not think of yourself more highly than you ought, but rather think of yourself with sober judgment, in accordance with the faith God has distributed to each of you. 4For just as each of us has one body with many members, and these members do not all have the same function, 5so in Christ we, though many, form one body, and each member belongs to all the others. 6We have different gifts, according to the grace given to each of us. If your gift is prophesying, then prophesy in accordance with your12:6 Or the faith; 7if it is serving, then serve; if it is teaching, then teach; 8if it is to encourage, then give encouragement; if it is giving, then give generously; if it is to lead,12:8 Or to provide for others do it diligently; if it is to show mercy, do it cheerfully.

Love in action

9Love must be sincere. Hate what is evil; cling to what is good. 10Be devoted to one another in love. Honour one another above yourselves. 11Never be lacking in zeal, but keep your spiritual fervour, serving the Lord. 12Be joyful in hope, patient in affliction, faithful in prayer. 13Share with the Lord’s people who are in need. Practise hospitality.

14Bless those who persecute you; bless and do not curse. 15Rejoice with those who rejoice; mourn with those who mourn. 16Live in harmony with one another. Do not be proud, but be willing to associate with people of low position.12:16 Or willing to do menial work Do not be conceited.

17Do not repay anyone evil for evil. Be careful to do what is right in the eyes of everyone. 18If it is possible, as far as it depends on you, live at peace with everyone. 19Do not take revenge, my dear friends, but leave room for God’s wrath, for it is written: ‘It is mine to avenge; I will repay,’12:19 Deut. 32:35 says the Lord. 20On the contrary:

‘If your enemy is hungry, feed him;

if he is thirsty, give him something to drink.

In doing this, you will heap burning coals on his head.’12:20 Prov. 25:21,22

21Do not be overcome by evil, but overcome evil with good.