Aroma 12 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 12:1-21

Nsembe za Moyo

1Nʼchifukwa chake ine ndikukupemphani abale, mwa chifundo cha Mulungu, kuti mupereke matupi anu monga nsembe yamoyo, yopatulika ndi yokondweretsa Mulungu. Nsembeyi ndiye kupembedza kwanu kwa uzimu. 2Musafanizidwenso ndi makhalidwe a dziko lino koma musandulike pokonzanso maganizo anu. Ndipo mudzadziwa ndi kuzindikira chifuniro chabwino cha Mulungu chomwe ndi chokondweretsa ndi changwiro.

3Chifukwa cha chisomo chopatsidwa kwa ine, ndinena kwa aliyense wa inu kuti musadziyenereze nokha kuposa mmene mulili. Koma mudziganizire nokha modzichepetsa, molingana ndi muyeso wa chikhulupiriro chimene Mulungu wakupatsani. 4Pakuti monga aliyense wa ife ali ndi thupi limodzi koma ziwalo zambiri, ziwalozi sizili ndi ntchito yofanana. 5Momwemonso mwa Khristu ife amene tili ambiri tipanga thupi limodzi ndipo chiwalo chilichonse ndi cholumikizika ku chinzake. 6Ife tili ndi mphatso zosiyana, molingana ndi chisomo chopatsidwa kwa ife. Ngati mphatso ya munthu ndi kunenera, musiyeni ayigwiritse ntchito molingana ndi chikhulupiriro chake. 7Ngati ndi kutumikira, musiyeni atumikire. Ngati ndi kuphunzitsa, musiyeni aphunzitse. 8Ngati ndi kulimbikitsa, musiyeni alimbikitse. Ngati ndi kupereka kuthandiza osowa, musiyeni apereke mowolowamanja. Ngati ndi utsogoleri, musiyeni alamulire mosamala. Ngati ndi kuonetsa chifundo, musiyeni achite mosangalala.

Chikondi

9Chikondi chikhale chopanda chinyengo. Dana nacho choyipa; gwiritsitsa chabwino. 10Mukondane kwathunthu monga abale. Lemekezanani wina ndi mnzake kuposa inu eni. 11Musakhale aulesi mʼmachitidwe anu. Khalani achangu mu mzimu ndipo tumikirani Ambuye. 12Kondwerani mʼchiyembekezo, pirirani mʼmasautso ndiponso khulupirikani mʼpemphero. 13Gawanani ndi anthu a Mulungu amene ali ndi chosowa. Cherezani alendo.

14Adalitseni amene akuzunzani. Adalitseni ndipo musawatemberere. 15Kondwani pamodzi ndi amene akukondwa ndipo lirani ndi amene akulira. 16Muyanjane wina ndi mnzake. Musakhale onyada, koma lolani kuyanjana ndi anthu wamba. Musaganize kuti mumadziwa zonse.

17Musabwezere choyipa ndi choyipa kwa aliyense. Samalitsani kuchita chabwino pamaso pa aliyense. 18Ngati nʼkotheka, khalani mwamtendere ndi aliyense monga momwe mungathere. 19Okondedwa anga, musabwezere choyipa, koma lekerani Mulungu. Pakuti kwalembedwa, “Kubwezera chilango nʼkwanga. Ndidzawalanga ndine,” akutero Ambuye. 20Koma,

“Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya.

Ngati ali ndi ludzu, mupatse kanthu kakumwa.

Pochita ichi, udzamuwunjikira makala amoto pamutu pake.”

21Musagonjetsedwe ndi choyipa, koma gonjetsani choyipa pochita chabwino.

Luganda Contemporary Bible

Abaruumi 12:1-21

Ssaddaaka Ennamu

112:1 a Bef 4:1 b Bar 6:13, 16, 19; 1Pe 2:5Noolwekyo abooluganda mbeegayirira olw’okusaasira kwa Katonda, muwengayo emibiri gyammwe nga ssaddaaka ennamu entukuvu esanyusa Katonda, kwe kuweereza kwammwe okw’omwoyo. 212:2 a 1Pe 1:14 b 1Yk 2:15 c Bef 4:23 d Bef 5:17So temwefaananyirizanga ba mirembe gino, naye mukyusibwe olw’okudda obuggya mu birowoozo byammwe okukakasibwa okusiimibwa kwa Katonda, okusanyusa era okw’amazima.

312:3 Bar 15:15; Bag 2:9; Bef 4:7Kubanga njogera olw’ekisa kye naweebwa, eri buli muntu mu mmwe, obuteerowooza okusinga ekyo ky’asaanidde okulowooza, naye okulowoozanga nga yeegendereza, nga Katonda bwe yagabira buli muntu ekigera ky’okukkiriza. 412:4 1Ko 12:12-14; Bef 4:16Kubanga nga bwe tulina ebitundu ebingi mu mubiri ogumu, ebitundu ebyo byonna bikola emirimu gya njawulo. 512:5 1Ko 10:17Noolwekyo nga bwe tuli omubiri ogumu mu Kristo, buli muntu kitundu ku mubiri ogumu ogwo. 612:6 a 1Ko 7:7; 12:4, 8-10 b 1Pe 4:10, 11Tulina ebirabo, ng’ekisa kye tulina bwe kyatuweebwa mu ngeri ey’enjawulo, oba bunnabbi, ng’ekigera ky’okukkiriza bwe kiri, 712:7 Bef 4:11oba buweereza, mu buweereza, oba omu okuyigiriza, mu kuyigiriza; 812:8 a Bik 15:32 b 2Ko 9:5-13oba omulala okugumya banne mu kubazzaamu amaanyi, oba omulala mu kugaba, oba omulala, okufuga n’obunyiikivu, n’omulala okulaga ekisa nga musanyufu.

Okwagala

912:9 1Ti 1:5Mube n’okwagala okutaliimu bukuusa. Mukyawenga ekibi, munywererenga ku kirungi, 1012:10 a Beb 13:1 b Baf 2:3nga mwagalana mu kwagala okw’abooluganda, nga muwaŋŋana ekitiibwa, 1112:11 Bik 18:25mu kunyiikira so si mu kugayaala. Musanyukirenga mu mwoyo nga muweereza Mukama, 1212:12 a Bar 5:2 b Beb 10:32, 36nga musanyukira mu kusuubira, nga mugumiikiriza mu kubonaabona era nga munyiikira mu kusaba. 1312:13 1Ti 3:2Mufengayo ku byetaago by’abantu ba Katonda, era mwanirizenga abagenyi.

1412:14 Mat 5:44Musabirenga ababayigganya; mubasabirenga so temubakolimiranga. 1512:15 Yob 30:25Musanyukirenga wamu n’abo abasanyuka, era mukaabirenga wamu n’abo abakaaba. 1612:16 a Bar 15:5 b Yer 45:5; Bar 11:25Buli muntu abeerenga mu mirembe muntu ne munne, nga temwegulumiza naye nga muba bakkakkamu. Temwekulumbazanga.

1712:17 a Nge 20:22 b 2Ko 8:21Temusasulanga kibi olw’ekibi, naye mukolenga birungi byereere eri bonna. 18Mukolenga kyonna ekisoboka okutabagana n’abantu bonna; 19abaagalwa, temuwalananga ggwanga, era ekiruyi mukirekere Katonda, nga bwe kyawandiikibwa nti, “Okuwoolera eggwanga kwange, nze ndisasula,” bw’ayogera Mukama. 20“Noolwekyo omulabe wo bw’alumwanga enjala, muliisenga; bw’alumwanga ennyonta muwenga ekyokunywa, bw’okola bw’otyo olimukumira amanda g’omuliro ku mutwe gwe.” 21Towangulwanga kibi, naye wangulanga ekibi ng’okola obulungi.