Agalatiya 6 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Agalatiya 6:1-18

Kuchita Zabwino kwa Onse

1Abale, ngati munthu agwa mʼtchimo lililonse, inu amene Mzimu amakutsogolerani, mumuthandize munthuyo ndi mtima wofatsa kuti akonzekenso. Koma mukhale maso kuti inu nomwe mungayesedwe. 2Thandizanani kusenza zolemetsa zanu, ndipo mʼnjira imeneyi mudzakwanitsa lamulo la Khristu. 3Ngati wina adziyesa kanthu pamene iyeyo sali kanthu konse, akudzinamiza yekha. 4Munthu aliyense aziyesa yekha ntchito zake mmene zilili. Ngati zili bwino, adzatha kunyadira chifukwa cha ntchito zake zokhazo, iyeyo asadzifanizire ndi munthu wina wake, 5pakuti aliyense ayenera kusenza katundu wake.

6Koma munthu amene akuphunzira mawu, agawireko mphunzitsi wake zinthu zonse zabwino zimene iye ali nazo.

7Musanamizidwe: nʼkosatheka kupusitsa Mulungu. Munthu amakolola zimene wafesa. 8Pakuti amene amafesa zokondweretsa thupi lake la uchimo, kuchokera ku khalidwe limenelo adzakolola chiwonongeko; amene amafesa zokondweretsa Mzimu, kuchokera kwa Mzimu adzakolola moyo wosatha. 9Tisatope nʼkuchita zabwino, pakuti pa nthawi yoyenera tidzakolola ngati sititopa. 10Nʼchifukwa chake ngati tapeza mpata, tiyenera kuchitira zabwino anthu onse, makamaka amene ndi a banja la okhulupirira.

Osati Mdulidwe koma Kulengedwa Mwatsopano

11Onani zilembo zazikulu zimene ine ndikulemba ndi dzanja langa.

12Onse amene akufuna kuoneka abwino pamaso pa anthu akukukakamizani kuti muchite mdulidwe. Akuchita izi ndi cholinga chimodzi chokha, chakuti apewe kuzunzidwa chifukwa cha mtanda wa Khristu. 13Pakuti ngakhale iwowa amene anachita mdulidwe satsata Malamulo, komabe akufuna kuti muchite mdulidwe kuti anyadire mdulidwe wanuwo. 14Ine sindingathe kunyadira kanthu kena koma mtanda wa Ambuye athu Yesu Khristu, kudzera mwa mtandawo dziko lapansi linapachikidwa kwa ine ndi ine ku dziko lapansi. 15Pakuti kaya mdulidwe kapena kusachita mdulidwe, sizitanthauza kanthu; chofunika ndi kulengedwa mwatsopano. 16Mtendere ndi chifundo zikhale kwa onse amene amatsata chiphunzitso ichi, ndi pa Israeli wa Mulungu.

17Pomaliza wina asandivutitse, pakuti mʼthupi mwanga muli zizindikiro za Yesu.

18Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu zikhale ndi mzimu wanu abale. Ameni.

Thai New Contemporary Bible

กาลาเทีย 6:1-18

ทำดีต่อคนทั้งปวง

1พี่น้องทั้งหลาย หากใครถูกจับได้ว่าทำบาป ท่านที่อยู่ฝ่ายจิตวิญญาณควรช่วยเขาอย่างสุภาพอ่อนโยนให้เขากลับตั้งตัวใหม่ แต่จงระวังตัวท่านเอง มิฉะนั้นท่านเองจะถูกล่อลวงให้ทำบาปไปด้วย 2จงช่วยรับภาระของกันและกัน ทำดังนี้แล้วท่านก็ได้ปฏิบัติตามบทบัญญัติของพระคริสต์ 3หากผู้ใดคิดว่าตนสำคัญทั้งๆ ที่ไม่สำคัญ ผู้นั้นก็หลอกตัวเอง 4แต่ละคนควรสำรวจการกระทำของตนเองจึงจะมีข้อภาคภูมิใจในตัวเอง โดยไม่ต้องเอาตัวไปเปรียบเทียบกับคนอื่น 5เพราะว่าแต่ละคนต้องแบกภาระของตัวเอง

6ผู้ที่รับคำสั่งสอนจงแบ่งสิ่งดีทั้งปวงแก่ผู้สอน

7อย่าหลงเลย ท่านไม่อาจหลอกลวงพระเจ้า ใครหว่านอะไรย่อมเก็บเกี่ยวสิ่งนั้น 8ผู้ที่หว่านเพื่อวิสัยบาปของเขาจะเก็บเกี่ยวความพินาศจากวิสัยนั้น6:8 หรือเพื่อเนื้อหนังของเขาจะเก็บเกี่ยวความพินาศจากเนื้อหนังของเขา ส่วนผู้ที่หว่านเพื่อพระวิญญาณจะเก็บเกี่ยวชีวิตนิรันดร์จากพระวิญญาณ 9อย่าให้เราอ่อนล้าในการทำดี เพราะถ้าเราไม่ย่อท้อ เราก็จะเก็บเกี่ยวในเวลาอันเหมาะสม 10เหตุฉะนั้นเมื่อมีโอกาส ให้เราทำดีต่อคนทั้งปวง โดยเฉพาะอย่างยิ่งต่อคนที่อยู่ในครอบครัวแห่งความเชื่อ

ไม่ใช่เข้าสุหนัตแต่รับการทรงสร้างใหม่

11ดูเถิด ข้าพเจ้าใช้ตัวอักษรขนาดใหญ่เพียงไร เมื่อเขียนถึงท่านด้วยมือของข้าพเจ้าเอง!

12บรรดาผู้ที่อยากสร้างความประทับใจแต่เพียงเปลือกนอกพยายามบังคับให้ท่านเข้าสุหนัต เพียงเพื่อหลีกเลี่ยงไม่ให้ตนเองถูกข่มเหงเพราะเรื่องไม้กางเขนของพระคริสต์ 13แม้แต่คนที่เข้าสุหนัตแล้วยังไม่เชื่อฟังบทบัญญัติ แต่พวกเขาต้องการให้ท่านเข้าสุหนัตจะได้อวดอ้างเนื้อหนังของท่าน 14ขออย่าให้ข้าพเจ้าอวดอะไรเว้นแต่ไม้กางเขนขององค์พระเยซูคริสต์เจ้าของเรา โดยไม้กางเขนนั้น6:14 หรือโดยผู้นั้น โลกถูกตรึงไว้จากข้าพเจ้าแล้วและข้าพเจ้าถูกตรึงไว้จากโลกแล้ว 15เข้าสุหนัตหรือไม่เข้าสุหนัตก็ไม่มีความหมาย ความสำคัญอยู่ที่การได้รับการทรงสร้างใหม่ 16สันติสุขและพระเมตตาคุณจงมีแก่คนทั้งปวงที่ทำตามกฎนี้ คือแก่ชนอิสราเอลของพระเจ้า

17สุดท้ายนี้อย่าให้ใครมาก่อความเดือดร้อนแก่ข้าพเจ้า เพราะข้าพเจ้ามีเครื่องหมายของพระเยซูอยู่บนกายของข้าพเจ้า

18พี่น้องทั้งหลาย ขอให้พระคุณขององค์พระเยซูคริสต์เจ้าของเราดำรงอยู่กับวิญญาณจิตของท่านทั้งหลายเถิด อาเมน