Akolose 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Akolose 1:1-29

1Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu, ndi Timoteyo mʼbale wathu.

2Kulembera abale oyera mtima ndi okhulupirira a ku Kolose mwa Khristu.

Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu.

Kuyamika ndi Pemphero

3Timayamika Mulungu Atate wa Ambuye athu Yesu Khristu, nthawi zonse pamene tikukupemphererani. 4Timayamika chifukwa tinamva za chikhulupiriro chanu mwa Khristu Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse. 5Chikhulupiriro ndi chikondi, gwero lake ndi chiyembekezo chomwe muli nacho chodzalandira zimene anakusungirani kumwamba. Munamva kale za zimenezi kudzera mʼmawu a choonadi, Uthenga Wabwino 6umene unafika kwa inu. Pa dziko lonse lapansi Uthenga Wabwino ukubereka chipatso ndi kukula monga momwe zakhala zikuchitikira pakati panu kuyambira tsiku limene munawumva ndi kuzindikira chisomo cha Mulungu mu choonadi chonse. 7Inu munaphunzira zimenezi kuchokera kwa Epafra, mtumiki mnzathu wokondedwa, amene ndi mtumiki wokhulupirika wa Khristu mʼmalo mwathu. 8Iye anatiwuza za chikondi chanu chimene Mzimu anakupatsani.

9Chifukwa cha ichi, kuyambira tsiku limene tinamva za inu, sitinasiye kukupemphererani ndi kumupempha Mulungu kuti akudzazeni ndi chidziwitso cha chifuniro chake kudzera mu nzeru yonse yauzimu ndi kumvetsetsa. 10Ndipo tikupempherera zimenezi ndi cholinga chakuti inu mukhale moyo oyenera Ambuye ndi kumukondweretsa mʼnjira zonse. Kubereka chipatso pa ntchito iliyonse yabwino, ndi kukula mʼchidziwitso cha Mulungu. 11Timapempheranso kuti Mulungu akulimbikitseni ndi mphamvu yake yonse ya ulemerero wake, kuti muzipirira zonse ndi mitima yofatsa ndi ya chimwemwe 12ndi kuyamika Atate nthawi zonse, amene wakuyenerezani kuti mulandire nawo chuma cha oyera mtima mu ufumu wa kuwunika. 13Pakuti Iye anatipulumutsa ku ulamuliro wa mdima ndi kutibweretsa mu ufumu wa Mwana wake wokondedwa. 14Mwa Iyeyu ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo.

Kupambana Koposa kwa Khristu

15Mwanayu ndiye chithunzi cha Mulungu wosaonekayo. Iye ndiye Mwana wake woyamba kubadwa ndi wolamulira zolengedwa zonse. 16Pakuti zinthu zonse zinalengedwa kudzera mwa Iye. Zinthu zakumwamba ndi za pa dziko lapansi, zooneka ndi zosaoneka, maufumu, akuluakulu, aulamuliro ndi amphamvu. Zinthu zonse zinalengedwa kudzera mwa Iye ndipo anazilengera Iyeyo. 17Iyeyo analipo zinthu zonse zisanalengedwe ndipo zinthu zonse zimamangika pamodzi mwa Iye. 18Iye ndiyenso mutu wa thupi, limene ndi mpingo. Iye ndiye chiyambi chake, woyamba kuuka kwa akufa, kuti Iyeyo akhale wopambana zonse. 19Pakuti kunamukomera Mulungu kuti umulungu wake wonse ukhalemo mwa Khristu. 20Ndipo kudzera mwa Iye Mulungu ayanjanitsenso zinthu zonse ndi Iye mwini, zinthu za pa dziko lapansi, kapena zinthu za kumwamba. Iye anachita mtendere kudzera mʼmagazi ake, wokhetsedwa pa mtanda.

21Kale inu munali kutali ndi Mulungu ndipo munali adani a Mulungu mʼmaganizo mwanu chifukwa cha khalidwe lanu loyipa. 22Koma tsopano Iye anakuyanjanitsani mʼthupi la Khristu kudzera mu imfa kuti akuperekeni pamaso pake oyera, opanda banga ndi opanda chotsutsidwa nacho 23ngati mupitirirabe kukhala mʼchikhulupiriro chanu, okhazikika ndi olimba, osasunthidwa kuchoka pa chiyembekezo chimene munachigwira mu Uthenga Wabwino. Uwu ndi Uthenga Wabwino umene munawumva, umene wakhala ukulalikidwa kwa olengedwa onse a pansi pa thambo, ndi umenenso, ine Paulo ndinakhala mtumiki wake.

Utumiki wa Paulo ku Mpingo

24Tsopano ine ndikukondwa kuti ndinavutika chifukwa cha inu, ndipo ndikukwaniritsa mʼthupi langa zimene zikuperewera pa masautso a Khristu, chifukwa cha thupi lake, limene ndi Mpingo. 25Ine ndakhala mtumiki wake mwa lamulo limene Mulungu anandipatsa kuti ndipereke Mawu a Mulungu athunthu, 26chinsinsi chimene chakhala chikubisika kwa nthawi ndi mibado, koma tsopano chawululidwa kwa oyera mtima. 27Kwa iwo amene Mulungu anawasankha kuti awadziwitse pakati pa a mitundu ina, ulemerero wa chuma cha chinsinsi ichi, amene ndi Khristu mwa inu, chiyembekezo cha ulemerero.

28Ife tikulalikira Khristu, kulangiza ndi kuphunzitsa aliyense mwa nzeru zonse kuti timupereke aliyense wangwiro mwa Khristu. 29Ndi cholinga chimenechi, ine ndikugwira ntchito molimbika ndi mwamphamvu zonse zimene Iye anachita mwa ine.

New Russian Translation

Колоссянам 1:1-29

1От Павла, по воле Бога апостола Иисуса Христа, и от брата Тимофея.

2Святым и верным братьям во Христе, находящимся в Колоссах.

Благодать и мир вам от Бога, нашего Отца.

Благодарность Богу и молитва за церковь в Колоссах

3Мы всегда в молитвах благодарим за вас Бога – Отца нашего Господа Иисуса Христа, 4потому что до нас доходят слухи о вашей вере в Иисуса Христа и о вашей любви ко всем святым. 5Ваши вера и любовь порождены надеждой – той, что дожидается вас на небесах. Вы слышали о ней раньше в слове истины – Радостной Вести, 6которая пришла и к вам. Эта Весть распространяется и приносит плоды по всему миру, как и у вас с того дня, когда вы впервые услышали ее и познали истину о благодати Божьей. 7Вы узнали о ней от Эпафраса, нашего любимого сотрудника, который верно служит Христу ради вас1:7 Или: «ради нас».. 8Он и рассказал нам о любви, которую дал вам Дух.

9Поэтому, с тех пор как мы о вас впервые услышали, мы постоянно о вас молимся и просим, чтобы Бог дал вам знание Его воли, мудрость и духовное понимание. 10Мы молимся о том, чтобы вы жили достойно Господа и во всем угождали Ему, принося плоды ваших добрых дел и все больше узнавая Бога, 11чтобы вы укреплялись через Его силу и величие, становясь выносливыми, терпеливыми и радостными. 12Благодарите Отца, Который сделал вас достойными получить часть в наследии святых во свете. 13Он избавил нас от власти тьмы и ввел нас в Царство Своего любимого Сына, 14через жертвенную смерть Которого мы обрели искупление, прощение грехов.

Иисус Христос превыше всего творения

15Он – видимый образ невидимого Бога,

и Он превыше1:15 Слово, стоящее в тексте на языке оригинала, включает в себя и второе значение: «источник». всего творения.

16Через Него было сотворено все на небе и на земле,

все видимое и невидимое:

будь то престолы, господства, начальства или власти –

все было сотворено через Него и для Него.

17Еще до того, как все было сотворено,

Он уже существовал,

и все творение держится благодаря Ему.

18Он – глава тела, то есть Церкви,

Он начало всего, первый среди воскресших из мертвых1:18 Первый среди воскресших из мертвых – Лазарь и другие, которые были воскрешены до Иисуса, вновь умерли, но Иисус воскрес, чтобы жить вечно.,

чтобы во всем иметь первенство.

19Богу было угодно, чтобы во Христе обитала вся полнота,

20и чтобы через Него примирить с Собою все,

заключив благодаря Его крови,

пролитой на кресте, мир со всем,

что на небесах и на земле.

21Когда-то вы были далеки от Бога и враждебны Ему в своем разуме, направленном на злые дела. 22Но сейчас Бог примирил вас с Собой через жертвенную смерть Христа, когда Тот был еще в Своем земном теле. Он поставит вас перед Собою как святых и непорочных, и не заслуживающих упрека, 23если вы будете стоять на твердом основании веры и не станете изменять надежде, которую вам дала услышанная вами Радостная Весть. Она была возвещена всему творению под небесами, и я, Павел, стал ее служителем.

Служение Павла Церкви

24Теперь я радуюсь в моих страданиях за вас. Я в своем теле восполняю ту меру страданий Христа, которая предназначена мне, ради Его тела, то есть ради Церкви. 25Я стал ее служителем по поручению Бога, чтобы представить вам во всей полноте Его слово, 26которое оставалось тайной для людей из века в век и из поколения в поколение, а сейчас оно открывается Его святым. 27Бог захотел открыть им, как велико и для язычников богатство славы этой тайны, которая заключается в том, что Христос живет в вас. Он – ваша надежда на будущую славу.

28Мы возвещаем о Нем, наставляя и уча каждого человека. Мы используем всю мудрость, чтобы сделать каждого зрелым христианином. 29Ради этого я, собственно, и тружусь, и борюсь, применяя силу, исходящую от Него, которая мощно действует во мне.