Mboni Zotsutsa Israeli
1Inu Aisraeli, imvani mawu awa amene Yehova wayankhula kutsutsana nanu, kutsutsana ndi banja lonse limene analitulutsa mu Igupto:
2“Inu nokha ndi amene ndinakusankhani
pakati pa mabanja onse a dziko lapansi;
nʼchifukwa chake ndidzakulangani
chifukwa cha machimo anu onse.”
3Kodi anthu awiri nʼkuyendera limodzi
asanapangane?
4Kodi mkango umabangula mʼnkhalango
usanagwire nyama?
Kodi msona wamkango umalira mʼphanga mwake
pamene sunagwire kanthu?
5Kodi mbalame nʼkutera pa msampha
pamene palibe nyambo yake?
Kodi msampha umafwamphuka
usanakole kanthu?
6Kodi pamene lipenga la nkhondo lalira mu mzinda,
anthu sanjenjemera?
Pamene tsoka lafika mu mzinda,
kodi si Yehova amene wachititsa zimenezo?
7Zoonadi Ambuye Yehova sachita kanthu
asanawulule zimene akufuna kuchita
kwa atumiki ake, aneneri.
8Mkango wabangula,
ndani amene sachita mantha?
Ambuye Yehova wayankhula,
ndani amene sanganenere?
9Lengezani zimenezi ku nyumba zaufumu za ku Asidodi
ndiponso ku nyumba zaufumu za ku Igupto:
“Sonkhanani ku mapiri a ku Samariya;
onani chisokonezo pakati pake
ndiponso kuponderezana pakati pa anthu ake.”
10“Iwo sadziwa kuchita zolungama,
ndipo amadzaza malo awo otetezedwa ndi zinthu zolanda ku nkhondo ndi zakuba,” akutero Yehova.
11Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akunena izi:
“Mdani adzalizungulira dzikoli;
iye adzagwetsa malinga ako,
ndi kufunkha nyumba zako zaufumu.”
12Yehova akuti,
“Monga mʼbusa amalanditsa mʼkamwa mwa mkango
miyendo iwiri yokha kapena msonga yokha ya khutu,
moteronso ndimo mmene adzapulumukire Aisraeli
amene amakhala mu Samariya
pa msonga za mabedi awo,
ndi ku Damasiko pa akakhutagona awo.”
13“Imvani izi ndipo mupereke umboni wotsutsa nyumba ya Yakobo,” akutero Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
14“Pa tsiku limene ndidzalange Israeli chifukwa cha machimo ake,
ndidzagumula maguwa ansembe a ku Beteli;
nyanga za guwa zidzathyoka
ndipo zidzagwa pansi.
15Ndidzagwetsa nyumba ya pa nthawi yozizira
pamodzi ndi nyumba ya pa nthawi yotentha;
nyumba zokongoletsedwa ndi minyanga ya njovu zidzawonongedwa
ndipo nyumba zikuluzikulu zidzaphwasulidwa,”
akutero Yehova.
Testemunhas Convocadas para Acusar Israel
1Ouçam esta palavra que o Senhor falou contra vocês, ó israelitas; contra toda esta família que tirei do Egito:
2“Escolhi apenas vocês
de todas as famílias da terra;
por isso eu os castigarei
por todas as suas maldades”.
3Duas pessoas andarão juntas
se não estiverem de acordo3.3 Ou tiverem combinado?
4O leão ruge na floresta
se não apanhou presa alguma?
O leão novo ruge em sua toca
se nada caçou?
5Cai o pássaro numa armadilha
que não foi armada?
Será que a armadilha se desarma
se nada foi apanhado?
6Quando a trombeta toca na cidade,
o povo não treme?
Ocorre alguma desgraça na cidade
sem que o Senhor a tenha mandado?
7Certamente o Senhor, o Soberano,
não faz coisa alguma
sem revelar o seu plano
aos seus servos, os profetas.
8O leão rugiu,
quem não temerá?
O Senhor, o Soberano, falou,
quem não profetizará?
9Proclamem nos palácios de Asdode3.9 A Septuaginta diz da Assíria. e do Egito:
“Reúnam-se nos montes de Samaria
para verem o grande tumulto que há ali,
e a opressão no meio do seu povo”.
10“Eles não sabem agir com retidão”,
declara o Senhor,
“eles, que acumulam em seus palácios
o que roubaram e saquearam”.
11Portanto, assim diz o Senhor, o Soberano:
“Um inimigo cercará o país.
Ele derrubará as suas fortalezas
e saqueará os seus palácios”.
12Assim diz o Senhor:
“Assim como o pastor livra a ovelha,
arrancando da boca do leão só dois ossos da perna
ou um pedaço da orelha,
assim serão arrancados os israelitas de Samaria,
com a ponta de uma cama
e um pedaço de sofá3.12 Ou uma capa de sofá; ou ainda uma almofada de Damasco.
13“Ouçam isto e testemunhem contra a descendência de Jacó”, declara o Senhor, o Soberano, o Deus dos Exércitos.
14“No dia em que eu castigar Israel
por causa dos seus pecados,
destruirei os altares de Betel;
as pontas do altar serão cortadas e cairão no chão.
15Derrubarei a casa de inverno
junto com a casa de verão;
as casas enfeitadas de marfim serão destruídas,
e as mansões desaparecerão”,
declara o Senhor.