1Mawu a Amosi, mmodzi mwa anthu oweta nkhosa ku Tekowa. Zimene iye anaona mʼmasomphenya zokhudza Israeli patatsala zaka ziwiri kuti chivomerezi chichitike, nthawi imene Uziya anali mfumu ya Yuda ndipo Yeroboamu mwana wa Yowasi anali mfumu ya Israeli.
2Amosi anati:
“Yehova akubangula mu Ziyoni
ndipo akumveka ngati bingu mu Yerusalemu;
msipu wa abusa ukulira,
ndipo pamwamba pa Karimeli pakuwuma.”
Chiweruzo pa Anthu Oyandikana ndi Israeli
3Yehova akuti,
“Chifukwa anthu a ku Damasiko akunka nachimwirachimwira,
Ine sindileka kuwalanga.
Popeza anapuntha Giliyadi
ndi zopunthira za mano achitsulo,
4Ine ndidzatumiza moto pa nyumba ya Hazaeli
umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.
5Ndidzathyola chipata cha Damasiko;
ndidzawononga mfumu yokhala ku Chigwa cha Aveni,
ndiponso iye amene akugwira ndodo yaufumu mu Beti-Edeni.
Anthu a ku Aramu adzapita ku ukapolo ku Kiri,”
akutero Yehova.
6Yehova akuti,
“Chifukwa anthu a ku Gaza akunka nachimwirachimwira,
Ine sindileka kuwalanga.
Popeza anatenga ukapolo mtundu wathunthu
ndi kuwugulitsa ku Edomu,
7ndidzatumiza moto pa makoma a Gaza
umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.
8Ndidzawononga mfumu ya ku Asidodi
komanso amene akugwira ndodo yaufumu ku Asikeloni.
Ndidzalanga Ekroni,
mpaka wotsala mwa Afilisti atafa,”
akutero Ambuye Yehova.
9Yehova akuti,
“Chifukwa anthu a ku Turo akunka nachimwirachimwira,
Ine sindileka kuwalanga.
Popeza iwo anagulitsa mtundu wathunthu ku ukapolo ku Edomu,
osasunga pangano laubale lija,
10Ine ndidzatumiza moto pa makoma a Turo
umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.”
11Yehova akuti,
“Chifukwa anthu a ku Edomu akunka nachimwirachimwira,
Ine sindileka kuwalanga.
Popeza anathamangitsa mʼbale wake ndi lupanga,
popanda nʼchifundo chomwe.
Popeza mkwiyo wake unakulabe
ndipo ukali wake sunatonthozeke,
12Ine ndidzatumiza moto pa Temani
umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Bozira.”
13Yehova akuti,
“Chifukwa anthu a ku Amoni akunka nachimwirachimwira,
Ine sindileka kuwalanga.
Popeza anatumbula akazi oyembekezera a ku Giliyadi
nʼcholinga choti akuze malire awo,
14Ine ndidzayatsa moto pa makoma a ku Raba
umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.
Padzakhala kulira kwakukulu pa tsiku la nkhondoyo,
kumenyana kudzakhala kwafumbi ngati mkuntho wa kamvuluvulu.
15Mfumu yawo idzatengedwa kupita ku ukapolo,
iyo pamodzi ndi akuluakulu ake,”
akutero Yehova.
Amos kündigt Juda, Israel und den Nachbarvölkern Gottes Gericht an
(Kapitel 1–6)
Gott spricht sein Urteil über Israels Nachbarvölker
1In diesem Buch sind die Worte von Amos aufgeschrieben, einem Schafzüchter aus dem Dorf Tekoa. Zwei Jahre vor dem großen Erdbeben offenbarte ihm Gott, was er mit dem Nordreich Israel vorhatte. Damals regierte in Juda König Usija, und in Israel herrschte Jerobeam, der Sohn von Joasch.
2Amos verkündete dem Volk:
»Mächtig wie das Brüllen eines Löwen ertönt die Stimme des Herrn vom Berg Zion in Jerusalem. Da vertrocknen die saftigen Weiden der Hirten, und die Wälder auf dem Gipfel des Karmel verdorren.
3So spricht der Herr: Die Leute von Damaskus begehen ein abscheuliches Verbrechen nach dem anderen. Sie haben die Bewohner von Gilead wie mit einem eisernen Dreschschlitten niedergewalzt und zermalmt. Das werde ich nicht ungestraft lassen! 4Ich brenne die Paläste nieder, die König Hasaël und König Ben-Hadad errichtet haben. 5Ich zerschmettere die Riegel an den Stadttoren von Damaskus und töte die Herrscher von Bikat-Awen (›Unrechtstal‹) und Bet-Eden (›Freudenhaus‹). Die Bevölkerung von Syrien wird nach Kir verschleppt. Darauf gebe ich, der Herr, mein Wort!
6So spricht der Herr: Die Leute von der Philisterstadt Gaza begehen ein abscheuliches Verbrechen nach dem anderen. Sie haben die Einwohner ganzer Dörfer gefangen genommen und an die Edomiter verkauft. Das werde ich nicht ungestraft lassen! 7Ich brenne die Stadtmauern von Gaza nieder, seine Paläste werden ein Raub der Flammen. 8Die Herrscher von Aschdod und Aschkelon bringe ich um, und auch die Stadt Ekron bekommt meine Macht zu spüren. Die Philister, die dann noch übrig geblieben sind, finden den Tod. Darauf gebe ich, Gott, der Herr, mein Wort!
9So spricht der Herr: Die Leute von Tyrus begehen ein abscheuliches Verbrechen nach dem anderen. Sie haben ihren Freundschaftsbund mit Israel gebrochen und die Einwohner ganzer Dörfer an die Edomiter verkauft. Das werde ich nicht ungestraft lassen! 10Ich brenne die Stadtmauern von Tyrus nieder, seine Paläste werden ein Raub der Flammen.
11So spricht der Herr: Die Leute von Edom begehen ein abscheuliches Verbrechen nach dem anderen. Sie haben die Israeliten, ihr Brudervolk, erbarmungslos bekämpft und unschuldiges Blut vergossen. Ihr Hass kennt keine Grenzen, ständig führen sie Krieg gegen mein Volk. Das werde ich nicht ungestraft lassen! 12Ich brenne Teman nieder, und auch die Paläste der Hauptstadt Bozra werden ein Raub der Flammen.
13So spricht der Herr: Die Leute von Ammon begehen ein abscheuliches Verbrechen nach dem anderen. Sie führten Krieg, um ihre Herrschaft auszudehnen, sie ließen sogar schwangeren Frauen im Gebiet von Gilead den Bauch aufschlitzen. Das werde ich nicht ungestraft lassen! 14Die Mauern ihrer Hauptstadt Rabba lege ich in Schutt und Asche, ihre Paläste werden ein Raub der Flammen. Dann ertönt überall das Kriegsgeschrei, und die Schlacht tobt wie ein verheerender Sturm. 15Der König der Ammoniter und alle führenden Männer werden in die Verbannung geschickt. Darauf gebe ich, der Herr, mein Wort!