Agalatiya 6 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Agalatiya 6:1-18

Kuchita Zabwino kwa Onse

1Abale, ngati munthu agwa mʼtchimo lililonse, inu amene Mzimu amakutsogolerani, mumuthandize munthuyo ndi mtima wofatsa kuti akonzekenso. Koma mukhale maso kuti inu nomwe mungayesedwe. 2Thandizanani kusenza zolemetsa zanu, ndipo mʼnjira imeneyi mudzakwanitsa lamulo la Khristu. 3Ngati wina adziyesa kanthu pamene iyeyo sali kanthu konse, akudzinamiza yekha. 4Munthu aliyense aziyesa yekha ntchito zake mmene zilili. Ngati zili bwino, adzatha kunyadira chifukwa cha ntchito zake zokhazo, iyeyo asadzifanizire ndi munthu wina wake, 5pakuti aliyense ayenera kusenza katundu wake.

6Koma munthu amene akuphunzira mawu, agawireko mphunzitsi wake zinthu zonse zabwino zimene iye ali nazo.

7Musanamizidwe: nʼkosatheka kupusitsa Mulungu. Munthu amakolola zimene wafesa. 8Pakuti amene amafesa zokondweretsa thupi lake la uchimo, kuchokera ku khalidwe limenelo adzakolola chiwonongeko; amene amafesa zokondweretsa Mzimu, kuchokera kwa Mzimu adzakolola moyo wosatha. 9Tisatope nʼkuchita zabwino, pakuti pa nthawi yoyenera tidzakolola ngati sititopa. 10Nʼchifukwa chake ngati tapeza mpata, tiyenera kuchitira zabwino anthu onse, makamaka amene ndi a banja la okhulupirira.

Osati Mdulidwe koma Kulengedwa Mwatsopano

11Onani zilembo zazikulu zimene ine ndikulemba ndi dzanja langa.

12Onse amene akufuna kuoneka abwino pamaso pa anthu akukukakamizani kuti muchite mdulidwe. Akuchita izi ndi cholinga chimodzi chokha, chakuti apewe kuzunzidwa chifukwa cha mtanda wa Khristu. 13Pakuti ngakhale iwowa amene anachita mdulidwe satsata Malamulo, komabe akufuna kuti muchite mdulidwe kuti anyadire mdulidwe wanuwo. 14Ine sindingathe kunyadira kanthu kena koma mtanda wa Ambuye athu Yesu Khristu, kudzera mwa mtandawo dziko lapansi linapachikidwa kwa ine ndi ine ku dziko lapansi. 15Pakuti kaya mdulidwe kapena kusachita mdulidwe, sizitanthauza kanthu; chofunika ndi kulengedwa mwatsopano. 16Mtendere ndi chifundo zikhale kwa onse amene amatsata chiphunzitso ichi, ndi pa Israeli wa Mulungu.

17Pomaliza wina asandivutitse, pakuti mʼthupi mwanga muli zizindikiro za Yesu.

18Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu zikhale ndi mzimu wanu abale. Ameni.

O Livro

Gálatas 6:1-18

Fazer o bem a todos

1Meus irmãos, se alguém vier a cometer pecado, aqueles de entre vocês que possuem uma mente espiritual procurem encaminhá-lo com bondade; e sem qualquer sentimento de superioridade, pois cada um de nós está sujeito a ser tentado. 2Partilhem uns com os outros o peso das vossas dificuldades e assim cumprirão o mandamento de Cristo. 3Se alguém se julga importante demais para ajudar a levar os fardos dos outros, está a iludir-se a si próprio.

4Que cada um verifique a sua própria conduta; e se houver razão para estar satisfeito, guarde esse sentimento para si, sem se comparar com os outros. 5Cada um terá de suportar as suas próprias responsabilidades.

6Aqueles que recebem instrução sobre a palavra de Deus devem repartir os seus recursos com aqueles que os instruem.

7Não se iludam: Deus não se deixa enganar! Toda a gente virá a ceifar aquilo que tiver semeado. 8Os que semeiam atos que resultam apenas de desejos e ambições humanas, virão a ceifar a corrupção. Mas os que semeiam coisas do domínio do Espírito, receberão do Espírito a vida eterna.

9Não nos cansemos então de fazer o bem, porque a seu tempo viremos a recolher muitas bênçãos, se formos perseverantes. 10E assim, sempre que tenhamos oportunidade, pratiquemos o bem para com todos, mas primeiramente para com os que têm a mesma fé que nós.

A nova criatura em Cristo

11Estas palavras sou eu próprio agora que as escrevo com estas grandes letras. 12Repito: esses que querem obrigar-vos a cumprir a circuncisão, fazem-no só por uma razão. Eles não querem ser perseguidos por ensinarem que só a cruz de Cristo pode salvar. 13Pois a verdade é que nem esses que se circuncidam conseguem guardar a Lei. Pretendem marcar-vos, no vosso corpo, com um sinal de que são seus discípulos.

14Quanto a mim, bem longe esteja a ideia de ter satisfação noutra coisa que não seja a cruz do nosso Senhor Jesus Cristo, pela qual eu morri para o mundo e o mundo deixou de ter qualquer valor para mim. 15Em Cristo, mais uma vez o digo, não interessa estar ou não circuncidado; o que conta é ser uma nova criatura. 16A todos os que andarem segundo esta regra de vida, que Deus lhes conceda a sua paz e misericórdia, bem como ao Israel de Deus.

17Peço-vos então que, daqui para o futuro, não tenha mais que me incomodar com dificuldades semelhantes a estas. Lembrem-se que trago no meu corpo as marcas daquilo que tenho sofrido pela causa de Jesus.

18Que a graça do nosso Senhor Jesus Cristo esteja sempre com o vosso espírito, meus irmãos. Amém!