Akolose 2 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Akolose 2:1-23

1Ndikufuna mudziwe kuti ndikukuvutikirani kwambiri, inuyo pamodzi ndi anzanu a ku Laodikaya, ndi ena onse amene sitinaonane maso ndi maso. 2Cholinga changa nʼchakuti alimbikitsidwe ndi kuyanjana pamodzi mʼchikondi, akhale odzaza ndi nzeru zomvetsa zinthu, ndi kuti azindikire chinsinsi cha Mulungu, chimene ndi Khristu. 3Mwa Iyeyu muli chuma chonse chobisidwa cha nzeru ndi chidziwitso. 4Ndikukuwuzani zimenezi kuti wina aliyense asakunamizeni ndi kukukopani ndi mawu ake. 5Pakuti ngakhale sindili pakati panu mʼthupi, ndili nanu pamodzi mu mzimu, ndipo ndikukondwa kuona kuti mukulongosola bwino zonse ndiponso kuti chikhulupiriro chanu mwa Khristu ndi chokhazikika ndithu.

Za Moyo Weniweni mwa Khristu

6Tsono popeza munavomereza Khristu Yesu kukhala Ambuye anu, mupitirire kukhala mwa Iyeyo. 7Mukhale ozikika mizu mwa Iye, ndipo moyo wanu umangike pa Iye. Mulimbike mʼchikhulupiriro monga momwe munaphunzirira, ndipo kuyamika kwanu kusefukire.

8Musalole kuti wina aliyense akutengeni ukapolo ndi mʼnzeru zachinyengo zolongosola zinthu zozama, zomwe zimachokera ku miyambo ya anthu ndi ku maganizo awo okhudza za dziko lapansi osati kwa Khristu.

9Pakuti mʼthupi la Khristu mumakhala umulungu wonse wathunthu. 10Ndipo inunso ndinu athunthu mwa Khristu. Iye ndiye mtsogoleri wa pamwamba pa maufumu onse ndi maulamuliro wonse. 11Mwa Iye inunso munachita mdulidwe mʼthupi lanu, osati mdulidwe ochitidwa ndi manja a anthu ayi, koma ochitidwa ndi Khristu pamene anavula khalidwe lanu lauchimo lija. 12Mu ubatizo, munayikidwa mʼmanda pamodzi ndi Khristu ndi kuukitsidwa naye pamodzi, pokhulupirira mphamvu za Mulungu amene anamuukitsa kwa akufa.

13Pamene munali akufa chifukwa cha machimo anu ndi osachita mdulidwe mʼmitima mwanu, Mulungu anakupatsani moyo mwa Khristu. Iye anatikhululukira machimo athu onse. 14Anafafaniza kalata ya ngongole yathu, pomwe panali milandu yotitsutsa ife. Iye anayichotsa, nayikhomera pa mtanda. 15Ndipo atalanda zida maufumu ndi maulamuliro, Iye anawachititsa manyazi powayendetsa pamaso pa anthu onse atawagonjetsa ndi mtanda.

Ufulu Wathu

16Nʼchifukwa chake musalole wina aliyense kukuzengani mlandu chifukwa cha zimene mumadya kapena kumwa, kapena za masiku achikondwerero cha chipembedzo, za chikondwerero cha mwezi watsopano, kapena za tsiku la Sabata. 17Zimenezi ndi chithunzithunzi chabe cha zinthu zimene zikubwera, koma choonadi chenicheni chikupezeka mwa Khristu. 18Musalole kuti wina aliyense amene amakonda kudzichepetsa mwachiphamaso ndi kumapembedza angelo akulepheretseni kukalandira mphotho. Munthu woteroyu amayankhulanso mwatsatanetsatane zinthu zimene akuti anaziona mʼmasomphenya. Anthuwa ndi odzitukumula ndi fundo zopanda pake zochokera mʼmaganizo mwawo amene si auzimu. 19Iwo sakulumikizananso ndi mutu, kumene kumachokera thupi lonse, logwirizidwa ndi kumangiriridwa pamodzi ndi mʼmitsempha yake ndi mnofu, limene limakula monga mmene Mulungu afunira kuti likulire.

20Popeza munafa pamodzi ndi Khristu kusiyana nayo miyambo ya dziko lapansi lino, nʼchifukwa chiyani mukukhalanso ngati a dziko lapansi lino? Bwanji mukumvera malamulo monga awa: 21“Usagwire chakuti,” “Usalawe chakuti,” “Usakhudze chakuti?” 22Malamulo amenewa amakhudza zinthu zimene zimatha zikamagwiritsidwa ntchito, ndipo malamulo ndi zophunzitsa za anthu chabe. 23Ndithu malamulo oterewa amaoneka ngati anzeru, pakuti amalamulira anthu ambiri pa zachipembedzo ndi pa zakudzichepetsa kwa chiphamaso, ndi pa zakuzunza thupi lawo, koma alibe mphamvu zoletsa kuchita zofuna za thupilo.

Knijga O Kristu

Kološanima 2:1-23

1Želim da znate koliko sam se mučio za vas, za Crkvu u Laodiceji i za sve one koji me još nisu osobno upoznali. 2Želim da se njihova srca ohrabre, povezana u ljubavi, da dobiju bogatu i punu spoznaju Božje tajne: Krista. 3U njemu su skrivena sva bogatstva mudrosti i spoznaje.

4Govorim vam to da vas nitko ne prevari uvjerljivim riječima. 5Iako sam daleko od vas, u mislima sam s vama. Veoma me raduje što živite kako treba i što je vaša vjera u Krista čvrsta.

Sloboda od pravila i novi život u Kristu

6Kako ste prihvatili Krista za Gospodina, tako nastavite s njime živjeti. 7Budite u njemu ukorijenjeni pa ćete se izgrađivati i učvršćivati u vjeri kako ste i poučeni. Obilno zahvaljujte Bogu.

8Nemojte da vas tko odvuče ispraznim mudrovanjem koje se temelji na ljudskim predajama i na počelima ovoga svijeta, a ne na Kristu. 9Jer u Kristu doslovce prebiva sva punina božanstva, 10a vi ste ispunjeni kroz zajedništvo s njime, koji je iznad svakoga poglavarstva i vlasti u svemiru.

11Kad ste došli Kristu, “obrezani” ste, ali ne tjelesno. Bio je to duhovni zahvat—“odrezana” je vaša grešna narav. 12Jer s Kristom ste ukopani pri krštenju. I s njim ste uskrsnuli u novi život jer ste se pouzdali u moćnu Božju silu, koja je i Krista podignula od mrtvih.

13Bili ste nekoć mrtvi zbog svojih prijestupa i zbog toga što vaša grešna narav još nije bila “odrezana”. Tada vas je Bog oživio s Kristom. Oprostio nam je sve prijestupe. 14Izbrisao je zadužnicu čije su odredbe bile protiv nas. Pribio ju je na Kristov križ i uništio. 15Tako je Bog razoružao zle vladare i vlasti. Javno ih je osramotio pobjedom na Kristovu križu.

16Neka vas zato nitko ne osuđuje zbog jela, pića ili zbog svetkovanja blagdana, mlađaka ili subote. 17Jer ta su pravila bila tek sjena prave stvarnosti—Krista. 18Ne dajte da vam oni koji uživaju u lažnoj poniznosti i štovanju anđela kažu kako niste zaslužili nagradu. Takvi ljudi, oholi zbog svoje tjelesne pameti, unedogled nabrajaju pojedinosti viđenja koja su imali. 19Ali ne drže se Krista, glave Tijela koje je snažno povezano i koje raste samo dobivajući hranu i snagu od Boga.

20Ako ste zaista umrli s Kristom, onda vas je on oslobodio temeljnih počela ovoga svijeta. Zašto se onda, kao da još pripadate ovomu svijetu, podvrgavate propisima kao što su: 21“Ne jedi! Ne kušaj! Ne takni!” 22Takva pravila obična su ljudska umotvorina jer se odnose na stvari koje uporabom nestaju. 23Ti propisi prividno su mudri zbog samozvanog bogoštovlja, poniznosti i trapljenja tijela, ali ne pomažu čovjeku da nadvlada svoje zle misli i želje.