Amosi 1 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 1:1-15

1Mawu a Amosi, mmodzi mwa anthu oweta nkhosa ku Tekowa. Zimene iye anaona mʼmasomphenya zokhudza Israeli patatsala zaka ziwiri kuti chivomerezi chichitike, nthawi imene Uziya anali mfumu ya Yuda ndipo Yeroboamu mwana wa Yowasi anali mfumu ya Israeli.

2Amosi anati:

“Yehova akubangula mu Ziyoni

ndipo akumveka ngati bingu mu Yerusalemu;

msipu wa abusa ukulira,

ndipo pamwamba pa Karimeli pakuwuma.”

Chiweruzo pa Anthu Oyandikana ndi Israeli

3Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Damasiko akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza anapuntha Giliyadi

ndi zopunthira za mano achitsulo,

4Ine ndidzatumiza moto pa nyumba ya Hazaeli

umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.

5Ndidzathyola chipata cha Damasiko;

ndidzawononga mfumu yokhala ku Chigwa cha Aveni,

ndiponso iye amene akugwira ndodo yaufumu mu Beti-Edeni.

Anthu a ku Aramu adzapita ku ukapolo ku Kiri,”

akutero Yehova.

6Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Gaza akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza anatenga ukapolo mtundu wathunthu

ndi kuwugulitsa ku Edomu,

7ndidzatumiza moto pa makoma a Gaza

umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.

8Ndidzawononga mfumu ya ku Asidodi

komanso amene akugwira ndodo yaufumu ku Asikeloni.

Ndidzalanga Ekroni,

mpaka wotsala mwa Afilisti atafa,”

akutero Ambuye Yehova.

9Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Turo akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza iwo anagulitsa mtundu wathunthu ku ukapolo ku Edomu,

osasunga pangano laubale lija,

10Ine ndidzatumiza moto pa makoma a Turo

umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.”

11Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Edomu akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza anathamangitsa mʼbale wake ndi lupanga,

popanda nʼchifundo chomwe.

Popeza mkwiyo wake unakulabe

ndipo ukali wake sunatonthozeke,

12Ine ndidzatumiza moto pa Temani

umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Bozira.”

13Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Amoni akunka nachimwirachimwira,

Ine sindileka kuwalanga.

Popeza anatumbula akazi oyembekezera a ku Giliyadi

nʼcholinga choti akuze malire awo,

14Ine ndidzayatsa moto pa makoma a ku Raba

umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.

Padzakhala kulira kwakukulu pa tsiku la nkhondoyo,

kumenyana kudzakhala kwafumbi ngati mkuntho wa kamvuluvulu.

15Mfumu yawo idzatengedwa kupita ku ukapolo,

iyo pamodzi ndi akuluakulu ake,”

akutero Yehova.

New Serbian Translation

Књига пророка Амоса 1:1-15

1Речи Амоса које је видео за Израиљ, док је био међу сточарима из Текује. Било је то две године пре земљотреса, у време Озије, цара Јуде, и за време Јеровоама, цара Израиља, Јоасовог сина.

2Он је рекао:

„Господ риче са Сиона,

из Јерусалима глас свој пушта.

Тугују пастирски пашњаци

и врх Кармила се суши.“

Суд над околним народима

3Овако каже Господ:

„Због три преступа Дамаска,

а и због четири, своју казну нећу да повучем,

јер су Галад овршили

гвозденом вршилицом.

4Бацићу огањ на кућу Азаилову

и спалиће Вен-Ададова утврђења.

5Изломићу преворнице на Дамаску,

истребићу живаљ из те долине Авен1,5 Или: долине идолатрије, што је погрдан назив за Дамаск и цара Арама.

и онога што у Вет-Едену жезло држи.

У изгнанство, у Кир ће отићи Арамов народ –

каже Господ.“

6Овако каже Господ:

„Због три преступа Газе,

а и због четири, своју казну нећу да повучем,

јер су све изгнанике одвели у ропство

и предали их Едому.

7Бацићу огањ на зидине Газе

и спалиће њена утврђења.

8Истребићу живаљ из Азота

и онога што у Аскалону жезло држи.

Руку ћу своју да окренем на Акарон,

и пострадаће остатак филистејски

– говори Господ Бог.“

9Овако каже Господ:

„Због три преступа Тира,

а и због четири, своју казну нећу да повучем,

јер су све изгнанике предали Едому.

Нису се сетили братског савеза.

10Бацићу огањ на зидине Тира

и спалиће његова утврђења.“

11Овако каже Господ:

„Због три преступа Едома,

а и због четири, своју казну нећу да повучем,

јер је мачем свога брата прогонио

и потиснуо своје смиловање.

У свом га је бесу сатирао стално

и довека разјарен био.

12Бацићу огањ на Теман

и спалиће утврђења Восоре.“

13Овако каже Господ:

„Због три преступа синова Амонових,

а и због четири, своју казну нећу да повучем,

јер су распорили труднице Галада

да би међу своју проширили.

14Запалићу огањ на зидинама Раве

и спалиће њена утврђења,

све уз поклич на дан боја

и уз вихор олујнога дана.

15А њихов ће цар отићи у изгнанство,

заједно – он и главари његови“ –

каже Господ.