Afilipi 4 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Afilipi 4:1-23

1Tsono abale anga, ndimakukondani ndipo ndikukulakalakani. Ndinu chimwemwe changa ndi chipewa cha ulemerero wanga. Abwenzi okondedwa, chilimikani choncho mwa Ambuye.

2Ndikudandaulira Euodiya ndi Suntuke kuti akhale ndi mtima umodzi mwa Ambuye. 3Inde, ndikupempha iwe mnzanga pa ntchitoyi, thandiza amayiwa amene ndagwira nawo ntchito ya Uthenga Wabwino pamodzi ndi Klementonso ndi ena onse antchito anzanga amene mayina awo ali mʼbuku lamoyo.

Malangizo Otsiriza

4Nthawi zonse muzikondwa mwa Ambuye. Ndikubwerezanso; muzikondwa! 5Kufatsa kwanu kuzioneka pamaso pa anthu onse. Ambuye anu ali pafupi. 6Musade nkhawa ndi kanthu kalikonse, koma pa china chilichonse, mwa pemphero ndi chidandaulo pamodzi ndi chiyamiko, perekani zopempha zanu kwa Mulungu. 7Ndipo mtendere wa Mulungu, umene upambana nzeru zonse udzasunga bwino mitima yanu ndi maganizo anu mwa Khristu Yesu.

8Potsiriza, abale, muziyika mtima wanu pa zinthu zilizonse zabwino ndi zotamandika monga, zinthu zoona, zinthu zolemekezeka, zinthu zolungama, zinthu zoyera, zinthu zokongola ndi zinthu zosiririka. 9Muzichita chilichonse chimene mwaphunzira kapena kulandira kapena kumva kuchokera kwa ine kapena mwaona mwa ine. Ndipo Mulungu wamtendere adzakhala nanu.

Kuthokoza Chifukwa cha Mphatso

10Ndikukondwa kwambiri mwa Ambuye kuti patapita nthawi tsopano mwayambanso kuonetsa kuti mumandiganizira. Zoonadi, mwakhala mukundikumbukira, koma munalibe mpata woti muonetsere zimenezi. 11Sindikunena izi chifukwa choti ndikusowa thandizo, poti ine ndaphunzira kukhala wokwaniritsidwa ndi zimene ndili nazo. 12Ndimadziwa kusauka nʼkutani, ndipo ndimadziwa kulemera nʼkutani. Ndaphunzira chinsinsi chokhala wokhutitsidwa mwa njira ina iliyonse, kaya nʼkudya bwino kapena kukhala ndi njala, kaya kukhala ndi chuma kapena umphawi. 13Ndikhoza kuchita zonse kudzera mwa Iye amene amandipatsa mphamvu.

14Komatu munachita bwino kundithandiza mʼmavuto anga. 15Ndipo inu Afilipi mukudziwa kuti masiku oyambirira olalikira Uthenga Wabwino, nditachoka ku Makedoniya, panalibe mpingo ndi umodzi omwe umene unagwirizana nane pa nkhani yopereka ndi kulandira, kupatula inu. 16Pakuti ngakhale pamene ndinali ku Tesalonika, munanditumizira kangapo zondithandiza pa zosowa zanga. 17Osati ndikufuna mphatso zanu, koma ndikufuna kuti pa zimene muli nazo pawonjezerekepo phindu. 18Ndalandira zonse ndipo ndili nazo zokwanira zoposa zosowa zanga popeza ndalandira kwa Epafrodito mphatso zochuluka zimene munatumiza. Ndizo zopereka za fungo labwino, nsembe zolandiridwa zokondweretsa Mulungu. 19Ndipo Mulungu wanga adzakwaniritsa zosowa zanu monga mwa chuma chake chaulemerero mwa Khristu Yesu.

20Kwa Mulungu ndi Atate athu, kukhale ulemerero mpaka muyaya. Ameni.

Malonje Otsiriza

21Perekani moni kwa oyera mtima onse mwa Khristu Yesu. Abale amene ali ndi ine akupereka moni wawo. 22Oyera mtima onse akupereka moni, makamaka iwo a ku nyumba ya Kaisara.

23Chisomo cha Ambuye Yesu Khristu chikhale ndi mzimu wanu. Ameni.

King James Version

Philippians 4:1-23

1Therefore, my brethren dearly beloved and longed for, my joy and crown, so stand fast in the Lord, my dearly beloved. 2I beseech Euodias, and beseech Syntyche, that they be of the same mind in the Lord. 3And I intreat thee also, true yokefellow, help those women which laboured with me in the gospel, with Clement also, and with other my fellowlabourers, whose names are in the book of life. 4Rejoice in the Lord alway: and again I say, Rejoice. 5Let your moderation be known unto all men. The Lord is at hand. 6Be careful for nothing; but in every thing by prayer and supplication with thanksgiving let your requests be made known unto God. 7And the peace of God, which passeth all understanding, shall keep your hearts and minds through Christ Jesus. 8Finally, brethren, whatsoever things are true, whatsoever things are honest, whatsoever things are just, whatsoever things are pure, whatsoever things are lovely, whatsoever things are of good report; if there be any virtue, and if there be any praise, think on these things. 9Those things, which ye have both learned, and received, and heard, and seen in me, do: and the God of peace shall be with you.

10But I rejoiced in the Lord greatly, that now at the last your care of me hath flourished again; wherein ye were also careful, but ye lacked opportunity. 11Not that I speak in respect of want: for I have learned, in whatsoever state I am, therewith to be content. 12I know both how to be abased, and I know how to abound: every where and in all things I am instructed both to be full and to be hungry, both to abound and to suffer need. 13I can do all things through Christ which strengtheneth me. 14Notwithstanding ye have well done, that ye did communicate with my affliction. 15Now ye Philippians know also, that in the beginning of the gospel, when I departed from Macedonia, no church communicated with me as concerning giving and receiving, but ye only. 16For even in Thessalonica ye sent once and again unto my necessity. 17Not because I desire a gift: but I desire fruit that may abound to your account. 18But I have all, and abound: I am full, having received of Epaphroditus the things which were sent from you, an odour of a sweet smell, a sacrifice acceptable, wellpleasing to God. 19But my God shall supply all your need according to his riches in glory by Christ Jesus. 20Now unto God and our Father be glory for ever and ever. Amen.

21Salute every saint in Christ Jesus. The brethren which are with me greet you. 22All the saints salute you, chiefly they that are of Caesar’s household. 23The grace of our Lord Jesus Christ be with you all. Amen.