Ahebri 1 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ahebri 1:1-14

Khristu Mwana wa Mulungu Aposa Angelo

1Kale lija Mulungu ankayankhula ndi makolo athu pa nthawi zosiyanasiyana ndiponso mwa njira zosiyanasiyana kudzera mwa aneneri. 2Koma masiku otsiriza ano, Mulungu wayankhula nafe kudzera mwa Mwana wake. Mwanayu anamusankha kuti akhale mwini wa zinthu zonse, ndiponso Mulungu analenga dziko lonse kudzera mwa Iye. 3Mwanayo ndiye kuwala kwa ulemerero wa Mulungu, chithunzithunzi chenicheni cha khalidwe lake. Iyeyu amachirikiza zinthu zonse ndi mphamvu ya mawu ake. Iye atayeretsa anthu kuchoka ku machimo awo, anakhala pansi kumwamba kudzanja lamanja la Mulungu waulemerero. 4Mwanayu ndi wamkulu koposa angelo, monga momwe dzina limene analandira limaposa dzina la angelo.

5Kodi ndi kwa mngelo uti, kumene Mulungu anati,

“Iwe ndiwe mwana wanga;

Ine lero ndakhala Atate ako.”

Kapena kunenanso kuti,

“Ine ndidzakhala abambo ake;

iye adzakhala mwana wanga.”

6Pamene Mulungu amatuma Mwana wake woyamba kubadwa ku dziko lapansi anati,

“Angelo onse a Mulungu amupembedze Iye.”

7Iye ponena za angelo akuti,

“Mulungu amasandutsa angelo ake mphepo,

amasandutsa atumiki ake malawi amoto.”

8Koma za Mwana wake akuti,

“Inu Mulungu, mpando wanu waufumu udzakhala mpaka muyaya,

ndipo mudzaweruza molungama mu ufumu wanu.

9Mwakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa;

Nʼchifukwa chake, Mulungu wanu wakukwezani kuposa anzanu

pokudzozani mafuta osonyeza chimwemwe.”

10Mulungu akutinso,

“Ambuye, pachiyambi Inu munayika maziko a dziko lapansi;

ndipo zakumwambako ndi ntchito za manja anu.

11Zimenezi zidzatha, koma Inu ndinu wachikhalire.

Izo zidzatha ngati zovala.

12Mudzazipindapinda ngati chofunda;

ndipo zidzasinthidwa ngati chovala.

Koma Inu simudzasintha,

ndipo zaka zanu sizidzatha.”

13Kodi ndi kwa Mngelo uti kumene Mulungu ananenapo kuti,

“Khala kudzanja langa lamanja

mpaka nditapanga adani ako

kukhale chopondapo mapazi ako.”

14Kodi angelo onse si mizimu yotumikira odzalandira chipulumutso?

Knijga O Kristu

Hebrejima 1:1-14

Isus Krist je Božji Sin

1Bog je nekoć više puta i na mnoge načine govorio našim precima kroz proroke. 2Ali u ove zadnje dane nama je progovorio kroz svojega Sina. Njega, po kojemu je sve stvorio, postavio je za baštinika svega. 3Sin je odsjaj Božje slave i otisak njegova Bića. On održava svemir snagom svoje silne riječi. Pošto je umro da nas očisti od grijeha, sjeo je na počasno mjesto, zdesna veličanstvenome Bogu u nebu.

Isus je uzvišeniji od anđela

4To pokazuje da je Božji Sin mnogo uzvišeniji od anđela, kao što je i ime koje je baštinio uzvišenije od njihovih imena. 5Jer kome je od anđela ikada rekao:

“Ti si moj Sin,

danas sam ti postao Ocem”1:5 Psalam 2:7.,

i još:

“Ja ću mu biti Otac,

a on će meni biti Sin”1:5 2 Samuelova 7:14.?

6A kada je predstavio svojeg prvorođenca svijetu, Bog je rekao:

“Klanjajte mu se, svi anđeli Božji!”1:6 Ponovljeni zakon 32:43.

7Za anđele kaže:

“On čini svoje anđele vjetrovima

i sluge poput ognjenih plamenova.”1:7 Psalam 104:4.

8Ali za svojega Sina kaže:

“Tvoje kraljevstvo, o Bože, traje zauvijek.

Ti vladaš žezlom pravednosti.

9Ti ljubiš pravednost i mrziš nepravednost.

Zato te je, Bože, tvoj Bog, pomazao

uljem radosti više nego ijednoga tvojeg druga.”1:8-9 Psalam 45:7-8.

10I još:

“Gospodine, u početku si postavio temelje zemlji

i nebesa su djelo tvojih ruku.

11Čak će i ona nestati,

ali ti ostaješ zauvijek.

12Smotat ćeš ih poput starog kaputa

i nestat će kao stara odjeća.

Ali ti si uvijek isti;

tvojim godinama nema svršetka.”1:10-12 Psalam 102:26-28.

13Bog nikada nije nekom anđelu rekao:

“Sjedni mi s desne strane

dok ti ne bacim pod noge tvoje neprijatelje.”1:13 Psalam 110:1.

14Jer anđeli su samo poslužnički duhovi koje Bog šalje služiti onima koji će baštiniti spasenje.