Ahebri 8 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ahebri 8:1-13

Mkulu wa Ansembe wa Pangano Latsopano

1Fundo yayikulu pa zimene tikunenazi ndi iyi: Tili naye ife Mkulu wa ansembe, amene anakhala ku dzanja lamanja la mpando waufumu wa Mulungu Waulemerero kumwamba. 2Ndipo akutumikira mʼmalo opatulika, mu Tenti yeniyeni yoyikidwa ndi Ambuye, osati ndi munthu.

3Mkulu wa ansembe aliyense amasankhidwa kuti azipereka mphatso ndi nsembe kwa Mulungu, ndipo kunali koyenera kuti wansembe wathunso akhale nʼkanthu kopereka. 4Ngati iye akanakhala pa dziko lapansi, sakanakhala wansembe pakuti alipo kale anthu amene amapereka mphatso zolembedwa mʼMalamulo. 5Iwo amatumikira pamalo opatulika amene ndi chithunzi ndi chifanizo cha zimene zili kumwamba. Ichi ndi chifukwa chake Mose anachenjezedwa pamene anali pafupi kumanga Tenti: “Uwonetsetse kuti wapanga zonse monga momwe ndikukuonetsera pa phiri pano.” 6Koma Yesu analandira utumiki wopambana kuposa wawo monga Iyenso ali Nkhoswe ya pangano lopambana kuposa lakale lija, chifukwa pangano latsopano lakhazikika pa malonjezano opambana kwambiri.

7Ngati pangano loyamba lija likanakhala langwiro, sipakanafunikanso lina mʼmalo mwake. 8Koma Mulungu anapeza zolakwika pakati pa anthu ndipo anati,

“Masiku akubwera,” akutero Yehova,

“pamene ndidzachita pangano latsopano

ndi Aisraeli

ndiponso nyumba ya Yuda.

9Silidzakhala ngati pangano

limene ndinachita ndi makolo awo,

pamene ndinawagwira padzanja

nʼkuwatulutsa ku Igupto

chifukwa iwo sanasunge pangano langa lija

ndipo Ine sindinawasamalire,

akutero Ambuye.

10Tsono ili ndi pangano ndidzapangane ndi nyumba ya Israeli:

Atapita masiku amenewa, akutero Ambuye,

Ine ndidzayika malamulo anga mʼmaganizo mwawo,

ndi kulemba mʼmitima mwawo.

Ine ndidzakhala Mulungu wawo,

ndipo iwo adzakhala anthu anga.

11Sipadzafunikanso wina kuti aphunzitse mnzake,

kapena munthu kuphunzitsa mʼbale wake, kunena kuti, udziwe Ambuye

chifukwa onse adzandidziwa,

kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu.

12Pakuti Ine ndidzawakhululukira zoyipa zawo,

ndipo sindidzakumbukiranso machimo awo.”

13Ponena kuti, pangano “latsopano” Mulungu wapanga pangano loyamba lija kukhala lotha ntchito, ndipo chilichonse chimene chayamba kutha ntchito ndi kukalamba, chili pafupi kuchokeratu.

Nueva Versión Internacional

Hebreos 8:1-13

El sumo sacerdote de un nuevo pacto

1Ahora bien, el punto principal de lo que venimos diciendo es este: tenemos un sumo sacerdote que se sentó a la derecha del trono de la Majestad en el cielo 2y que sirve en el santuario, es decir, en el verdadero santuario levantado por el Señor y no por ningún ser humano.

3A todo sumo sacerdote se le nombra para presentar ofrendas y sacrificios, por lo cual fue necesario que Jesús también tuviera algo que ofrecer. 4Si él estuviera en la tierra, no sería sacerdote, pues aquí ya hay sacerdotes que presentan las ofrendas en conformidad con la Ley. 5Estos sacerdotes sirven en un santuario que es copia y sombra del que está en el cielo, tal como se le advirtió a Moisés cuando estaba a punto de construir el santuario: «Asegúrate de hacerlo todo según el modelo que se te ha mostrado en el monte».8:5 Éx 25:40. 6Pero el servicio sacerdotal que Jesús ha recibido es superior al de ellos, así como el pacto del cual es mediador es superior al antiguo, puesto que se basa en mejores promesas.

7Porque si ese primer pacto hubiera sido perfecto, no habría necesidad de proveer un segundo pacto. 8Pero Dios, reprochándoles sus defectos, dijo:

«Vienen días», afirma el Señor,

«en que haré un nuevo pacto

con Israel y con Judá.

9No será un pacto

como el que hice con sus antepasados

el día en que los tomé de la mano

y los saqué de Egipto,

ya que ellos no permanecieron fieles a mi pacto,

y yo los abandoné»,

dice el Señor.

10«Este es el pacto que después de aquel tiempo

haré con el pueblo de Israel», afirma el Señor.

«Pondré mis leyes en su mente

y las escribiré en su corazón.

Yo seré su Dios

y ellos serán mi pueblo.

11Ya no tendrá nadie que enseñar a su prójimo;

tampoco dirá nadie a su hermano: “¡Conoce al Señor!”,

porque todos, desde el más pequeño hasta el más grande, me conocerán.

12Yo perdonaré sus iniquidades

y nunca más me acordaré de sus pecados».8:12 Jer 31:31-34.

13Al llamar «nuevo» a ese pacto, ha declarado obsoleto al anterior; y lo que se vuelve obsoleto y envejece ya está por desaparecer.