Ahebri 1 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ahebri 1:1-14

Khristu Mwana wa Mulungu Aposa Angelo

1Kale lija Mulungu ankayankhula ndi makolo athu pa nthawi zosiyanasiyana ndiponso mwa njira zosiyanasiyana kudzera mwa aneneri. 2Koma masiku otsiriza ano, Mulungu wayankhula nafe kudzera mwa Mwana wake. Mwanayu anamusankha kuti akhale mwini wa zinthu zonse, ndiponso Mulungu analenga dziko lonse kudzera mwa Iye. 3Mwanayo ndiye kuwala kwa ulemerero wa Mulungu, chithunzithunzi chenicheni cha khalidwe lake. Iyeyu amachirikiza zinthu zonse ndi mphamvu ya mawu ake. Iye atayeretsa anthu kuchoka ku machimo awo, anakhala pansi kumwamba kudzanja lamanja la Mulungu waulemerero. 4Mwanayu ndi wamkulu koposa angelo, monga momwe dzina limene analandira limaposa dzina la angelo.

5Kodi ndi kwa mngelo uti, kumene Mulungu anati,

“Iwe ndiwe mwana wanga;

Ine lero ndakhala Atate ako.”

Kapena kunenanso kuti,

“Ine ndidzakhala abambo ake;

iye adzakhala mwana wanga.”

6Pamene Mulungu amatuma Mwana wake woyamba kubadwa ku dziko lapansi anati,

“Angelo onse a Mulungu amupembedze Iye.”

7Iye ponena za angelo akuti,

“Mulungu amasandutsa angelo ake mphepo,

amasandutsa atumiki ake malawi amoto.”

8Koma za Mwana wake akuti,

“Inu Mulungu, mpando wanu waufumu udzakhala mpaka muyaya,

ndipo mudzaweruza molungama mu ufumu wanu.

9Mwakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa;

Nʼchifukwa chake, Mulungu wanu wakukwezani kuposa anzanu

pokudzozani mafuta osonyeza chimwemwe.”

10Mulungu akutinso,

“Ambuye, pachiyambi Inu munayika maziko a dziko lapansi;

ndipo zakumwambako ndi ntchito za manja anu.

11Zimenezi zidzatha, koma Inu ndinu wachikhalire.

Izo zidzatha ngati zovala.

12Mudzazipindapinda ngati chofunda;

ndipo zidzasinthidwa ngati chovala.

Koma Inu simudzasintha,

ndipo zaka zanu sizidzatha.”

13Kodi ndi kwa Mngelo uti kumene Mulungu ananenapo kuti,

“Khala kudzanja langa lamanja

mpaka nditapanga adani ako

kukhale chopondapo mapazi ako.”

14Kodi angelo onse si mizimu yotumikira odzalandira chipulumutso?

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

希伯来书 1:1-14

划时代的启示

1在古代,上帝曾借着先知以各种方式多次向我们的祖先说话; 2在这世界的末期,祂又借着自己的儿子亲自向我们说话。上帝早已立祂承受万物,并借着祂创造了宇宙万物。 3祂正是上帝荣耀的光辉,是上帝本体的真像。祂用自己充满能力的话语维系万物。祂洗净了世人的罪之后,便坐在天上至高上帝的右边。 4祂既承受了比天使更高的名分,就远超越天使。

5上帝从未对任何一个天使说:

“你是我的儿子,我今日成为你父亲。”

或说:

“我要做你的父亲,你要做我的儿子。”

6上帝差遣祂的长子到世上来时,说:

“上帝的天使都要敬拜祂。”

7上帝提到天使的时候,也只是说:

“上帝使祂的天使成为风,使祂的仆役成为火焰。”

8但论到祂的儿子,祂却说:

“上帝啊,你的宝座永远长存,

你以公义的杖执掌王权。

9你喜爱公义,憎恶邪恶。

所以上帝,你的上帝,

用喜乐之油膏你,使你超过同伴。”

10此外又说:

“主啊,太初你奠立大地的根基,

亲手创造诸天。

11天地都要消亡,但你永远长存。

天地都会像衣服渐渐破旧,

12你要像卷外衣一样把天地卷起来。

天地将如衣服一样被更换,

但你永远不变,

你的年日永无穷尽。”

13上帝从未对任何一个天使说:

“你坐在我的右边,

等我使你的仇敌成为你的脚凳。”

14天使岂不都是服役的灵吗?他们奉差遣,岂不是去为那些将要承受救恩的人服务吗?