Agalatiya 6 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Agalatiya 6:1-18

Kuchita Zabwino kwa Onse

1Abale, ngati munthu agwa mʼtchimo lililonse, inu amene Mzimu amakutsogolerani, mumuthandize munthuyo ndi mtima wofatsa kuti akonzekenso. Koma mukhale maso kuti inu nomwe mungayesedwe. 2Thandizanani kusenza zolemetsa zanu, ndipo mʼnjira imeneyi mudzakwanitsa lamulo la Khristu. 3Ngati wina adziyesa kanthu pamene iyeyo sali kanthu konse, akudzinamiza yekha. 4Munthu aliyense aziyesa yekha ntchito zake mmene zilili. Ngati zili bwino, adzatha kunyadira chifukwa cha ntchito zake zokhazo, iyeyo asadzifanizire ndi munthu wina wake, 5pakuti aliyense ayenera kusenza katundu wake.

6Koma munthu amene akuphunzira mawu, agawireko mphunzitsi wake zinthu zonse zabwino zimene iye ali nazo.

7Musanamizidwe: nʼkosatheka kupusitsa Mulungu. Munthu amakolola zimene wafesa. 8Pakuti amene amafesa zokondweretsa thupi lake la uchimo, kuchokera ku khalidwe limenelo adzakolola chiwonongeko; amene amafesa zokondweretsa Mzimu, kuchokera kwa Mzimu adzakolola moyo wosatha. 9Tisatope nʼkuchita zabwino, pakuti pa nthawi yoyenera tidzakolola ngati sititopa. 10Nʼchifukwa chake ngati tapeza mpata, tiyenera kuchitira zabwino anthu onse, makamaka amene ndi a banja la okhulupirira.

Osati Mdulidwe koma Kulengedwa Mwatsopano

11Onani zilembo zazikulu zimene ine ndikulemba ndi dzanja langa.

12Onse amene akufuna kuoneka abwino pamaso pa anthu akukukakamizani kuti muchite mdulidwe. Akuchita izi ndi cholinga chimodzi chokha, chakuti apewe kuzunzidwa chifukwa cha mtanda wa Khristu. 13Pakuti ngakhale iwowa amene anachita mdulidwe satsata Malamulo, komabe akufuna kuti muchite mdulidwe kuti anyadire mdulidwe wanuwo. 14Ine sindingathe kunyadira kanthu kena koma mtanda wa Ambuye athu Yesu Khristu, kudzera mwa mtandawo dziko lapansi linapachikidwa kwa ine ndi ine ku dziko lapansi. 15Pakuti kaya mdulidwe kapena kusachita mdulidwe, sizitanthauza kanthu; chofunika ndi kulengedwa mwatsopano. 16Mtendere ndi chifundo zikhale kwa onse amene amatsata chiphunzitso ichi, ndi pa Israeli wa Mulungu.

17Pomaliza wina asandivutitse, pakuti mʼthupi mwanga muli zizindikiro za Yesu.

18Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu zikhale ndi mzimu wanu abale. Ameni.

Священное Писание

Галатам 6:1-18

Что посеет человек, то и пожнёт

1Братья, если кто-то уличён в грехе, то вы, будучи людьми духовными, помогите этому человеку, но делайте это с кротостью. Смотрите, чтобы и вам не поддаться искушению. 2Помогайте друг другу в трудностях, тем самым вы исполните Закон Масиха. 3Если кто-либо мнит о себе больше, чем есть на самом деле, он тем самым лишь обманывает себя. 4Пусть каждый трезво судит о своих делах, тогда он сможет радоваться сделанному, не сравнивая себя с другими, 5потому что каждый отвечает за свои дела.

6Тот, кого наставляют словом, пусть делится всяким добром с тем, кто наставляет его.

7Не поддавайтесь заблуждению: никому не удастся провести Всевышнего. Человек пожнёт то, что он посеял. 8Тот, кто сеет ради угождения своей греховной природе, пожнёт от этой природы гибель. А тот, кто сеет для угождения Духу, от Духа пожнёт вечную жизнь. 9Не уставайте делать добро. Если мы не прекратим делать добро, то настанет время, когда мы соберём и жатву с посеянного. 10Поэтому, пока это возможно, будем делать добро всем, особенно нашим братьям по вере.

Обобщение

11Видите, что с этого места начались большие буквы? Здесь я писал вам своей собственной рукой.

12Те, кто хотят лишь угодить ревнителям Закона, стараются заставить вас принять обрезание. Они делают это только ради того, чтобы не быть преследуемыми за веру в искупительную смерть Масиха на кресте. 13Ведь даже они сами, хотя и обрезанные, не исполняют Закон. Они хотят, чтобы вы были обрезаны для того, чтобы им потом хвалиться этим. 14Я же не хочу хвалиться ничем, кроме искупительной смерти нашего Повелителя Исы Масиха на кресте, благодаря которой мир распят для меня, а я – для мира. 15Ни обрезание, ни необрезание не имеют никакого значения. Главное – это быть новым творением! 16Пусть со всеми, следующими этому правилу, будут мир и милость. Они – Исраил, народ Всевышнего6:16 Или: «…мир и милость, а также с Исраилом, народом Всевышнего»..

17Пусть никто больше не доставляет мне таких переживаний, ведь я на своём теле ношу печать того, что я принадлежу Исе.

18Пусть благодать нашего Повелителя Исы Масиха будет с вашим духом, братья. Аминь.