Agalatiya 6 – CCL & NCA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Agalatiya 6:1-18

Kuchita Zabwino kwa Onse

1Abale, ngati munthu agwa mʼtchimo lililonse, inu amene Mzimu amakutsogolerani, mumuthandize munthuyo ndi mtima wofatsa kuti akonzekenso. Koma mukhale maso kuti inu nomwe mungayesedwe. 2Thandizanani kusenza zolemetsa zanu, ndipo mʼnjira imeneyi mudzakwanitsa lamulo la Khristu. 3Ngati wina adziyesa kanthu pamene iyeyo sali kanthu konse, akudzinamiza yekha. 4Munthu aliyense aziyesa yekha ntchito zake mmene zilili. Ngati zili bwino, adzatha kunyadira chifukwa cha ntchito zake zokhazo, iyeyo asadzifanizire ndi munthu wina wake, 5pakuti aliyense ayenera kusenza katundu wake.

6Koma munthu amene akuphunzira mawu, agawireko mphunzitsi wake zinthu zonse zabwino zimene iye ali nazo.

7Musanamizidwe: nʼkosatheka kupusitsa Mulungu. Munthu amakolola zimene wafesa. 8Pakuti amene amafesa zokondweretsa thupi lake la uchimo, kuchokera ku khalidwe limenelo adzakolola chiwonongeko; amene amafesa zokondweretsa Mzimu, kuchokera kwa Mzimu adzakolola moyo wosatha. 9Tisatope nʼkuchita zabwino, pakuti pa nthawi yoyenera tidzakolola ngati sititopa. 10Nʼchifukwa chake ngati tapeza mpata, tiyenera kuchitira zabwino anthu onse, makamaka amene ndi a banja la okhulupirira.

Osati Mdulidwe koma Kulengedwa Mwatsopano

11Onani zilembo zazikulu zimene ine ndikulemba ndi dzanja langa.

12Onse amene akufuna kuoneka abwino pamaso pa anthu akukukakamizani kuti muchite mdulidwe. Akuchita izi ndi cholinga chimodzi chokha, chakuti apewe kuzunzidwa chifukwa cha mtanda wa Khristu. 13Pakuti ngakhale iwowa amene anachita mdulidwe satsata Malamulo, komabe akufuna kuti muchite mdulidwe kuti anyadire mdulidwe wanuwo. 14Ine sindingathe kunyadira kanthu kena koma mtanda wa Ambuye athu Yesu Khristu, kudzera mwa mtandawo dziko lapansi linapachikidwa kwa ine ndi ine ku dziko lapansi. 15Pakuti kaya mdulidwe kapena kusachita mdulidwe, sizitanthauza kanthu; chofunika ndi kulengedwa mwatsopano. 16Mtendere ndi chifundo zikhale kwa onse amene amatsata chiphunzitso ichi, ndi pa Israeli wa Mulungu.

17Pomaliza wina asandivutitse, pakuti mʼthupi mwanga muli zizindikiro za Yesu.

18Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu zikhale ndi mzimu wanu abale. Ameni.

New Chhattisgarhi Translation (नवां नियम छत्तीसगढ़ी)

गलातिया 6:1-18

जम्मो झन के भलई करई

1हे भाईमन हो, यदि कोनो मनखे ह कोनो पाप म पड़ जाथे, त तुमन जऊन मन आतमिक अव, ओला नमरता से संभालव। पर अपन धियान रखव कि कहूं तुमन घलो परिछा म झन पड़ जावव। 2तुमन एक-दूसर के बोझा उठावव, तब ए किसम ले तुमन मसीह के कानून ला पूरा करहू। 3कहूं कोनो मनखे ह ए सोचथे कि ओह कुछू अय, जबकि सही म ओह कुछू नो हय, त ओह अपन-आप ला धोखा देथे। 4हर एक झन अपन खुद के चाल-चलन ला जांचय, तब ओह आने मनखे संग तुलना करे बिगर, अपन चाल-चलन के ऊपर घमंड करय। 5काबरकि हर एक मनखे ला अपन बोझा खुद उठाय बर पड़ही।

6तुमन अपन जम्मो सुघर चीज ला ओकर संग बांटव, जऊन ह तुमन ला परमेसर के बचन के सिकछा देथे।

7धोखा झन खावव: परमेसर के ठट्ठा नइं करे जा सकय। मनखे ह जऊन कुछू बोथे, ओहीच ला लूथे। 8जऊन ह अपन पापी सुभाव ला खुस करे बर बोथे, ओह ओ पापी सुभाव ले बिनास के फसल लूथे; अऊ जऊन ह पबितर आतमा ला खुस करे बर बोथे, ओह पबितर आतमा के दुवारा परमेसर के संग सदाकाल के जिनगी के फसल ला काटही। 9आवव, हमन भलई के काम करे बर झन छोड़न। काबरकि यदि हमन हिम्मत नइं हारन, त सही मऊका म फसल ला लुबो। 10एकरसेति, आवव, जिहां तक हो सकय, हमन जम्मो मनखे के भलई करन, खास करके ओमन के भलई करन, जऊन मन मसीह ऊपर बिसवास करइया परिवार ले आथें।

11देखव, मेंह कइसने बड़े-बड़े अकछर म तुमन ला अपन हांथ ले लिखत हवंव।

12जऊन मन बाहिरी रूप ले परभाव जमाय चाहथें, ओमन तुम्‍हर ऊपर दबाव डारे के कोसिस करथें कि तुमन खतना करवाव। ओमन ए काम सिरिप एकरसेति करथें, ताकि मसीह के कुरुस के कारन ओमन के ऊपर सतावा झन आवय। 13अऊ त अऊ जऊन मन खतना करवाथें, ओमन मूसा के कानून ला नइं मानंय, तभो ले ओमन चाहथें कि तुमन खतना करवाव, ताकि ओमन तुम्‍हर देहें के बारे म डींग मार सकंय। 14ए बात ह मोर ले दूरिहा रहय कि मेंह अऊ काकरो ऊपर घमंड करंव, सिरिप हमर परभू यीसू मसीह के कुरुस के छोंड़, जेकर दुवारा संसार ह मोर बर कुरुस म चघाय गीस अऊ मेंह संसार बर कुरुस म चघाय गेंव। 15काकरो खतना होवय या झन होवय, एकर कोनो मतलब नइं ए; सिरिप नवां सिरिस्टी होना ही जम्मो कुछू अय। 16जऊन मन ए नियम म चलथें, ओ जम्मो झन ऊपर अऊ परमेसर के इसरायल ऊपर सांति अऊ दया होवय।

17आखिरी बात ए अय कि कोनो मोर बर समस्या झन ठाढ़ करय, काबरकि जऊन दागमन मोर देहें म हवय, ओमन साबित करथें कि मेंह यीसू के गुलाम अंव।

18हे भाईमन हो, हमर परभू यीसू मसीह के अनुग्रह तुम्‍हर ऊपर बने रहय। आमीन।