Akolose 3 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Akolose 3:1-25

Moyo Watsopano

1Tsono popeza munaukitsidwa pamodzi ndi Khristu, ikani mitima yanu pa zinthu za kumwamba, kumene Khristu akukhala ku dzanja lamanja la Mulungu. 2Muzifunafuna zinthu za kumwamba, osati zinthu za pa dziko lapansi. 3Pakuti munafa, ndipo moyo wanu tsopano wabisika pamodzi ndi Khristu mwa Mulungu. 4Khristu, amene ndiye moyo wanu, akadzaonekanso, pamenepo inunso mudzaoneka naye pamodzi mu ulemerero.

5Choncho, iphani zilakolako za dziko lapansi mwa inu, monga: dama, zodetsa, kulakalaka zosayenera, kukhumba zoyipa ndi umbombo, pakuti umbombo ndiko kupembedza mafano. 6Chifukwa cha zimenezi, mkwiyo wa Mulungu ukubwera pa ana osamvera. 7Inunso kale munkachita zomwezi, mʼmoyo wanu wakale uja. 8Koma tsopano mukuyenera kuzichotsa zinthu zonsezi monga: mkwiyo, ukali, dumbo, chipongwe ndi mawu onyansa. 9Musanamizane wina ndi mnzake, popeza munavula munthu wakale pamodzi ndi zochita zake 10ndipo mwavala munthu watsopano, amene nzeru zake zikukonzedwanso kuti afanane ndi Mlengi wake. 11Pano palibe kusiyana pakati pa Mgriki ndi Myuda, wochita mdulidwe ndi wosachita, wosaphunzira kapena wosachangamuka, kapolo kapena mfulu, koma Khristu yekha basi ndipo amakhala mwa onse.

12Choncho, ngati anthu osankhidwa ndi Mulungu, oyera mtima ndi okondedwa kwambiri, muvale chifundo, kukoma mtima, kudzichepetsa, kufatsa ndi kupirira. 13Mulezerane mtima ndipo muzikhululukirana ngati wina ali ndi chifukwa ndi mnzake. Muzikhululukirana monga Ambuye anakhululukira inu. 14Ndipo kuwonjezera pa zonsezi valani chikondi, chimene chimangirira zonsezi pamodzi mu mgwirizano wangwiro.

15Mtendere wa Khristu ulamulire mʼmitima mwanu, popeza monga ziwalo za thupi limodzi, munayitanidwa kuti mukhale ndi mtendere. Ndipo muziyamika. 16Mawu a Khristu akhazikike kwathunthu mʼmitima mwanu. Muziphunzitsana ndi kulangizana wina ndi mnzake ndi nzeru zonse pamene mukuyimba Masalimo, nyimbo zotamanda ndi nyimbo zauzimu, kuyimbira Mulungu ndi mitima yoyamika. 17Ndipo chilichonse chimene mungachite, kaya nʼkuyankhula, kaya nʼkugwira ntchito, muchite zonse mʼdzina la Ambuye Yesu, kuyamika kwa Mulungu Atate kudzera mwa Iye.

Malangizo a Moyo wa Mʼbanja la Chikhristu

18Inu akazi, gonjerani amuna anu, monga kuyenera mwa Ambuye.

19Inu amuna, kondani akazi anu ndipo musawapsere mtima.

20Inu ana, mverani makolo anu mu zonse pakuti izi zimakondweretsa Ambuye.

21Inu abambo, musakwiyitse ana anu, kuti angataye mtima.

22Inu antchito, mverani mabwana anu mu zonse, ndipo muzichita zimenezi osati nthawi yokhayo imene akukuonani kuti akukondeni, koma muzichite moona mtima ndi mopereka ulemu kwa Ambuye. 23Chilichonse mungachite, muchite ndi mtima wanu onse, monga mmene mungagwirire ntchito ya Ambuye osati ya anthu. 24Inu mukudziwa kuti mudzalandira mphotho monga cholowa kuchokera kwa Ambuye. Ndi Ambuye Khristu amene mukumutumikira. 25Aliyense amene amachita zolakwa adzalandira malipiro molingana ndi kulakwa kwake, ndipo palibe tsankho.

New International Reader’s Version

Colossians 3:1-25

Teachings About Holy Living

1You have been raised up with Christ. So think about things that are in heaven. That is where Christ is. He is sitting at God’s right hand. 2Think about things that are in heaven. Don’t think about things that are only on earth. 3You died. Now your life is hidden with Christ in God. 4Christ is your life. When he appears again, you also will appear with him in heaven’s glory.

5So put to death anything that comes from sinful desires. Get rid of sexual sins and impure acts. Don’t let your feelings get out of control. Remove from your life all evil desires. Stop always wanting more and more. You might as well be worshiping statues of gods. 6God’s anger is going to come because of these things. 7That’s the way you lived at one time in your life. 8But now here are the kinds of things you must also get rid of. You must get rid of anger, rage, hate and lies. Let no dirty words come out of your mouths. 9Don’t lie to one another. You have gotten rid of your old way of life and its habits. 10You have started living a new life. Your knowledge of how that life should have the Creator’s likeness is being made new. 11Here there is no Gentile or Jew. There is no difference between those who are circumcised and those who are not. There is no rude outsider, or even a Scythian. There is no slave or free person. But Christ is everything. And he is in everything.

12You are God’s chosen people. You are holy and dearly loved. So put on tender mercy and kindness as if they were your clothes. Don’t be proud. Be gentle and patient. 13Put up with one another. Forgive one another if you are holding something against someone. Forgive, just as the Lord forgave you. 14And over all these good things put on love. Love holds them all together perfectly as if they were one.

15Let the peace that Christ gives rule in your hearts. As parts of one body, you were appointed to live in peace. And be thankful. 16Let the message about Christ live among you like a rich treasure. Teach and correct one another wisely. Teach one another by singing psalms and hymns and songs from the Spirit. Sing to God with thanks in your hearts. 17Do everything you say or do in the name of the Lord Jesus. Always give thanks to God the Father through Christ.

Teachings About Christian Families

18Wives, follow the lead of your husbands. That’s what the Lord wants you to do.

19Husbands, love your wives. Don’t be mean to them.

20Children, obey your parents in everything. That pleases the Lord.

21Fathers, don’t make your children bitter. If you do, they will lose hope.

22Slaves, obey your earthly masters in everything. Don’t do it just to please them when they are watching you. Obey them with an honest heart. Do it out of respect for the Lord. 23Work at everything you do with all your heart. Work as if you were working for the Lord, not for human masters. 24Work because you know that you will finally receive as a reward what the Lord wants you to have. You are slaves of the Lord Christ. 25Anyone who does wrong will be paid back for what they do. God treats everyone the same.