Amosi 9 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 9:1-15

Israeli Adzawonongedwa

1Ine ndinaona Ambuye atayima pambali pa guwa lansembe, ndipo anati:

“Kantha mitu ya nsanamira

kuti ziwundo za nyumba zigwedezeke.

Muzigwetsere pa mitu ya anthu onse,

onse amene atsalira ndidzawapha ndi lupanga.

Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzathawe,

palibe amene adzapulumuke.

2Ngakhale atakumba pansi mpaka ku malo a anthu akufa,

dzanja langa lidzawatulutsa kumeneko.

Ngakhale atakwera kumwamba

Ine ndidzawatsakamutsa kumeneko.

3Ngakhale atakabisala pamwamba pa phiri la Karimeli,

Ine ndidzawasaka kumeneko ndi kuwagwira.

Ngakhale atakabisala pansi pa nyanja yayikulu,

ndidzalamula njoka kuti iwalume kumeneko.

4Ngakhale adani awo awakusire ku ukapolo,

ndidzalamula lupanga kuti liwaphe kumeneko.

Ndidzawayangʼanitsitsa

kuti zoyipa ziwagwere; osati zabwino.”

5Ambuye Yehova Wamphamvuzonse

amene amakhudza dziko lapansi ndipo dzikolo limasungunuka,

onse amene amakhala mʼmenemo amalira.

Dziko lonse lidzadzaza ngati mtsinje wa Nailo,

kenaka nʼkuphwera ngati mtsinje wa ku Igupto.

6Iye amene amamanga malo ake okhalamo kumwamba,

ndi kuyika maziko ake pa dziko lapansi,

Iye amene amayitana madzi a ku nyanja

ndikuwakhuthulira pa dziko lapansi,

dzina lake ndiye Yehova.

7“Kodi kwa Ine, inu Aisraeli, simuli

chimodzimodzi ndi Akusi?”

Akutero Yehova.

“Kodi sindine amene ndinatulutsa Israeli ku Igupto,

Afilisti ku Kafitori

ndi Aaramu ku Kiri?

8“Taonani, maso a Ambuye Yehova

ali pa ufumu wochimwawu.

Ndidzawufafaniza

pa dziko lapansi.

Komabe sindidzawononga kotheratu

nyumba ya Yakobo,”

akutero Yehova.

9“Pakuti ndidzalamula,

ndipo ndidzagwedeza nyumba ya Israeli

pakati pa mitundu yonse ya anthu

monga momwe amasefera ufa mʼsefa,

koma palibe nʼkamwala kamodzi komwe kamene kadzagwe pansi.

10Anthu onse ochimwa pakati pa anthu anga

adzaphedwa ndi lupanga,

onse amene amanena kuti,

‘Tsoka silidzatigwera ife kapena kutiwononga.’

Kubwezeretsedwa kwa Israeli

11“Tsiku limenelo ndidzabwezeretsa

nyumba ya Davide imene inagwa.

Ndidzakonzanso malo amene anagumuka,

ndi kuyimanganso

monga inalili poyamba,

12kuti adzatengenso otsala a Edomu

ndi mitundu yonse imene imatchedwa ndi dzina langa,”

akutero Yehova amene adzachita zinthu izi.

13Yehova akunena kuti

“Nthawi ikubwera pamene mlimi wotipula adzapyola wokolola

ndipo woponda mphesa adzapyola wodzala mbewu.

Mapiri adzachucha vinyo watsopano

ndi kuyenderera pa zitunda zonse.

14Ndidzawabwezeranso pabwino anthu anga Aisraeli;

mizinda imene inali mabwinja idzamangidwanso ndipo azidzakhalamo.

Adzalima minda ya mpesa ndipo adzamwa vinyo wake;

adzalima minda ndipo adzadya zipatso zake.

15Ndidzakhazika Aisraeli mʼdziko mwawo,

ndipo sadzachotsedwamonso mʼdziko

limene Ine ndawapatsa,”

akutero Yehova Mulungu wako.

Bibelen på hverdagsdansk

Amosʼ Bog 9:1-15

Israel rammes af Guds straf, men en rest bliver reddet

1Derpå så jeg i et syn Herren stå ved siden af alteret og give følgende befaling: „Slå på søjlehovederne, så afgudstemplet styrter sammen og murbrokkerne knuser alle i nærheden. Resten vil falde i krig. Ingen slipper bort. 2Hvis de kunne flygte ned i dødsriget, kunne jeg stadig hente dem op. Hvis de kunne stige op til himlen, kunne jeg stadig hente dem ned. 3Hvis de prøver at gemme sig i Karmelbjergets klippehuler, skal jeg nok finde dem. Hvis de kunne søge tilflugt på havets bund, ville jeg befale havuhyret at fortære dem. 4Selv hvis de føres i eksil, vil jeg give befaling om, at de skal dræbes dér. Jeg holder øje med dem overalt, men det er for at straffe dem, ikke for at redde dem.”

5Når Herren, den Almægtige, sender et jordskælv, vil alle, som bor i landet, fyldes af rædsel. Jorden vil hæve sig og synke ned igen som Egyptens flod. 6Herrens bolig har sit fundament på jorden, men den rækker ind i Himlen. Han opsamler vandet fra havet og lader det falde ned på jorden. Herren er hans navn.

7Han siger: „Israels folk, tror I, at I er bedre end kushitterne? Jeg førte jer ud af Egypten, men jeg førte også filistrene ud af Kaftor og aramæerne ud af Kir.

8Jeg har fæstet blikket på denne oprørske nation og vil fjerne den fra jordens overflade. Dog vil jeg ikke fuldstændigt udrydde Jakobs efterkommere. 9Jeg har besluttet at sigte Israels folk i deres eksil og fjerne alt det værdiløse. 10Alle selvsikre syndere skal falde for sværdet.

Davids rige skal genrejses

11Til sin tid vil jeg genopbygge Davids rige. Jeg vil udbedre skaderne, genopbygge det, som blev revet ned, og få det op at stå igen, så det bliver som før. 12Derefter skal Israels folk overtage resterne af Edom og de andre folkeslag, som også tilhører mig.” Det er Herren, der siger det, og han vil gøre det.

13Herren siger: „Engang bliver der igen fremgang og frugtbarhed, så man ikke bliver færdig med at høste, før det er tid til at pløje, og så man ikke bliver færdig med at presse druerne, før det er tid til at plante. Bjergskråningerne vil dryppe af druernes saft. 14Jeg vil sætte mit folk, Israel, fri af fangenskabet. Da skal de genopbygge deres ødelagte byer og flytte ind i dem. De skal plante vingårde og drikke vinen derfra. De skal anlægge haver og nyde frugten deraf. 15Jeg planter dem tilbage i deres land. Aldrig mere skal de rykkes op fra det land, jeg har givet dem.” Herren, Israels Gud, har talt!