Amosi 9 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 9:1-15

Israeli Adzawonongedwa

1Ine ndinaona Ambuye atayima pambali pa guwa lansembe, ndipo anati:

“Kantha mitu ya nsanamira

kuti ziwundo za nyumba zigwedezeke.

Muzigwetsere pa mitu ya anthu onse,

onse amene atsalira ndidzawapha ndi lupanga.

Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzathawe,

palibe amene adzapulumuke.

2Ngakhale atakumba pansi mpaka ku malo a anthu akufa,

dzanja langa lidzawatulutsa kumeneko.

Ngakhale atakwera kumwamba

Ine ndidzawatsakamutsa kumeneko.

3Ngakhale atakabisala pamwamba pa phiri la Karimeli,

Ine ndidzawasaka kumeneko ndi kuwagwira.

Ngakhale atakabisala pansi pa nyanja yayikulu,

ndidzalamula njoka kuti iwalume kumeneko.

4Ngakhale adani awo awakusire ku ukapolo,

ndidzalamula lupanga kuti liwaphe kumeneko.

Ndidzawayangʼanitsitsa

kuti zoyipa ziwagwere; osati zabwino.”

5Ambuye Yehova Wamphamvuzonse

amene amakhudza dziko lapansi ndipo dzikolo limasungunuka,

onse amene amakhala mʼmenemo amalira.

Dziko lonse lidzadzaza ngati mtsinje wa Nailo,

kenaka nʼkuphwera ngati mtsinje wa ku Igupto.

6Iye amene amamanga malo ake okhalamo kumwamba,

ndi kuyika maziko ake pa dziko lapansi,

Iye amene amayitana madzi a ku nyanja

ndikuwakhuthulira pa dziko lapansi,

dzina lake ndiye Yehova.

7“Kodi kwa Ine, inu Aisraeli, simuli

chimodzimodzi ndi Akusi?”

Akutero Yehova.

“Kodi sindine amene ndinatulutsa Israeli ku Igupto,

Afilisti ku Kafitori

ndi Aaramu ku Kiri?

8“Taonani, maso a Ambuye Yehova

ali pa ufumu wochimwawu.

Ndidzawufafaniza

pa dziko lapansi.

Komabe sindidzawononga kotheratu

nyumba ya Yakobo,”

akutero Yehova.

9“Pakuti ndidzalamula,

ndipo ndidzagwedeza nyumba ya Israeli

pakati pa mitundu yonse ya anthu

monga momwe amasefera ufa mʼsefa,

koma palibe nʼkamwala kamodzi komwe kamene kadzagwe pansi.

10Anthu onse ochimwa pakati pa anthu anga

adzaphedwa ndi lupanga,

onse amene amanena kuti,

‘Tsoka silidzatigwera ife kapena kutiwononga.’

Kubwezeretsedwa kwa Israeli

11“Tsiku limenelo ndidzabwezeretsa

nyumba ya Davide imene inagwa.

Ndidzakonzanso malo amene anagumuka,

ndi kuyimanganso

monga inalili poyamba,

12kuti adzatengenso otsala a Edomu

ndi mitundu yonse imene imatchedwa ndi dzina langa,”

akutero Yehova amene adzachita zinthu izi.

13Yehova akunena kuti

“Nthawi ikubwera pamene mlimi wotipula adzapyola wokolola

ndipo woponda mphesa adzapyola wodzala mbewu.

Mapiri adzachucha vinyo watsopano

ndi kuyenderera pa zitunda zonse.

14Ndidzawabwezeranso pabwino anthu anga Aisraeli;

mizinda imene inali mabwinja idzamangidwanso ndipo azidzakhalamo.

Adzalima minda ya mpesa ndipo adzamwa vinyo wake;

adzalima minda ndipo adzadya zipatso zake.

15Ndidzakhazika Aisraeli mʼdziko mwawo,

ndipo sadzachotsedwamonso mʼdziko

limene Ine ndawapatsa,”

akutero Yehova Mulungu wako.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

阿摩司書 9:1-15

耶和華的審判

1我看見主站在祭壇旁,祂說:

「要擊打柱頂,使殿的根基震動;

要打碎柱頂,使殿宇坍塌壓死眾人。

僥倖生還的,我要用刀劍殺掉,

沒有一個能逃脫,沒有一個能倖免。

2即使他們挖洞鑽進陰間,

我也要把他們揪出來;

即使他們爬上高天,

我也要把他們拉下來;

3即使他們藏在迦密山的峰頂,

我也要去搜尋,捉住他們;

即使他們潛到海底,

我也要派海蛇去吞咬他們;

4即使他們被敵人擄去,

我也要命刀劍追殺他們。

我要定睛在他們身上,

不是要賜福而是要降禍。」

5主——萬軍之耶和華觸摸大地,

大地就消融,地上的人都要哀號;

大地如埃及尼羅河漲起退落。

6那位在天上建造樓閣,

在大地之上立定穹蒼,

召來海水澆在大地上的——

祂的名字是耶和華。

7耶和華說:

以色列人啊,

在我眼中,你們不是和古實人一樣嗎?

我不是領你們出埃及

也領非利士人出迦斐托9·7 迦斐托」即克里特島。

亞蘭人出吉珥嗎?

8主耶和華的眼目察看這罪惡的國家,

我要從地上除滅它,

但不會完全毀滅雅各家。

這是耶和華說的。

9「因為我要下令在列國中篩以色列家,

就像人篩穀物,一粒石子也不會落在地上。

10在我的子民中,

所有誇口說『災禍不會追上我們,也不會迎面而來』的罪人,

都要死在刀下。

以色列的復興

11「到那日,

我要重建已傾覆的大衛王朝,

修補它城牆的缺口。

我要從廢墟中重建它,

恢復它往日的榮耀。

12這樣,以色列人必擁有以東所剩的和所有屬於我名下的國家。

這是要成就這事的耶和華說的。」

13耶和華說:

「時候將到,

五穀還未收完又該耕種了,

葡萄還未踩完又該栽種了。

甜酒從群山上滴下,在丘嶺間流淌。

14我要使我被擄的以色列子民返回故鄉,

他們要重建廢城並住在城中,

栽種葡萄園,喝園中釀出的美酒,

整理園圃,吃園中出產的佳果。

15我要將以色列人栽種在他們自己的土地上,

永不再從我賜給他們的土地上拔除他們。」

這是你們的上帝耶和華說的。