Amosi 3 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 3:1-15

Mboni Zotsutsa Israeli

1Inu Aisraeli, imvani mawu awa amene Yehova wayankhula kutsutsana nanu, kutsutsana ndi banja lonse limene analitulutsa mu Igupto:

2“Inu nokha ndi amene ndinakusankhani

pakati pa mabanja onse a dziko lapansi;

nʼchifukwa chake ndidzakulangani

chifukwa cha machimo anu onse.”

3Kodi anthu awiri nʼkuyendera limodzi

asanapangane?

4Kodi mkango umabangula mʼnkhalango

usanagwire nyama?

Kodi msona wamkango umalira mʼphanga mwake

pamene sunagwire kanthu?

5Kodi mbalame nʼkutera pa msampha

pamene palibe nyambo yake?

Kodi msampha umafwamphuka

usanakole kanthu?

6Kodi pamene lipenga la nkhondo lalira mu mzinda,

anthu sanjenjemera?

Pamene tsoka lafika mu mzinda,

kodi si Yehova amene wachititsa zimenezo?

7Zoonadi Ambuye Yehova sachita kanthu

asanawulule zimene akufuna kuchita

kwa atumiki ake, aneneri.

8Mkango wabangula,

ndani amene sachita mantha?

Ambuye Yehova wayankhula,

ndani amene sanganenere?

9Lengezani zimenezi ku nyumba zaufumu za ku Asidodi

ndiponso ku nyumba zaufumu za ku Igupto:

“Sonkhanani ku mapiri a ku Samariya;

onani chisokonezo pakati pake

ndiponso kuponderezana pakati pa anthu ake.”

10“Iwo sadziwa kuchita zolungama,

ndipo amadzaza malo awo otetezedwa ndi zinthu zolanda ku nkhondo ndi zakuba,” akutero Yehova.

11Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akunena izi:

“Mdani adzalizungulira dzikoli;

iye adzagwetsa malinga ako,

ndi kufunkha nyumba zako zaufumu.”

12Yehova akuti,

“Monga mʼbusa amalanditsa mʼkamwa mwa mkango

miyendo iwiri yokha kapena msonga yokha ya khutu,

moteronso ndimo mmene adzapulumukire Aisraeli

amene amakhala mu Samariya

pa msonga za mabedi awo,

ndi ku Damasiko pa akakhutagona awo.”

13“Imvani izi ndipo mupereke umboni wotsutsa nyumba ya Yakobo,” akutero Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.

14“Pa tsiku limene ndidzalange Israeli chifukwa cha machimo ake,

ndidzagumula maguwa ansembe a ku Beteli;

nyanga za guwa zidzathyoka

ndipo zidzagwa pansi.

15Ndidzagwetsa nyumba ya pa nthawi yozizira

pamodzi ndi nyumba ya pa nthawi yotentha;

nyumba zokongoletsedwa ndi minyanga ya njovu zidzawonongedwa

ndipo nyumba zikuluzikulu zidzaphwasulidwa,”

akutero Yehova.

La Bible du Semeur

Amos 3:1-15

Avertissements et menaces

Les reproches

1Ecoutez bien cette parole que l’Eternel prononce sur vous, Israélites, sur toute la famille que j’ai fait sortir d’Egypte :

2Je vous ai choisis, et vous seuls,

de toutes les familles de la terre,

aussi vous châtierai-je

pour tous vos crimes.

3Deux hommes marchent-ils ensemble

sans s’être mis d’accord ?

4Le lion rugit-il ╵au fond de la forêt

sans avoir une proie ?

Le jeune lion gronde-t-il ╵au fond de sa tanière

s’il n’a rien capturé ?

5L’oiseau se jette-t-il ╵dans le filet qui est à terre

s’il n’y a pas d’appât ?

Le piège se referme-t-il

sans avoir fait de prise ?

6Et sonne-t-on du cor ╵aux remparts de la ville

sans que les habitants ╵se mettent à trembler ?

Un malheur viendra-t-il ╵frapper une cité

à moins que l’Eternel ╵en soit l’auteur ?

7Ainsi, le Seigneur, l’Eternel, ╵n’accomplit rien

sans avoir d’abord révélé ses plans

à ses serviteurs, les prophètes.

8Le lion a rugi : ╵qui n’aurait pas de crainte ?

Oui, le Seigneur, ╵l’Eternel, a parlé.

Qui oserait ne pas prophétiser ?

Le châtiment de la corruption

9Faites retentir cet appel ╵dans les palais d’Ashdod

et dans les palais de l’Egypte :

Rassemblez-vous sur les montagnes ╵de Samarie,

voyez quels grands désordres

et combien d’oppressions ╵règnent au milieu d’elle.

10Ces gens ne savent pas ╵agir avec droiture,

l’Eternel le déclare.

Ils entassent dans leurs palais ╵ce qu’ils ont obtenu ╵par la violence et le pillage.

11C’est pourquoi, le Seigneur, ╵l’Eternel, dit ceci :

Un ennemi viendra ╵tout autour du pays,

il abattra ta force

et tes palais seront pillés.

12L’Eternel dit ceci :

Comme un berger arrache ╵de la gueule du lion

deux jarrets ou un bout d’oreille ╵du mouton qu’il a pris3.12 Voir Ex 22.12.,

de même, des Israélites

qui demeurent à Samarie ╵seront arrachés à l’ennemi

– il en restera le coin d’un divan ╵ou le morceau d’un pied de lit3.12 Samarie seront arrachés… pied de lit. La traduction : le morceau d’un pied de lit est incertaine. Autre traduction : Samarie, installés au creux d’un divan ou au fond d’un lit, seront arrachés à l’ennemi..

13Ecoutez bien ceci ╵et transmettez ensuite ╵cet avertissement ╵aux enfants de Jacob

– c’est là ce que déclare le Seigneur, ╵l’Eternel, le Dieu des armées célestes.

14Car le jour où j’interviendrai ╵pour punir Israël ╵de ses nombreux péchés,

j’interviendrai ╵contre les autels de Béthel3.14 A Béthel, à environ 15 kilomètres au nord de Jérusalem, le roi Jéroboam Ier avait fait ériger un autel et un veau d’or afin d’empêcher les membres des dix tribus du royaume du Nord de se rendre à Jérusalem pour adorer au Temple (voir 1 R 12.26-29 ; 2 R 23.15).,

leurs cornes seront abattues

et elles tomberont à terre.

15Je ferai s’écrouler

ses maisons pour l’hiver, ╵ses maisons pour l’été,

et ses maisons ornées d’ivoire ╵seront anéanties,

ses maisons imposantes ╵disparaîtront,

l’Eternel le déclare.