Amosi 9 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 9:1-15

Israeli Adzawonongedwa

1Ine ndinaona Ambuye atayima pambali pa guwa lansembe, ndipo anati:

“Kantha mitu ya nsanamira

kuti ziwundo za nyumba zigwedezeke.

Muzigwetsere pa mitu ya anthu onse,

onse amene atsalira ndidzawapha ndi lupanga.

Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzathawe,

palibe amene adzapulumuke.

2Ngakhale atakumba pansi mpaka ku malo a anthu akufa,

dzanja langa lidzawatulutsa kumeneko.

Ngakhale atakwera kumwamba

Ine ndidzawatsakamutsa kumeneko.

3Ngakhale atakabisala pamwamba pa phiri la Karimeli,

Ine ndidzawasaka kumeneko ndi kuwagwira.

Ngakhale atakabisala pansi pa nyanja yayikulu,

ndidzalamula njoka kuti iwalume kumeneko.

4Ngakhale adani awo awakusire ku ukapolo,

ndidzalamula lupanga kuti liwaphe kumeneko.

Ndidzawayangʼanitsitsa

kuti zoyipa ziwagwere; osati zabwino.”

5Ambuye Yehova Wamphamvuzonse

amene amakhudza dziko lapansi ndipo dzikolo limasungunuka,

onse amene amakhala mʼmenemo amalira.

Dziko lonse lidzadzaza ngati mtsinje wa Nailo,

kenaka nʼkuphwera ngati mtsinje wa ku Igupto.

6Iye amene amamanga malo ake okhalamo kumwamba,

ndi kuyika maziko ake pa dziko lapansi,

Iye amene amayitana madzi a ku nyanja

ndikuwakhuthulira pa dziko lapansi,

dzina lake ndiye Yehova.

7“Kodi kwa Ine, inu Aisraeli, simuli

chimodzimodzi ndi Akusi?”

Akutero Yehova.

“Kodi sindine amene ndinatulutsa Israeli ku Igupto,

Afilisti ku Kafitori

ndi Aaramu ku Kiri?

8“Taonani, maso a Ambuye Yehova

ali pa ufumu wochimwawu.

Ndidzawufafaniza

pa dziko lapansi.

Komabe sindidzawononga kotheratu

nyumba ya Yakobo,”

akutero Yehova.

9“Pakuti ndidzalamula,

ndipo ndidzagwedeza nyumba ya Israeli

pakati pa mitundu yonse ya anthu

monga momwe amasefera ufa mʼsefa,

koma palibe nʼkamwala kamodzi komwe kamene kadzagwe pansi.

10Anthu onse ochimwa pakati pa anthu anga

adzaphedwa ndi lupanga,

onse amene amanena kuti,

‘Tsoka silidzatigwera ife kapena kutiwononga.’

Kubwezeretsedwa kwa Israeli

11“Tsiku limenelo ndidzabwezeretsa

nyumba ya Davide imene inagwa.

Ndidzakonzanso malo amene anagumuka,

ndi kuyimanganso

monga inalili poyamba,

12kuti adzatengenso otsala a Edomu

ndi mitundu yonse imene imatchedwa ndi dzina langa,”

akutero Yehova amene adzachita zinthu izi.

13Yehova akunena kuti

“Nthawi ikubwera pamene mlimi wotipula adzapyola wokolola

ndipo woponda mphesa adzapyola wodzala mbewu.

Mapiri adzachucha vinyo watsopano

ndi kuyenderera pa zitunda zonse.

14Ndidzawabwezeranso pabwino anthu anga Aisraeli;

mizinda imene inali mabwinja idzamangidwanso ndipo azidzakhalamo.

Adzalima minda ya mpesa ndipo adzamwa vinyo wake;

adzalima minda ndipo adzadya zipatso zake.

15Ndidzakhazika Aisraeli mʼdziko mwawo,

ndipo sadzachotsedwamonso mʼdziko

limene Ine ndawapatsa,”

akutero Yehova Mulungu wako.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Amós 9:1-15

Quinta visión

1Vi al Señor de pie junto al altar, y él dijo:

«Golpea los capiteles de las columnas

para que se estremezcan los umbrales,

y que caigan en pedazos sobre sus cabezas.

A los que queden los mataré a espada.

Ni uno solo escapará,

ninguno saldrá con vida.

2Aunque se escondan en lo profundo del sepulcro,

de allí los sacará mi mano.

Aunque suban hasta el cielo,

de allí los derribaré.

3Aunque se oculten en la cumbre del Carmelo,

allí los buscaré y los atraparé.

Aunque de mí se escondan en el fondo del mar,

allí ordenaré a la serpiente que los muerda.

4Aunque vayan al destierro delante de sus enemigos,

allí ordenaré que los mate la espada.

Para mal, y no para bien,

fijaré en ellos mis ojos».

5El Señor omnipotente, el Todopoderoso,

toca la tierra, y ella se desmorona.

Sube y baja la tierra

como las aguas del Nilo, el río de Egipto,

y se enlutan todos los que en ella viven.

6Dios construye su excelso palacio en el cielo

y pone su cimiento9:6 excelso palacio … cimiento. Palabras de difícil traducción. en la tierra,

llama a las aguas del mar

y las derrama sobre la superficie de la tierra:

su nombre es el Señor.

7«Israelitas, ¿acaso vosotros

no me sois como cusitas?

¿Acaso no saqué de Egipto a Israel,

de Creta9:7 Creta. Lit. Caftor. a los filisteos

y de Quir a los sirios?

—afirma el Señor—.

8Por eso los ojos del Señor omnipotente

están sobre este reino pecaminoso.

Borraré de la faz de la tierra a los descendientes de Jacob,

aunque no del todo

—afirma el Señor—.

9Daré la orden de zarandear al pueblo de Israel

entre todas las naciones,

como se zarandea la arena en una criba,

sin que caiga a tierra ni una sola piedra.

10Morirán a filo de espada

todos los pecadores de mi pueblo,

todos los que dicen:

“No nos alcanzará la calamidad;

¡jamás se nos acercará!”

Restauración de Israel

11»En aquel día levantaré

la choza caída de David.

Repararé sus grietas,

restauraré sus ruinas

y la reconstruiré tal como era en días pasados,

12para que ellos posean el remanente de Edom

y todas las naciones que llevan mi nombre

—afirma el Señor,

que hará estas cosas—.

13»Vienen días —afirma el Señor—,

»en los cuales el que ara alcanzará al segador

y el que pisa las uvas, al sembrador.

Los montes destilarán vino dulce,

el cual correrá por todas las colinas.

14Restauraré a9:14 Restauraré a. Alt. Haré volver a los cautivos de. mi pueblo Israel;

ellos reconstruirán las ciudades arruinadas

y vivirán en ellas.

Plantarán viñedos y beberán su vino;

cultivarán huertos y comerán sus frutos.

15Plantaré a Israel en su propia tierra,

para que nunca más sea arrancado

de la tierra que yo le di»,

dice el Señor tu Dios.