Ahebri 1 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ahebri 1:1-14

Khristu Mwana wa Mulungu Aposa Angelo

1Kale lija Mulungu ankayankhula ndi makolo athu pa nthawi zosiyanasiyana ndiponso mwa njira zosiyanasiyana kudzera mwa aneneri. 2Koma masiku otsiriza ano, Mulungu wayankhula nafe kudzera mwa Mwana wake. Mwanayu anamusankha kuti akhale mwini wa zinthu zonse, ndiponso Mulungu analenga dziko lonse kudzera mwa Iye. 3Mwanayo ndiye kuwala kwa ulemerero wa Mulungu, chithunzithunzi chenicheni cha khalidwe lake. Iyeyu amachirikiza zinthu zonse ndi mphamvu ya mawu ake. Iye atayeretsa anthu kuchoka ku machimo awo, anakhala pansi kumwamba kudzanja lamanja la Mulungu waulemerero. 4Mwanayu ndi wamkulu koposa angelo, monga momwe dzina limene analandira limaposa dzina la angelo.

5Kodi ndi kwa mngelo uti, kumene Mulungu anati,

“Iwe ndiwe mwana wanga;

Ine lero ndakhala Atate ako.”

Kapena kunenanso kuti,

“Ine ndidzakhala abambo ake;

iye adzakhala mwana wanga.”

6Pamene Mulungu amatuma Mwana wake woyamba kubadwa ku dziko lapansi anati,

“Angelo onse a Mulungu amupembedze Iye.”

7Iye ponena za angelo akuti,

“Mulungu amasandutsa angelo ake mphepo,

amasandutsa atumiki ake malawi amoto.”

8Koma za Mwana wake akuti,

“Inu Mulungu, mpando wanu waufumu udzakhala mpaka muyaya,

ndipo mudzaweruza molungama mu ufumu wanu.

9Mwakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa;

Nʼchifukwa chake, Mulungu wanu wakukwezani kuposa anzanu

pokudzozani mafuta osonyeza chimwemwe.”

10Mulungu akutinso,

“Ambuye, pachiyambi Inu munayika maziko a dziko lapansi;

ndipo zakumwambako ndi ntchito za manja anu.

11Zimenezi zidzatha, koma Inu ndinu wachikhalire.

Izo zidzatha ngati zovala.

12Mudzazipindapinda ngati chofunda;

ndipo zidzasinthidwa ngati chovala.

Koma Inu simudzasintha,

ndipo zaka zanu sizidzatha.”

13Kodi ndi kwa Mngelo uti kumene Mulungu ananenapo kuti,

“Khala kudzanja langa lamanja

mpaka nditapanga adani ako

kukhale chopondapo mapazi ako.”

14Kodi angelo onse si mizimu yotumikira odzalandira chipulumutso?

Nova Versão Internacional

Hebreus 1:1-14

O Filho é Superior aos Anjos

1Há muito tempo Deus falou muitas vezes e de várias maneiras aos nossos antepassados por meio dos profetas, 2mas nestes últimos dias falou-nos por meio do Filho, a quem constituiu herdeiro de todas as coisas e por meio de quem fez o universo. 3O Filho é o resplendor da glória de Deus e a expressão exata do seu ser, sustentando todas as coisas por sua palavra poderosa. Depois de ter realizado a purificação dos pecados, ele se assentou à direita da Majestade nas alturas, 4tornando-se tão superior aos anjos quanto o nome que herdou é superior ao deles.

5Pois a qual dos anjos Deus alguma vez disse:

“Tu és meu Filho;

eu hoje te gerei”1.5 Sl 2.7?

E outra vez:

“Eu serei seu Pai,

e ele será meu Filho”1.5 2Sm 7.14; 1Cr 17.13?

6E ainda, quando Deus introduz o Primogênito no mundo, diz:

“Todos os anjos de Deus o adorem”1.6 Dt 32.43 (segundo a Septuaginta e os manuscritos do mar Morto)..

7Quanto aos anjos, ele diz:

“Ele faz dos seus anjos ventos,

e dos seus servos, clarões reluzentes”1.7 Sl 104.4.

8Mas a respeito do Filho, diz:

“O teu trono, ó Deus, subsiste para todo o sempre;

cetro de equidade é o cetro do teu Reino.

9Amas a justiça e odeias a iniquidade;

por isso Deus, o teu Deus,

escolheu-te dentre os teus companheiros,

ungindo-te com óleo de alegria”1.8,9 Sl 45.6,7.

10E também diz:

“No princípio, Senhor, firmaste os fundamentos da terra,

e os céus são obras das tuas mãos.

11Eles perecerão, mas tu permanecerás;

envelhecerão como vestimentas.

12Tu os enrolarás como um manto,

como roupas eles serão trocados.

Mas tu permaneces o mesmo,

e os teus dias jamais terão fim”1.10-12 Sl 102.25-27.

13A qual dos anjos Deus alguma vez disse:

“Senta-te à minha direita,

até que eu faça dos teus inimigos

um estrado para os teus pés”1.13 Sl 110.1?

14Os anjos não são, todos eles, espíritos ministradores enviados para servir aqueles que hão de herdar a salvação?