Amosi 7 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 7:1-17

Dzombe, Moto ndi Chingwe Chowongolera Khoma

1Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Yehova ankasonkhanitsa gulu la dzombe nthawi imene gawo la zokolola za mfumu linali litakololedwa kale ndipo mbewu zachiwiri zinali zitangoyamba kumera kumene. 2Dzombelo litadya zomera zonse za mʼdzikomo, Ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, khululukani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”

3Kotero Yehova anakhululuka.

Yehovayo anati, “Izi sizidzachitika.”

4Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Ambuye Yehova ankayitana malawi a moto kuti alange anthu. Motowo unawumitsa nyanja yakuya ndi kupsereza dziko. 5Tsono ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, chonde ndikukupemphani, lekani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”

6Kotero Yehova anakhululuka.

Ambuye Yehova anati, “Izinso sizidzachitika.”

7Zimene Iye anandionetsa ndi izi: Ambuye anayima pambali pa khoma lomangamanga, mʼmanja mwake muli chingwe chowongolera khoma. 8Ndipo Ambuye anandifunsa kuti, “Amosi, nʼchiyani ukuonachi?”

Ine ndinayankha kuti, “Chingwe chowongolera khoma.”

Ndipo Yehova anati, “Taona, Ine ndikuyika chingwe chowongolerachi pakati pa anthu anga, Aisraeli; sindidzawalekereranso.

9“Malo achipembedzo a Isake adzawonongedwa

ndipo malo opatulika a Israeli adzasanduka bwinja;

ndidzagwetsa nyumba ya Yeroboamu ndi lupanga langa.”

Amosi ndi Amaziya

10Pamenepo Amaziya wansembe wa ku Beteli anatumiza uthenga kwa Yeroboamu mfumu ya Israeli kuti, “Amosi akukuutsirani chiwembu pakati pa Aisraeli. Dziko silingalekerere zonena zake zonsezo. 11Pakuti zimene Amosi akunena ndi izi:

“ ‘Yeroboamu adzaphedwa ndi lupanga,

ndipo Israeli adzapita ndithu ku ukapolo,

kutali ndi dziko lake.’ ”

12Ndipo Amaziya anawuza Amosi kuti, “Choka, mlosi iwe! Bwerera ku dziko la Yuda. Uzikalosera kumeneko ndipo anthu a kumeneko azikakudyetsa. 13Usanenerenso ku Beteli, chifukwa kumeneko ndi malo opatulika a mfumu ndiponso ndi malo a nyumba yachipembedzo yaufumu.”

14Amosi anayankha Amaziya kuti, “Ine sindine mneneri kapena mwana wa mneneri; koma ndine woweta ziweto, ndiponso mlimi wa nkhuyu. 15Koma Yehova ananditenga ndikuweta nkhosa ndipo anati, ‘Pita ukanenere kwa anthu anga Aisraeli.’ 16Tsono imva mawu a Yehova. Iwe ukunena kuti,

“ ‘Usanenere zotsutsa Israeli,

ndipo siya kulalikira motsutsa nyumba ya Isake.’ ”

17“Tsono zimene akunena Yehova ndi izi:

“ ‘Mkazi wako adzasanduka wachiwerewere mu mzindamu,

ndipo ana ako aamuna ndi aakazi adzaphedwa ndi lupanga.

Munda wako udzayezedwa ndi chingwe ndi kugawidwa,

ndipo iwe mwini udzafera mʼdziko la anthu osapembedza Mulungu.

Ndipo Israeli adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo,

kutali ndi dziko lake.’ ”

King James Version

Amos 7:1-17

1Thus hath the Lord GOD shewed unto me; and, behold, he formed grasshoppers in the beginning of the shooting up of the latter growth; and, lo, it was the latter growth after the king’s mowings.7.1 grasshoppers: or, green worms 2And it came to pass, that when they had made an end of eating the grass of the land, then I said, O Lord GOD, forgive, I beseech thee: by whom shall Jacob arise? for he is small.7.2 by…: or, who of (or, for,) Jacob shall stand? 3The LORD repented for this: It shall not be, saith the LORD.

4¶ Thus hath the Lord GOD shewed unto me: and, behold, the Lord GOD called to contend by fire, and it devoured the great deep, and did eat up a part. 5Then said I, O Lord GOD, cease, I beseech thee: by whom shall Jacob arise? for he is small.7.5 by…: or, who of (or, for,) Jacob shall stand? 6The LORD repented for this: This also shall not be, saith the Lord GOD.

7¶ Thus he shewed me: and, behold, the Lord stood upon a wall made by a plumbline, with a plumbline in his hand. 8And the LORD said unto me, Amos, what seest thou? And I said, A plumbline. Then said the Lord, Behold, I will set a plumbline in the midst of my people Israel: I will not again pass by them any more: 9And the high places of Isaac shall be desolate, and the sanctuaries of Israel shall be laid waste; and I will rise against the house of Jeroboam with the sword.

10¶ Then Amaziah the priest of Beth-el sent to Jeroboam king of Israel, saying, Amos hath conspired against thee in the midst of the house of Israel: the land is not able to bear all his words. 11For thus Amos saith, Jeroboam shall die by the sword, and Israel shall surely be led away captive out of their own land. 12Also Amaziah said unto Amos, O thou seer, go, flee thee away into the land of Judah, and there eat bread, and prophesy there: 13But prophesy not again any more at Beth-el: for it is the king’s chapel, and it is the king’s court.7.13 chapel: or, sanctuary7.13 king’s court: Heb. house of the kingdom

14¶ Then answered Amos, and said to Amaziah, I was no prophet, neither was I a prophet’s son; but I was an herdman, and a gatherer of sycomore fruit:7.14 sycomore…: or, wild figs 15And the LORD took me as I followed the flock, and the LORD said unto me, Go, prophesy unto my people Israel.7.15 as…: Heb. from behind

16¶ Now therefore hear thou the word of the LORD: Thou sayest, Prophesy not against Israel, and drop not thy word against the house of Isaac. 17Therefore thus saith the LORD; Thy wife shall be an harlot in the city, and thy sons and thy daughters shall fall by the sword, and thy land shall be divided by line; and thou shalt die in a polluted land: and Israel shall surely go into captivity forth of his land.