Amosi 3 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 3:1-15

Mboni Zotsutsa Israeli

1Inu Aisraeli, imvani mawu awa amene Yehova wayankhula kutsutsana nanu, kutsutsana ndi banja lonse limene analitulutsa mu Igupto:

2“Inu nokha ndi amene ndinakusankhani

pakati pa mabanja onse a dziko lapansi;

nʼchifukwa chake ndidzakulangani

chifukwa cha machimo anu onse.”

3Kodi anthu awiri nʼkuyendera limodzi

asanapangane?

4Kodi mkango umabangula mʼnkhalango

usanagwire nyama?

Kodi msona wamkango umalira mʼphanga mwake

pamene sunagwire kanthu?

5Kodi mbalame nʼkutera pa msampha

pamene palibe nyambo yake?

Kodi msampha umafwamphuka

usanakole kanthu?

6Kodi pamene lipenga la nkhondo lalira mu mzinda,

anthu sanjenjemera?

Pamene tsoka lafika mu mzinda,

kodi si Yehova amene wachititsa zimenezo?

7Zoonadi Ambuye Yehova sachita kanthu

asanawulule zimene akufuna kuchita

kwa atumiki ake, aneneri.

8Mkango wabangula,

ndani amene sachita mantha?

Ambuye Yehova wayankhula,

ndani amene sanganenere?

9Lengezani zimenezi ku nyumba zaufumu za ku Asidodi

ndiponso ku nyumba zaufumu za ku Igupto:

“Sonkhanani ku mapiri a ku Samariya;

onani chisokonezo pakati pake

ndiponso kuponderezana pakati pa anthu ake.”

10“Iwo sadziwa kuchita zolungama,

ndipo amadzaza malo awo otetezedwa ndi zinthu zolanda ku nkhondo ndi zakuba,” akutero Yehova.

11Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akunena izi:

“Mdani adzalizungulira dzikoli;

iye adzagwetsa malinga ako,

ndi kufunkha nyumba zako zaufumu.”

12Yehova akuti,

“Monga mʼbusa amalanditsa mʼkamwa mwa mkango

miyendo iwiri yokha kapena msonga yokha ya khutu,

moteronso ndimo mmene adzapulumukire Aisraeli

amene amakhala mu Samariya

pa msonga za mabedi awo,

ndi ku Damasiko pa akakhutagona awo.”

13“Imvani izi ndipo mupereke umboni wotsutsa nyumba ya Yakobo,” akutero Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.

14“Pa tsiku limene ndidzalange Israeli chifukwa cha machimo ake,

ndidzagumula maguwa ansembe a ku Beteli;

nyanga za guwa zidzathyoka

ndipo zidzagwa pansi.

15Ndidzagwetsa nyumba ya pa nthawi yozizira

pamodzi ndi nyumba ya pa nthawi yotentha;

nyumba zokongoletsedwa ndi minyanga ya njovu zidzawonongedwa

ndipo nyumba zikuluzikulu zidzaphwasulidwa,”

akutero Yehova.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Амос 3:1-15

Свидетельства против Исроила

1Слушай это слово, которое Вечный изрёк против тебя, о народ Исроила, против всех родов, которые Я вывел из Египта:

2– Вы единственные, кого Я избрал3:2 Букв.: «познал».

из всех народов земли;

поэтому Я накажу вас

за все ваши грехи.

3Разве пойдут двое вместе,

если не сговорятся заранее?

4Разве ревёт в чаще лев,

когда у него нет добычи?

Разве рычит молодой лев в своём логове,

когда он ничего не поймал?

5Разве птица попадётся в петлю на земле,

если для неё не положили приманку?

Разве поднимется с земли петля,

когда ничего в неё не попало?

6Когда в городе звучит рог,

разве народ не трепещет?

Когда в город приходит беда,

разве не Вечный наслал её?

7Также Владыка Вечный не делает ничего,

не открыв Своего замысла

Своим рабам пророкам.

8Лев заревел –

кто не испугается?

Владыка Вечный сказал –

кто не станет пророчествовать?

9Объявите крепостям Ашдода и Египта:

– Соберитесь на горах Сомарии;

посмотрите на великие бесчинства в ней,

на притеснения среди её народа.

10– Они не знают, как поступать праведно, –

возвещает Вечный, –

те, кто копит в своих крепостях добро,

собранное насилием и грабежом.

11Поэтому так говорит Владыка Вечный:

– Враг заполонит землю;

он разрушит твои твердыни

и разграбит твои крепости.

12Так говорит Вечный:

– Как пастух иногда вырывает из пасти льва

две голени или часть уха,

так спасены будут исроильтяне,

те, кто сидят в Сомарии

на краю своих постелей

и на своих ложах из Дамаска3:12 Или: «…исроильтяне, живущие в Сомарии; у них останутся лишь ножка постели или спинка ложа»..

13– Слушайте это и свидетельствуйте против потомков Якуба, – возвещает Владыка Вечный, Бог Сил.

14– В день, когда Я накажу Исроил за его грехи,

Я разрушу и жертвенники Вефиля3:14 Исроильский царь Иеровоам I приказал отлить двух золотых тельцов и одного из них поставил в Вефиле. Он возвёл поклонение тельцам в ранг национальной религии (см. 3 Цар. 12:25-33).;

рога жертвенника будут отсечены

и упадут на землю3:14 Человек, которому грозит смерть, мог просить о пощаде, взявшись за рога жертвенника, которые возвышались с каждого из его четырёх углов. И значит, этот стих говорит о том, что Исроилу негде будет искать защиты (см. 3 Цар. 1:50-53)..

15Я разорю зимний дом

вместе с летним домом;

украшенные слоновой костью дома будут уничтожены,

и особняки3:15 Или: «многие дома». будут снесены, –

возвещает Вечный.