Ahebri 10 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ahebri 10:1-39

Yesu Nsembe ya Anthu Onse

1Malamulo ndi chithunzithunzi cha zinthu zabwino zimene zikubwera, osati madalitso enieniwo. Pa chifukwa chimenechi sizingatheke konse kuti nsembe zimodzimodzi, zoperekedwa kawirikawiri, kosalekeza ndi chaka ndi chaka, kuti nʼkusandutsa angwiro amene amabwera kudzapembedza. 2Ngati zikanamatero iwowo akanasiya kupereka nsembezo. Pakuti opembedzawo akanamayeretsedwa kamodzi kokha, sibwenzi chikumbumtima chawo chikuwatsutsabe chifukwa cha machimo awo. 3Koma nsembezo zimawakumbutsa anthuwo machimo awo chaka ndi chaka. 4Chifukwa nʼkosatheka kuti magazi angʼombe yayimuna ndi mbuzi yayimuna achotse machimo.

5Nʼchifukwa chake Khristu atabwera pa dziko lapansi anati,

“Simunafune nsembe kapena zopereka,

koma thupi munandikonzera.

6Simunakondwere nazo nsembe zopsereza

ndi nsembe zopereka chifukwa cha tchimo.

7Tsono, Ine ndinati, ‘Ndili pano Ine,

Inu Mulungu, ndabwera kudzachita zimene mukufuna monga zinalembedwa mʼMalemba.’ ”

8Poyamba Iye anati, “Nsembe kapena zopereka zopsereza ndi nsembe zopereka chifukwa cha tchimo, Inu simunazifune kapena kukondwera nazo.” Ngakhale kuti Malamulo ndiye amanena kuti ziperekedwe. 9Pamenepo Iye anati, “Ndili pano Ine, ndabwera kudzachita zimene mukufuna.” Khristu anachotsa nsembe zoyamba zija kuti mʼmalo mwake ayikemo nsembe za mtundu wachiwiri. 10Chifukwa chakuti Yesu Khristu anachita zimene Mulungu anafuna kuti achite, ndife oyeretsedwa ndi nsembe ya thupi lake, limene analipereka kamodzi kokha.

11Wansembe aliyense amayimirira tsiku ndi tsiku nʼkutumikira, ndipo amapereka nsembe imodzimodzi mobwerezabwereza, nsembe zimene sizingathe kuchotsa machimo. 12Koma pamene wansembe uyu anapereka kamodzi kokha nsembe imodzi yokha chifukwa cha machimo, Iye anakhala pansi ku dzanja lamanja la Mulungu. 13Kumeneko akudikira tsono kuti Mulungu asandutse adani ake kukhala chopondapo mapazi ake. 14Chifukwa cha nsembe imodzi Iye anasandutsa angwiro kwamuyaya iwo amene akuwayeretsa.

15Mzimu Woyera nayenso akuchitira umboni za zimenezi kwa ife. Poyamba Iye anati,

16“Ili ndi pangano limene ndidzachita nawo

atapita masiku amenewo,” akutero Yehova.

“Ndidzayika malamulo anga mʼmitima mwawo,

ndipo ndidzawalemba mʼmaganizo mwawo.”

17Ndipo akutinso:

“Sindidzakumbukiranso konse

machimo awo ndi zolakwa zawo.”

18Ndipo pamene machimo akhululukidwa, sipafunikanso nsembe yoperekedwa chifukwa cha machimowo.

Kulimbika Mtima ndi Kupirira pa Chikhulupiriro

19Ndipo tsono abale, molimba mtima timalowa mʼMalo Opatulika kwambiri chifukwa cha magazi a Yesu. 20Iye anatitsekulira njira yatsopano ndi yamoyo kudutsa chinsalu chotchinga, chimene ndi thupi lake. 21Ndiponso tili ndi wansembe wamkulu woyangʼanira nyumba ya Mulungu. 22Tsono tiyeni tiyandikire kwa Mulungu ndi mtima woona ndi wodzaza ndi chikhulupiriro. Popeza mitima yathu yayeretsedwa, ndi yopanda chikumbumtima chotitsutsa, ndiponso matupi athu asambitsidwa ndi madzi woyera. 23Tiyeni tigwiritsitse mosagwedezeka zimene timaziyembekezera ndi kuzivomereza, pakuti amene anatilonjezayo ndi wokhulupirika. 24Tiziganizira mmene tingalimbikitsirane wina ndi mnzake pokondana ndi kuchita ntchito zabwino. 25Tiyeni tisaleke kusonkhana kwathu pamodzi monga mmene ena amachitira, koma tizilimbikitsana makamaka poona kuti tsiku la Ambuye layandikira.

26Ngati ife tipitirira kuchimwa mwadala pamene tikudziwa choona, palibenso nsembe ina imene ingaperekedwe chifukwa cha machimo athuwo. 27Koma kumangodikira kokha ndi mantha chiweruzo ndiponso moto woopsa umene udzawononga adani a Mulungu 28Aliyense amene amakana malamulo a Mose amaphedwa popanda nʼchifundo chomwe, malingana pali mboni ziwiri kapena zitatu. 29Koposa kotani nanga ululu wachilango chimene adzalandire munthu amene amapeputsa Mwana wa Mulungu, amene amayesa magazi a pangano, amene anamuyeretsa, kukhala chinthu chodetsedwa, ndi kunyoza Mzimu wachisomo? 30Pakuti timadziwa amene anati, “Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine.” Iye anatinso, “Ambuye adzaweruza anthu ake.” 31Nʼchinthu choopsa kugwa mʼmanja a Mulungu wamoyo.

32Kumbukirani masiku akale aja mutangowunikiridwa chatsopano, pa nthawi imeneyi munapirira zowawa zambiri. 33Nthawi zina ankakunyozani pagulu ndi kukuzunzani. Nthawi zina munkamva zowawa pamodzi ndi amene ankasautsidwa chotere. 34Munkawamvera chisoni amene anali mʼndende ndiponso munkalola mokondwera kuti akulandeni katundu wanu chifukwa munkadziwa kuti muli nacho chuma choposa ndi chosatha.

35Tsono musataye kulimbika mtima kwanuko pakuti mudzalandira nako mphotho yayikulu. 36Nʼkofunika kuti mupirire kuti pamene muchita chifuniro cha Mulungu mudzalandire zimene Iye analonjeza. 37Pakuti nʼkanthawi kochepa chabe,

Iye amene akubwera adzabwera ndipo sadzachedwa ayi.

38Koma wolungama wangayo adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.

Ndipo ngati iye abwerera mʼmbuyo chifukwa cha mantha,

Ine sindidzakondwera naye.

39Koma ife sindife amodzi a iwo obwerera mʼmbuyo mwa mantha ndi owonongedwa, koma ndife amodzi a amene akukhulupirira ndi wopulumutsidwa.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

希伯来书 10:1-39

永远的赎罪祭

1律法只是将来美事的一个投影,并非本体的真像,所以年复一年的献祭不能使前来敬拜的人纯全。 2否则,献祭的事早已终止了,因为敬拜的人若献一次祭就能彻底得到洁净,他们就不再觉得有罪了。 3然而,每年献祭的事都使人想起自己的罪来, 4因为公牛和山羊的血根本不能除去人的罪。

5所以,基督来到世上的时候曾说:

“上帝啊,祭物和供物非你所悦,

你为我预备了身体。

6你并非喜爱燔祭和赎罪祭。

7于是我说,

‘上帝啊,我来是要遵行你的旨意,

我的事都记在圣经上了。’”

8基督首先说:“祭物、供物、燔祭和赎罪祭都不是你想要的,也不是你喜悦的。”这些都是依照律法献上的。 9然后祂又说:“我来是要遵行你的旨意。”这样,祂废除了前者,为要设立后者。 10上帝的旨意是:耶稣基督只一次献上自己的身体,便使我们永远圣洁了。

11祭司都要天天站着供职,一次次地献上同样的祭物,只是这些祭物根本不能除罪。 12而基督一次献上自己成为永远的赎罪祭后,就坐在上帝的右边, 13等待祂的仇敌成为祂的脚凳。 14祂凭自己的一次牺牲,使那些得以圣洁的人永远纯全。

15圣灵也向我们做见证,说:

16“主说,那些日子以后,

我将与他们立这样的约,

我要把我的律例放在他们心中,

写在他们脑中。

17我要忘记他们的过犯和罪恶。”

18既然过犯和罪恶已经得到赦免,就不需要再为罪献祭了。

坚忍到底

19-20弟兄姊妹,耶稣已用宝血为我们开辟了一条又新又活的路,使我们可以穿过幔子,就是祂的身体,坦然进入至圣所。 21并且,我们有一位大祭司管理上帝的家, 22祂洁净了我们被罪困扰的良心,用清水洗净了我们的身体。因此,我们要信心十足、真诚地到上帝面前。 23我们要坚定不移地持守我们所认定的盼望,因为赐应许的那位是信实的。 24我们要想办法彼此相顾,激发爱心,勉励行善。 25不要停止聚会,像那些停止惯了的人,要互相鼓励,特别是你们知道主再来的日子近了。

26因为我们知道了真理以后,若仍然故意犯罪,就再没有赎罪祭了, 27只有可怕的审判和烧灭敌对者的烈火等候我们。 28人违犯摩西的律法,经两三个人指证后,尚且被毫不留情地处死, 29更何况人践踏上帝的儿子,轻看那使人圣洁的立约之血,又藐视赐人恩典的圣灵?这等人该受多么重的刑罚啊! 30我们知道上帝说过:“申冤在我,我必报应。”祂又说:“主要审判祂的百姓。” 31落在永活上帝的手中是可怕的!

32你们要回想当初的日子,那时你们蒙了光照以后,忍受了各种苦难的煎熬。 33有时候,你们在众目睽睽之下被辱骂,受迫害;有时候,你们和遭受这样苦难的人同舟共济。 34你们体恤那些坐牢的人,即使你们的家业被抢夺,仍然甘心忍受,因为你们知道自己有更美的、永远长存的家业。 35所以切勿失去勇敢的心,因为勇敢的心会给你们带来大赏赐。 36你们需要坚忍到底,这样你们遵行了上帝的旨意后,便可以得到祂的应许。

37因为“将要来临的那位很快要来了,绝不迟延。 38属我的义人必靠信心而活。他若畏缩退后,我必不喜悦他。” 39但我们都不是退后走向灭亡的人,而是因为有信心而灵魂得救的人。