Akolose 4 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Akolose 4:1-18

1Mabwana, antchito anu muzikhala nawo mwachilungamo ndi moyenera, podziwa kuti nanunso muli nawo Ambuye anu mmwamba.

Malangizo Ena

2Pempherani modzipereka, mukhale atcheru ndiponso oyamika. 3Ndipo muzitipemphereranso ife kuti Mulungu atitsekulire khomo la uthenga wathu, kuti tilalikire chinsinsi cha Khristu, chimene ndine womangidwa nacho mʼndende. 4Pempherani kuti ndilalikire momveka bwino, monga ndikuyenera. 5Mayendedwe anu pakati pa akunja, akhale anzeru ndipo mugwiritse ntchito mpata uliwonse umene muli nawo. 6Mayankhulidwe anu nthawi zonse akhale odzaza ndi chisomo ndi okoma, kuti mudziwe kuyankha aliyense.

Mawu Otsiriza

7Tukiko adzakuwuzani zonse za ine. Iye ndi mʼbale wokondedwa, mtumiki wokhulupirika ndiponso wantchito mnzanga mwa Ambuye. 8Ine ndikumutumiza kwa inu ndi cholinga choti mudziwe zimene tikukumana nazo ndiponso kuti alimbikitse mitima yanu. 9Iye akubwera ndi Onesimo, mʼbale wathu wokhulupirika ndi wokondedwa, amene ndi mmodzi mwa inu. Iwo adzakuwuzani zonse zimene zikuchitika kuno.

10Aristariko, wamʼndende mnzanga akupereka moni, Marko akuperekanso moni, msuweni wa Barnaba. (Inu munawuzidwa kale za Iye. Iye akabwera kwanuko, mulandireni). 11Yesu wotchedwa Yusto, akuperekanso moni. Amenewa ndi Ayuda okhawo pakati pa atumiki anzanga mu ufumu wa Mulungu, ndipo aonetsa kuti ndi chitonthozo kwa ine. 12Epafra ndi mmodzi mwa inu ndiponso mtumiki wa Khristu Yesu, akupereka moni. Iyeyu nthawi zonse amakupemphererani mwamphamvu, kuti mukhazikike pa chifuniro chonse cha Mulungu, mukhale okhwima ndi otsimikiza kwathunthu. 13Ine ndikumuchitira umboni kuti amagwira ntchito mwamphamvu chifukwa cha inu ndiponso kwa amene ali ku Laodikaya ndi Herapoli. 14Luka, dotolo wathu wokondedwa ndi Dema, akupereka moni. 15Perekani moni kwa abale a ku Laodikaya, ndiponso kwa Numfa ndi mpingo wa mʼnyumba mwake.

16Kalata iyi ikawerengedwa pakati panu, muonetsetse kuti ikawerengedwenso ku mpingo wa ku Laodikaya ndipo inunso muwerenge kalata yochokera ku Laodikaya.

17Uzani Arkipo kuti, “Wonetsetsa kuti wamaliza ntchito imene unayilandira mwa Ambuye.”

18Ine Paulo, ndikulemba ndi dzanja langa moni uwu. Kumbukirani kuti ndili mu unyolo. Chisomo chikhale ndi inu.

Słowo Życia

Kolosan 4:1-18

1Panowie, bądźcie sprawiedliwi i uczciwi wobec swoich poddanych. Pamiętajcie, że wy również macie nad sobą Pana, który mieszka w niebie.

Dalsze wskazówki

2Wytrwale się módlcie, uważajcie na siebie i okazujcie wdzięczność Bogu! 3Proście również, aby Bóg dawał nam nowe możliwości głoszenia tej wspaniałej tajemnicy Chrystusa, z powodu której jestem teraz w więzieniu, 4i abym przedstawiał ją ludziom tak, jak należy. 5Gdy jesteście wśród niewierzących, mądrze wykorzystujcie wasz czas. 6Niech wasze słowa będą uprzejme. Mówcie im o tym, co jest naprawdę ważne. Bądźcie też gotowi, aby odpowiadać na ich pytania.

Końcowe pozdrowienia

7-8Chcę, abyście wiedzieli, co u mnie słychać. Dlatego wysyłam do was Tychika, mojego drogiego przyjaciela oraz wiernego pomocnika i współpracownika w pracy dla Pana. On wszystko wam opowie i doda wam otuchy. 9Posyłam też waszego rodaka, Onezyma, wiernego i drogiego przyjaciela. Oni wam o wszystkim opowiedzą.

10Pozdrawia was Arystarch—mój współwięzień, Marek—kuzyn Barnaby (pamiętajcie, że prosiłem was, abyście okazali mu pomoc, gdy do was przybędzie), 11i Jezus Justus. Są to jedyni Żydzi, którzy tu ze mną pracują dla królestwa Bożego i są dla mnie wielką pociechą.

12Pozdrawia was Epafras, sługa Chrystusa i wasz rodak. Zawsze gorliwie modli się za was, abyście dojrzewali i byli doskonale przygotowani do wypełniania woli Boga. 13Zapewniam was, że bardzo ciężko pracował dla was oraz dla wierzących z Laodycei i Hierapolis.

14Pozdrawia was również nasz drogi doktor Łukasz oraz Demas. 15Przekażcie, proszę, moje pozdrowienia przyjaciołom w Laodycei. Pozdrówcie również Nimfę i kościół, który spotyka się w jej domu.

16Po przeczytaniu, przekażcie ten list kościołowi w Laodycei, a wy z kolei przeczytajcie list, który wysłałem do nich. 17Archipowi zaś przekażcie wiadomość: „Staraj się dobrze wykonać zadanie, które zlecił ci Pan”.

18Teraz ja, Paweł, dopisuję własnoręcznie moje pozdrowienia. Nie zapomnijcie o tym, że jestem w więzieniu. Niech Bóg obdarza was swoją łaską!