Afilipi 4 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Afilipi 4:1-23

1Tsono abale anga, ndimakukondani ndipo ndikukulakalakani. Ndinu chimwemwe changa ndi chipewa cha ulemerero wanga. Abwenzi okondedwa, chilimikani choncho mwa Ambuye.

2Ndikudandaulira Euodiya ndi Suntuke kuti akhale ndi mtima umodzi mwa Ambuye. 3Inde, ndikupempha iwe mnzanga pa ntchitoyi, thandiza amayiwa amene ndagwira nawo ntchito ya Uthenga Wabwino pamodzi ndi Klementonso ndi ena onse antchito anzanga amene mayina awo ali mʼbuku lamoyo.

Malangizo Otsiriza

4Nthawi zonse muzikondwa mwa Ambuye. Ndikubwerezanso; muzikondwa! 5Kufatsa kwanu kuzioneka pamaso pa anthu onse. Ambuye anu ali pafupi. 6Musade nkhawa ndi kanthu kalikonse, koma pa china chilichonse, mwa pemphero ndi chidandaulo pamodzi ndi chiyamiko, perekani zopempha zanu kwa Mulungu. 7Ndipo mtendere wa Mulungu, umene upambana nzeru zonse udzasunga bwino mitima yanu ndi maganizo anu mwa Khristu Yesu.

8Potsiriza, abale, muziyika mtima wanu pa zinthu zilizonse zabwino ndi zotamandika monga, zinthu zoona, zinthu zolemekezeka, zinthu zolungama, zinthu zoyera, zinthu zokongola ndi zinthu zosiririka. 9Muzichita chilichonse chimene mwaphunzira kapena kulandira kapena kumva kuchokera kwa ine kapena mwaona mwa ine. Ndipo Mulungu wamtendere adzakhala nanu.

Kuthokoza Chifukwa cha Mphatso

10Ndikukondwa kwambiri mwa Ambuye kuti patapita nthawi tsopano mwayambanso kuonetsa kuti mumandiganizira. Zoonadi, mwakhala mukundikumbukira, koma munalibe mpata woti muonetsere zimenezi. 11Sindikunena izi chifukwa choti ndikusowa thandizo, poti ine ndaphunzira kukhala wokwaniritsidwa ndi zimene ndili nazo. 12Ndimadziwa kusauka nʼkutani, ndipo ndimadziwa kulemera nʼkutani. Ndaphunzira chinsinsi chokhala wokhutitsidwa mwa njira ina iliyonse, kaya nʼkudya bwino kapena kukhala ndi njala, kaya kukhala ndi chuma kapena umphawi. 13Ndikhoza kuchita zonse kudzera mwa Iye amene amandipatsa mphamvu.

14Komatu munachita bwino kundithandiza mʼmavuto anga. 15Ndipo inu Afilipi mukudziwa kuti masiku oyambirira olalikira Uthenga Wabwino, nditachoka ku Makedoniya, panalibe mpingo ndi umodzi omwe umene unagwirizana nane pa nkhani yopereka ndi kulandira, kupatula inu. 16Pakuti ngakhale pamene ndinali ku Tesalonika, munanditumizira kangapo zondithandiza pa zosowa zanga. 17Osati ndikufuna mphatso zanu, koma ndikufuna kuti pa zimene muli nazo pawonjezerekepo phindu. 18Ndalandira zonse ndipo ndili nazo zokwanira zoposa zosowa zanga popeza ndalandira kwa Epafrodito mphatso zochuluka zimene munatumiza. Ndizo zopereka za fungo labwino, nsembe zolandiridwa zokondweretsa Mulungu. 19Ndipo Mulungu wanga adzakwaniritsa zosowa zanu monga mwa chuma chake chaulemerero mwa Khristu Yesu.

20Kwa Mulungu ndi Atate athu, kukhale ulemerero mpaka muyaya. Ameni.

Malonje Otsiriza

21Perekani moni kwa oyera mtima onse mwa Khristu Yesu. Abale amene ali ndi ine akupereka moni wawo. 22Oyera mtima onse akupereka moni, makamaka iwo a ku nyumba ya Kaisara.

23Chisomo cha Ambuye Yesu Khristu chikhale ndi mzimu wanu. Ameni.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

腓立比書 4:1-23

保羅的勸勉

1我所親愛、所想念的弟兄姊妹,你們就是我的喜樂,我的冠冕。我親愛的弟兄姊妹,你們要靠主堅定不移。 2我懇求友阿蝶循都姬要在主裡同心。 3忠心的同工啊,請你幫助她們二人,因為她們曾與我、革利免和其他同工一起為福音辛勞,這些人的名字都記錄在生命冊上了。

4你們要靠主常常喜樂!我再說,你們要喜樂! 5要讓眾人都知道你們是謙和寬容的人。主快來了。 6你們應該一無掛慮,凡事要藉著禱告和祈求,以感恩的心將你們的需要告訴上帝。 7這樣,上帝那超越人所能理解的平安必在基督耶穌裡保守你們的心思意念。

8最後,弟兄姊妹,你們要思想一切真實、可敬、公義、純潔、可愛、有好名聲、有美德和值得讚許的事情。 9你們從我身上學習、領受、看到和聽到的,都要照著去行。這樣,賜平安的上帝就必與你們同在。

致謝

10我在主裡真是非常喜樂,因為你們現在又一次關心我。其實你們向來都很關心我,只是沒有機會。 11我並非有缺乏才這樣說,因為我已經學會在任何處境中都能知足。 12我知道如何過貧窮的日子,也知道如何過富足的日子。我學到了秘訣,不論飽足或饑餓,豐裕或缺乏,在任何情況下都可以處之泰然。 13靠著賜我力量的那位,我凡事都能做。

14然而,你們與我共患難,真是太好了。 15腓立比人啊!你們也知道,在我離開馬其頓傳福音的初期,除了你們以外,沒有別的教會供應我的需要。 16即使我在帖撒羅尼迦的時候,你們也不止一次供應過我的需要。 17我不求得到你們的饋贈,只希望你們所做的會帶給你們更大的賞賜。 18我現在樣樣都有,豐富有餘。我從以巴弗提手上收到了你們送給我的禮物,已經充足了。這些饋贈是蒙上帝悅納的馨香祭物。 19我的上帝必按照祂在基督耶穌裡的榮耀,豐豐富富地賜給你們所需用的一切。

20願榮耀歸給我們的父上帝,直到永永遠遠。阿們!

問候

21請代我問候在基督耶穌裡的眾聖徒。我這裡的弟兄姊妹也問候你們。 22所有的聖徒,特別是在凱撒宮裡工作的人,都問候你們。

23願主耶穌基督的恩典與你們的靈同在!