Amosi 3 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 3:1-15

Mboni Zotsutsa Israeli

1Inu Aisraeli, imvani mawu awa amene Yehova wayankhula kutsutsana nanu, kutsutsana ndi banja lonse limene analitulutsa mu Igupto:

2“Inu nokha ndi amene ndinakusankhani

pakati pa mabanja onse a dziko lapansi;

nʼchifukwa chake ndidzakulangani

chifukwa cha machimo anu onse.”

3Kodi anthu awiri nʼkuyendera limodzi

asanapangane?

4Kodi mkango umabangula mʼnkhalango

usanagwire nyama?

Kodi msona wamkango umalira mʼphanga mwake

pamene sunagwire kanthu?

5Kodi mbalame nʼkutera pa msampha

pamene palibe nyambo yake?

Kodi msampha umafwamphuka

usanakole kanthu?

6Kodi pamene lipenga la nkhondo lalira mu mzinda,

anthu sanjenjemera?

Pamene tsoka lafika mu mzinda,

kodi si Yehova amene wachititsa zimenezo?

7Zoonadi Ambuye Yehova sachita kanthu

asanawulule zimene akufuna kuchita

kwa atumiki ake, aneneri.

8Mkango wabangula,

ndani amene sachita mantha?

Ambuye Yehova wayankhula,

ndani amene sanganenere?

9Lengezani zimenezi ku nyumba zaufumu za ku Asidodi

ndiponso ku nyumba zaufumu za ku Igupto:

“Sonkhanani ku mapiri a ku Samariya;

onani chisokonezo pakati pake

ndiponso kuponderezana pakati pa anthu ake.”

10“Iwo sadziwa kuchita zolungama,

ndipo amadzaza malo awo otetezedwa ndi zinthu zolanda ku nkhondo ndi zakuba,” akutero Yehova.

11Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akunena izi:

“Mdani adzalizungulira dzikoli;

iye adzagwetsa malinga ako,

ndi kufunkha nyumba zako zaufumu.”

12Yehova akuti,

“Monga mʼbusa amalanditsa mʼkamwa mwa mkango

miyendo iwiri yokha kapena msonga yokha ya khutu,

moteronso ndimo mmene adzapulumukire Aisraeli

amene amakhala mu Samariya

pa msonga za mabedi awo,

ndi ku Damasiko pa akakhutagona awo.”

13“Imvani izi ndipo mupereke umboni wotsutsa nyumba ya Yakobo,” akutero Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.

14“Pa tsiku limene ndidzalange Israeli chifukwa cha machimo ake,

ndidzagumula maguwa ansembe a ku Beteli;

nyanga za guwa zidzathyoka

ndipo zidzagwa pansi.

15Ndidzagwetsa nyumba ya pa nthawi yozizira

pamodzi ndi nyumba ya pa nthawi yotentha;

nyumba zokongoletsedwa ndi minyanga ya njovu zidzawonongedwa

ndipo nyumba zikuluzikulu zidzaphwasulidwa,”

akutero Yehova.

Luganda Contemporary Bible

Amosi 3:1-15

Okulabula Abantu ba Isirayiri

13:1 Am 2:10Muwulire ekigambo kino Mukama ky’aboogerako mmwe abaana ba Isirayiri, ennyumba yonna gye naggya mu Misiri.

23:2 a Ma 7:6; Luk 12:47 b Yer 14:10“Mu bantu bonna abali ku nsi,

mmwe mwekka be nalonda.

Kyendiva mbabonereza

olw’ebibi byammwe byonna.”

3Abantu ababiri bayinza okutambulira awamu

wabula nga bakkiriziganyizza?

43:4 Zab 104:21; Kos 5:14Empologoma ewulugumira mu kisaka

nga terina muyiggo?

Empologoma ento ekaabira mu mpuku yaayo

nga teriiko ky’ekutte?

5Akanyonyi kayinza okugwa mu mutego

nga tewali kikasikirizza?

Omutego gumasuka

nga teguliiko kye gukwasizza?

63:6 Is 14:24-27; 45:7Akagombe kavugira mu kibuga

abantu ne batatya?

Akabenje kagwa mu kibuga

nga Mukama si y’akaleese?

73:7 a Lub 18:17; Dan 9:22; Yk 15:15; Kub 10:7 b Yer 23:22Naye ddala Mukama Katonda takola kintu kyonna

nga tasoose kukibikkulira

baweereza be, bannabbi.

83:8 Yer 20:9; Yon 1:1-3; 3:1-3; Bik 4:20Empologoma ewulugumye,

ani ataatye?

Mukama Katonda ayogedde

ani ataawe bubaka bwe?

93:9 Am 4:1; 6:1Langirira eri ebigo by’e Asudodi

n’eri ebigo by’e Misiri nti,

“Mujje mukuŋŋaanire ku nsozi z’e Samaliya

mulabe akajagalalo akanene akali eyo

n’abantu be nga bwe bajoogebwa.”

103:10 a Yer 4:22; Am 5:7; 6:12 b Zef 1:9 c Kbk 2:8Mukama agamba nti, “Abantu abajjuzza

ebigo byabwe n’ebintu ebinyage,

tebamanyi kukola kituufu.”

113:11 Am 2:5; 6:14Noolwekyo bw’ati bw’ayogera Mukama Katonda nti,

“Omulabe alirumba ensi,

n’amenyaamenya ebigo byo eby’amaanyi

era n’abinyagulula.”

123:12 a 1Sa 17:34 b Am 6:4Bw’ati bw’ayogera Mukama nti,

“Ng’omusumba bw’agezaako okutaasa endiga ye okuva mu kamwa k’empologoma

n’asikayo amagulu abiri obubiri n’ekitundu ky’okutu,

bwe batyo Abayisirayiri bwe balinunulibwa,

abo abatuula mu Samaliya

ku nkomerero y’ebitanda byabwe

ne ku bitanda byabwe mu Ddamasiko.

133:13 Ez 2:7“Muwulirize kino era mulumirize enju ya Yakobo yonna,” bw’ayogera Mukama Katonda Ayinzabyonna.

143:14 Am 5:5-6“Ku lunaku lwe lumu lwe ndibonereza Isirayiri olw’ebibi bye,

ndisaanyaawo ebyoto by’e Beseri,

n’amayembe g’ekyoto galisalibwako

ne gagwa wansi.

153:15 a Yer 36:22 b Bal 3:20 c 1Bk 22:39Era ndisaanyaawo ennyumba ebeerwamu mu biseera eby’obutiti,

awamu n’ennyumba ebeerwamu mu biseera ey’ebbugumu;

era ndimenyaamenya n’ennyumba ezayolebwa n’amasanga,

ne nsanyaawo n’embiri,”

bw’ayogera Mukama.