Agalatiya 1 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Agalatiya 1:1-24

1Paulo mtumwi, osati wosankhidwa ndi anthu kapena kutumidwa ndi munthu ayi, koma Yesu Khristu, ndi Mulungu Atate amene anamuukitsa Yesuyo kwa akufa, 2pamodzi ndi abale onse amene ali nane,

Kulembera mipingo ya ku Galatiya:

3Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale nanu. 4Yesuyo anadzipereka yekha chifukwa cha machimo athu kuti atipulumutse ku njira za moyo woyipa uno, molingana ndi chifuniro cha Mulungu ndi Atate athu. 5Ulemerero ukhale kwa Mulunguyo mpaka muyaya. Ameni.

Uthenga Wabwino ndi Umodzi Wokha

6Ine ndikudabwa kuti mukusiya mwamsangamsanga chotere Mulungu amene anakuyitanani mwachisomo cha Khristu ndipo mwatembenuka ndi kutsatira uthenga wina wosiyana, 7umene si Uthenga Wabwino konse. Pali anthu ena amene akukusokonezani komanso akufuna kupotoza Uthenga Wabwino wa Khristu. 8Ngakhale ife kapena mngelo wochokera kumwamba, akalalikira Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene tinakulalikirani uja, iyeyo akhale wotembereredwa! 9Monga tanena kale, tsopano ndikubwereza kunenanso kuti, “Ngati wina aliyense akulalikirani Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene munawulandira, iyeyo akhale wotembereredwa.”

10Kodi tsopano ndikufuna kukopa anthu kuti andivomereze, kapena Mulungu? Kapena ndikufuna kukondweretsa anthu? Ngati ine ndikanakhala kuti ndikufunabe kukondweretsa anthu, sindikanakhala mtumiki wa Khristu.

Paulo Woyitanidwa ndi Mulungu

11Abale, ine ndikufuna kuti mudziwe, kuti Uthenga Wabwino umene ndinalalikira si ochokera kwa munthu ayi. 12Ine sindinawulandire kuchokera kwa munthu aliyense, kapena kuphunzitsidwa; koma ndinawulandira mwa vumbulutso lochokera kwa Khristu.

13Pakuti inu munamva za moyo wanga wakale mʼChiyuda, mmene ndinkazunzira mpingo wa Mulungu koopsa ndi kuyesetsa kuwuwononga. 14Ine ndinkapambana Ayuda ambiri a msinkhu wanga pochita za Chiyuda, ndipo ndinali wachangu koposa pa miyambo ya makolo athu. 15Koma Mulungu, amene anandipatula ine ndisanabadwe, ndi kundiyitana mwachisomo chake, atakondweretsedwa 16kuvumbulutsa Mwana wake mwa ine, kuti ndikalalikire Khristuyo pakati pa anthu a mitundu ina, ine sindinapemphe nzeru kwa munthu aliyense. 17Ine sindinapite ku Yerusalemu kukaonana ndi amene anali atumwi ine ndisanakhale mtumwi. Mʼmalo mwake nthawi yomweyo ndinapita ku Arabiya ndi kubwereranso ku Damasiko.

18Pambuyo pake, patatha zaka zitatu, ndinapita ku Yerusalemu kukaonana ndi Petro ndikukhala naye masiku khumi ndi asanu. 19Ine sindinaonane ndi atumwi enawo koma Yakobo yekha, mʼbale wa Ambuye. 20Ine ndikutsimikizira inu pamaso pa Mulungu kuti zimene ndikukulemberani si zonama ayi. 21Pambuyo pake ndinapita ku Siriya ndi ku Kilikiya. 22Koma sindimadziwika ndi nkhope ku mipingo ya ku Yudeya imene ili mwa Khristu. 23Iwo anangomva mbiri yokha yakuti, “Munthu amene poyamba anatizunza ife, tsopano akulalikira chikhulupiriro chimene iyeyo nthawi ina anafuna kuchiwononga.” 24Ndipo iwo anayamika Mulungu chifukwa cha ine.

Persian Contemporary Bible

غلاطيان 1:1‏-24

سلام و درود از پولس

1‏-3از طرف من، پولس رسول، و تمام برادرانی كه در اينجا با من می‌باشند،

به كليساهای ايالت غلاطيه.

از درگاه خدای پدر، و خداوندمان عيسی مسيح، طالب رحمت و آرامش برای شما هستم.

اگر من خود را رسول می‌خوانم، منظورم آن نيست كه يک گروه مذهبی يا هيئتی مرا به عنوان رسول به کار گمارده‌اند. رسالت و مأموريت من از جانب عيسی مسيح و خدای پدر است، خدايی كه او را پس از مرگ زنده كرد. 4زيرا مسيح، به خواست پدر ما خدا، جان خود را فدا كرد و مُرد تا گناهان ما بخشيده شود و از اين دنيای آلوده به گناه نجات يابيم. 5خدا را تا به ابد جلال و عزت باد! آمين.

راه رستگاری ديگری وجود ندارد

6تعجب می‌كنم كه شما به اين زودی از خدا روگردان شده‌ايد، از خدايی كه از روی لطف و محبت خود، شما را دعوت كرده تا در حيات جاودانی كه بوسيلهٔ مسيح عطا می‌كند، شريک باشيد. شما می‌خواهيد از «راه ديگری» به اين نجات و حيات جاودانی دست يابيد. اما اين راهی كه شما در پيش گرفته‌ايد، هرگز به حيات جاويد نخواهد رسيد. 7زيرا غير از راهی كه به شما اعلام كرديم، راه ديگری وجود ندارد. آنانی كه راه ديگری به شما معرفی می‌كنند، می‌خواهند شما را فريب داده، حقيقت انجيل مسيح را دگرگون كنند.

8اگر كسی بخواهد راه ديگری برای رستگاری به شما معرفی كند، به غیر از آن راهی كه ما به شما اعلام كرديم، خدا او را لعنت كند، حتی اگر اين شخص خود من باشم. اگر فرشته‌ای نيز از آسمان فرود آيد و شما را به سوی راه ديگری هدايت كند، لعنت خدا بر او باد! 9باز تكرار می‌كنم: اگر كسی مژدهٔ نجات ديگری، غير از آنچه كه پذيرفته‌ايد، به شما ارائه دهد، لعنت خدا بر او باد!

10هدف من اين نيست كه با تملق و چاپلوسی، اعتماد شما را به خود جلب كنم. كوشش من خشنود ساختن خداست؛ اگر تا به حال در پی جلب خشنودی مردم می‌بودم، هرگز نمی‌توانستم خدمتگزار واقعی مسيح باشم.

پولس، پيغام انجيل را از خدا آموخت

11ای برادران، خدا شاهد است كه اين راه نجات كه من بشارت می‌دهم، زاييدهٔ فكر و خيال انسانی نيست. 12زيرا خود عيسی مسيح مستقيماً آن را بر من آشكار و مكشوف ساخت. بلی، من آن را از هيچكس دريافت نكردم و از هيچ انسانی نياموختم.

13بدون شک سرگذشت مرا هنگامی كه هنوز پيرو دين يهود بودم شنيده‌ايد، كه چگونه به تعقيب مسيحيان می‌پرداختم و ايشان را با بی‌رحمی شكنجه و آزار می‌دادم و هميشه در پی آن بودم كه ريشهٔ آنان را از زمين بر كنم. 14من از بيشتر همسالان يهودی خود مؤمن‌تر بودم و نسبت به اجرای رسوم و سنن مذهبم تعصب زيادی داشتم.

15‏-16اما ناگهان همه چيز تغيير كرد! زيرا خدايی كه مرا از شكم مادر برگزيده بود، از روی لطف و رحمتش، فرزند خود را بر من آشكار ساخت و او را به من شناساند تا بتوانم نزد اقوام غيريهودی رفته، راه نجات بوسيلهٔ عيسی مسيح را به ايشان بشارت دهم.

وقتی اين تغيير در من پديد آمد، با هيچكس در اين باره سخن نگفتم. 17حتی به اورشليم هم نرفتم تا با كسانی كه پيش از من به رسالت برگزيده شده بودند، مشورت كنم. بلكه به بيابانهای عربستان رفتم، و پس از مدتی، به شهر «دمشق» بازگشتم. 18بعد از سه سال، سرانجام به اورشليم رفتم تا با پطرس ملاقات كنم. در آنجا مدت پانزده روز با او به سر بردم. 19اما از ساير رسولان، فقط يعقوب، برادر خداوند ما عيسی مسيح را ديدم.

20خدا شاهد است آنچه كه می‌نويسم عين حقيقت است. 21پس از اين ديدار، به ايالات «سوريه» و «قيليقيه» رفتم. 22اما مسيحيان يهوديه هنوز مرا نديده بودند؛ 23فقط اين را از ديگران شنيده بودند كه: «دشمن سابق ما، اكنون همان ايمانی را بشارت می‌دهد كه قبلاً در صدد نابودی آن بود.» 24و اين تغييری كه در من پديد آمده بود، سبب شد كه خدا را تمجيد و ستايش كنند.