Mboni Zotsutsa Israeli
1Inu Aisraeli, imvani mawu awa amene Yehova wayankhula kutsutsana nanu, kutsutsana ndi banja lonse limene analitulutsa mu Igupto:
2“Inu nokha ndi amene ndinakusankhani
pakati pa mabanja onse a dziko lapansi;
nʼchifukwa chake ndidzakulangani
chifukwa cha machimo anu onse.”
3Kodi anthu awiri nʼkuyendera limodzi
asanapangane?
4Kodi mkango umabangula mʼnkhalango
usanagwire nyama?
Kodi msona wamkango umalira mʼphanga mwake
pamene sunagwire kanthu?
5Kodi mbalame nʼkutera pa msampha
pamene palibe nyambo yake?
Kodi msampha umafwamphuka
usanakole kanthu?
6Kodi pamene lipenga la nkhondo lalira mu mzinda,
anthu sanjenjemera?
Pamene tsoka lafika mu mzinda,
kodi si Yehova amene wachititsa zimenezo?
7Zoonadi Ambuye Yehova sachita kanthu
asanawulule zimene akufuna kuchita
kwa atumiki ake, aneneri.
8Mkango wabangula,
ndani amene sachita mantha?
Ambuye Yehova wayankhula,
ndani amene sanganenere?
9Lengezani zimenezi ku nyumba zaufumu za ku Asidodi
ndiponso ku nyumba zaufumu za ku Igupto:
“Sonkhanani ku mapiri a ku Samariya;
onani chisokonezo pakati pake
ndiponso kuponderezana pakati pa anthu ake.”
10“Iwo sadziwa kuchita zolungama,
ndipo amadzaza malo awo otetezedwa ndi zinthu zolanda ku nkhondo ndi zakuba,” akutero Yehova.
11Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akunena izi:
“Mdani adzalizungulira dzikoli;
iye adzagwetsa malinga ako,
ndi kufunkha nyumba zako zaufumu.”
12Yehova akuti,
“Monga mʼbusa amalanditsa mʼkamwa mwa mkango
miyendo iwiri yokha kapena msonga yokha ya khutu,
moteronso ndimo mmene adzapulumukire Aisraeli
amene amakhala mu Samariya
pa msonga za mabedi awo,
ndi ku Damasiko pa akakhutagona awo.”
13“Imvani izi ndipo mupereke umboni wotsutsa nyumba ya Yakobo,” akutero Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
14“Pa tsiku limene ndidzalange Israeli chifukwa cha machimo ake,
ndidzagumula maguwa ansembe a ku Beteli;
nyanga za guwa zidzathyoka
ndipo zidzagwa pansi.
15Ndidzagwetsa nyumba ya pa nthawi yozizira
pamodzi ndi nyumba ya pa nthawi yotentha;
nyumba zokongoletsedwa ndi minyanga ya njovu zidzawonongedwa
ndipo nyumba zikuluzikulu zidzaphwasulidwa,”
akutero Yehova.
Сведоци против Израиља
1Чујте ову реч, јер Господ против вас говори, децо Израиљева. Говори против вас и свег рода који сам извео из египатске земље:
2„Само сам вас познавао
више од свих родова на земљи.
Зато ћу вас и казнити
за све ваше кривице.“
3Иду ли двоје заједно,
а да се нису срели?
4Риче ли лав у шуми
ако нема плена?
Јавља ли се риком лавић из брлога свога,
ако није нешто ухватио?
5Слеће ли птица у замку на тле,
ако нема мамца?
Склања ли се птичија замка са тла,
ако ништа ухваћено није?
6Огласи ли се труба у граду,
а да народ не задрхти?
Зар постоји несрећа у граду,
а да није од Господа?
7Јер Господ не чини ништа,
а да тајну своју не објави пророцима,
слугама својим.
8Зарикао је лав!
И ко да се не препадне?!
Проговорио је Господ Бог!
И ко да не пророкује?!
9Објавите по утврђењима у Азоту
и по утврђењима египатске земље.
Реците: „Саберите се по брдима Самарије,
гледајте велике немире сред ње
и насиље у њој.“
10„Нису знали добро да чине – говори Господ –
ти што згрћу насиљем
и пустошењем по својим утврђењима.“
11Зато овако каже Господ Бог:
„Непријатељ је око земље,
снагу ће твоју да обори,
оплениће твоја утврђења.“
12Овако каже Господ:
„Као када пастир истргне из лављих чељусти
пар ногу или комад ува,
тако ће истргнути децу Израиљеву
која у Самарији пребивају на углу постеље,
на свиленом кревету.
13Чуј и сведочи дому Јаковљевом, говори Господ, Господ Бог над војскама:
14На дан када казним Израиљ за преступе његове
казнићу и жртвенике Ветиља.
Одсеће се рогови жртвеника
и попадаће на тле.
15И зимску и летњу ћу кућу ударити.
Срушиће се куће пуне слоноваче
и многи ће домови бити збрисани
– говори Господ.“