Amosi 1 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 1:1-15

1Mawu a Amosi, mmodzi mwa anthu oweta nkhosa ku Tekowa. Zimene iye anaona mʼmasomphenya zokhudza Israeli patatsala zaka ziwiri kuti chivomerezi chichitike, nthawi imene Uziya anali mfumu ya Yuda ndipo Yeroboamu mwana wa Yowasi anali mfumu ya Israeli.

2Amosi anati:

“Yehova akubangula mu Ziyoni

ndipo akumveka ngati bingu mu Yerusalemu;

msipu wa abusa ukulira,

ndipo pamwamba pa Karimeli pakuwuma.”

Chiweruzo pa Anthu Oyandikana ndi Israeli

3Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Damasiko akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza anapuntha Giliyadi

ndi zopunthira za mano achitsulo,

4Ine ndidzatumiza moto pa nyumba ya Hazaeli

umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.

5Ndidzathyola chipata cha Damasiko;

ndidzawononga mfumu yokhala ku Chigwa cha Aveni,

ndiponso iye amene akugwira ndodo yaufumu mu Beti-Edeni.

Anthu a ku Aramu adzapita ku ukapolo ku Kiri,”

akutero Yehova.

6Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Gaza akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza anatenga ukapolo mtundu wathunthu

ndi kuwugulitsa ku Edomu,

7ndidzatumiza moto pa makoma a Gaza

umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.

8Ndidzawononga mfumu ya ku Asidodi

komanso amene akugwira ndodo yaufumu ku Asikeloni.

Ndidzalanga Ekroni,

mpaka wotsala mwa Afilisti atafa,”

akutero Ambuye Yehova.

9Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Turo akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza iwo anagulitsa mtundu wathunthu ku ukapolo ku Edomu,

osasunga pangano laubale lija,

10Ine ndidzatumiza moto pa makoma a Turo

umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.”

11Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Edomu akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza anathamangitsa mʼbale wake ndi lupanga,

popanda nʼchifundo chomwe.

Popeza mkwiyo wake unakulabe

ndipo ukali wake sunatonthozeke,

12Ine ndidzatumiza moto pa Temani

umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Bozira.”

13Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Amoni akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza anatumbula akazi oyembekezera a ku Giliyadi

nʼcholinga choti akuze malire awo,

14Ine ndidzayatsa moto pa makoma a ku Raba

umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.

Padzakhala kulira kwakukulu pa tsiku la nkhondoyo,

kumenyana kudzakhala kwafumbi ngati mkuntho wa kamvuluvulu.

15Mfumu yawo idzatengedwa kupita ku ukapolo,

iyo pamodzi ndi akuluakulu ake,”

akutero Yehova.

Persian Contemporary Bible

عاموس 1:1-15

1عاموس، چوپانی از اهالی تقوع بود. دو سال قبل از وقوع زلزله، در زمان عزيا، پادشاه يهودا و يربعام (پسر يهوآش) پادشاه اسرائيل، خداوند اين رؤيا را درباره آيندهٔ اسرائيل به او نشان داد. 2عاموس دربارهٔ آنچه ديد و شنيد چنين می‌گويد:

«خداوند از كوه صهيون در اورشليم، مانند شير غرش می‌كند و چراگاههای سبز و خرم كوه كرمل خشک می‌شوند و چوپانها ماتم می‌گيرند.»

مجازات همسايگان اسرائيل

سوريه

3خداوند می‌فرمايد: «اهالی دمشق بارها گناه كرده‌اند و من اين را فراموش نخواهم كرد و از سر تقصيرشان نخواهم گذشت، زيرا همانطور كه با ميله‌های آهنی خرمن را می‌كوبند، آنها هم در جلعاد قوم مرا در هم كوبيدند. 4پس من قصر حزائيل پادشاه را به آتش خواهم كشيد و قلعهٔ مستحكم بنهدد را ويران خواهم كرد. 5پشت‌بندهايی را كه دروازه‌های دمشق را می‌بندند خواهم شكست و مردمانش را تا دشت آون هلاک خواهم ساخت و پادشاه بيت‌عدن را نابود خواهم كرد. اهالی سوريه به شهر قير به اسارت خواهند رفت.»

فلسطين

6خداوند می‌فرمايد: «مردم غزه بارها مرتكب گناه شده‌اند و من اين را فراموش نخواهم كرد و از سر تقصيرشان نخواهم گذشت، زيرا آنها قوم مرا تبعيد نموده، ايشان را به عنوان برده در ادوم فروختند. 7پس من حصارهای غزه را به آتش خواهم كشيد و تمام قلعه‌هايش را ويران خواهم كرد. 8اهالی اشدود را می‌كشم. شهر عقرون و پادشاه اشقلون را از بين می‌برم. تمام فلسطينی‌هايی كه باقی مانده‌اند هلاک خواهند شد.»

صور

9خداوند می‌فرمايد: «اهالی صور بارها گناه كرده‌اند و من اين را فراموش نخواهم كرد و از سر تقصيرشان نخواهم گذشت، زيرا پيمان برادری خود را با اسرائيل شكستند و به ايشان حمله كرده، آنها را به ادوم به اسارت بردند. 10پس من حصارهای شهر صور را به آتش می‌كشم و تمام قلعه‌ها و كاخهايش را می‌سوزانم.»

ادوم

11خداوند می‌فرمايد: «مردم ادوم بارها مرتكب گناه شده‌اند و من اين را فراموش نخواهم كرد و از سر تقصيرشان نخواهم گذشت، چون آنها با بی‌رحمی تمام به جان برادران اسرائيلی خود افتادند و با خشم و غضب آنها را از دم شمشير گذراندند. 12پس من هم شهر تيمان را به آتش خواهم كشيد و قلعه‌های بصره را خواهم سوزاند.»

عمون

13خداوند می‌فرمايد: «اهالی عمون بارها مرتكب گناه شده‌اند و من اين را فراموش نخواهم كرد و از سر تقصيرشان نخواهم گذشت، زيرا در جنگ جلعاد برای توسعهٔ مرزهای خود دست به كشتار هولناكی زدند و با شمشير، شكم زنان حامله را پاره كردند.

14«پس، من حصارهای شهر ربه را به آتش خواهم كشيد و قلعه‌ها و كاخهايش را خواهم سوزاند. در آنجا غريو جنگ، همچون غرش طوفان بلند خواهد شد. 15پادشاه و شاهزادگان عمون همه با هم به اسارت خواهند رفت.»