Akolose 4 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Akolose 4:1-18

1Mabwana, antchito anu muzikhala nawo mwachilungamo ndi moyenera, podziwa kuti nanunso muli nawo Ambuye anu mmwamba.

Malangizo Ena

2Pempherani modzipereka, mukhale atcheru ndiponso oyamika. 3Ndipo muzitipemphereranso ife kuti Mulungu atitsekulire khomo la uthenga wathu, kuti tilalikire chinsinsi cha Khristu, chimene ndine womangidwa nacho mʼndende. 4Pempherani kuti ndilalikire momveka bwino, monga ndikuyenera. 5Mayendedwe anu pakati pa akunja, akhale anzeru ndipo mugwiritse ntchito mpata uliwonse umene muli nawo. 6Mayankhulidwe anu nthawi zonse akhale odzaza ndi chisomo ndi okoma, kuti mudziwe kuyankha aliyense.

Mawu Otsiriza

7Tukiko adzakuwuzani zonse za ine. Iye ndi mʼbale wokondedwa, mtumiki wokhulupirika ndiponso wantchito mnzanga mwa Ambuye. 8Ine ndikumutumiza kwa inu ndi cholinga choti mudziwe zimene tikukumana nazo ndiponso kuti alimbikitse mitima yanu. 9Iye akubwera ndi Onesimo, mʼbale wathu wokhulupirika ndi wokondedwa, amene ndi mmodzi mwa inu. Iwo adzakuwuzani zonse zimene zikuchitika kuno.

10Aristariko, wamʼndende mnzanga akupereka moni, Marko akuperekanso moni, msuweni wa Barnaba. (Inu munawuzidwa kale za Iye. Iye akabwera kwanuko, mulandireni). 11Yesu wotchedwa Yusto, akuperekanso moni. Amenewa ndi Ayuda okhawo pakati pa atumiki anzanga mu ufumu wa Mulungu, ndipo aonetsa kuti ndi chitonthozo kwa ine. 12Epafra ndi mmodzi mwa inu ndiponso mtumiki wa Khristu Yesu, akupereka moni. Iyeyu nthawi zonse amakupemphererani mwamphamvu, kuti mukhazikike pa chifuniro chonse cha Mulungu, mukhale okhwima ndi otsimikiza kwathunthu. 13Ine ndikumuchitira umboni kuti amagwira ntchito mwamphamvu chifukwa cha inu ndiponso kwa amene ali ku Laodikaya ndi Herapoli. 14Luka, dotolo wathu wokondedwa ndi Dema, akupereka moni. 15Perekani moni kwa abale a ku Laodikaya, ndiponso kwa Numfa ndi mpingo wa mʼnyumba mwake.

16Kalata iyi ikawerengedwa pakati panu, muonetsetse kuti ikawerengedwenso ku mpingo wa ku Laodikaya ndipo inunso muwerenge kalata yochokera ku Laodikaya.

17Uzani Arkipo kuti, “Wonetsetsa kuti wamaliza ntchito imene unayilandira mwa Ambuye.”

18Ine Paulo, ndikulemba ndi dzanja langa moni uwu. Kumbukirani kuti ndili mu unyolo. Chisomo chikhale ndi inu.

New International Version

Colossians 4:1-18

1Masters, provide your slaves with what is right and fair, because you know that you also have a Master in heaven.

Further Instructions

2Devote yourselves to prayer, being watchful and thankful. 3And pray for us, too, that God may open a door for our message, so that we may proclaim the mystery of Christ, for which I am in chains. 4Pray that I may proclaim it clearly, as I should. 5Be wise in the way you act toward outsiders; make the most of every opportunity. 6Let your conversation be always full of grace, seasoned with salt, so that you may know how to answer everyone.

Final Greetings

7Tychicus will tell you all the news about me. He is a dear brother, a faithful minister and fellow servant4:7 Or slave; also in verse 12 in the Lord. 8I am sending him to you for the express purpose that you may know about our4:8 Some manuscripts that he may know about your circumstances and that he may encourage your hearts. 9He is coming with Onesimus, our faithful and dear brother, who is one of you. They will tell you everything that is happening here.

10My fellow prisoner Aristarchus sends you his greetings, as does Mark, the cousin of Barnabas. (You have received instructions about him; if he comes to you, welcome him.) 11Jesus, who is called Justus, also sends greetings. These are the only Jews4:11 Greek only ones of the circumcision group among my co-workers for the kingdom of God, and they have proved a comfort to me. 12Epaphras, who is one of you and a servant of Christ Jesus, sends greetings. He is always wrestling in prayer for you, that you may stand firm in all the will of God, mature and fully assured. 13I vouch for him that he is working hard for you and for those at Laodicea and Hierapolis. 14Our dear friend Luke, the doctor, and Demas send greetings. 15Give my greetings to the brothers and sisters at Laodicea, and to Nympha and the church in her house.

16After this letter has been read to you, see that it is also read in the church of the Laodiceans and that you in turn read the letter from Laodicea.

17Tell Archippus: “See to it that you complete the ministry you have received in the Lord.”

18I, Paul, write this greeting in my own hand. Remember my chains. Grace be with you.