Afilipi 4 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Afilipi 4:1-23

1Tsono abale anga, ndimakukondani ndipo ndikukulakalakani. Ndinu chimwemwe changa ndi chipewa cha ulemerero wanga. Abwenzi okondedwa, chilimikani choncho mwa Ambuye.

2Ndikudandaulira Euodiya ndi Suntuke kuti akhale ndi mtima umodzi mwa Ambuye. 3Inde, ndikupempha iwe mnzanga pa ntchitoyi, thandiza amayiwa amene ndagwira nawo ntchito ya Uthenga Wabwino pamodzi ndi Klementonso ndi ena onse antchito anzanga amene mayina awo ali mʼbuku lamoyo.

Malangizo Otsiriza

4Nthawi zonse muzikondwa mwa Ambuye. Ndikubwerezanso; muzikondwa! 5Kufatsa kwanu kuzioneka pamaso pa anthu onse. Ambuye anu ali pafupi. 6Musade nkhawa ndi kanthu kalikonse, koma pa china chilichonse, mwa pemphero ndi chidandaulo pamodzi ndi chiyamiko, perekani zopempha zanu kwa Mulungu. 7Ndipo mtendere wa Mulungu, umene upambana nzeru zonse udzasunga bwino mitima yanu ndi maganizo anu mwa Khristu Yesu.

8Potsiriza, abale, muziyika mtima wanu pa zinthu zilizonse zabwino ndi zotamandika monga, zinthu zoona, zinthu zolemekezeka, zinthu zolungama, zinthu zoyera, zinthu zokongola ndi zinthu zosiririka. 9Muzichita chilichonse chimene mwaphunzira kapena kulandira kapena kumva kuchokera kwa ine kapena mwaona mwa ine. Ndipo Mulungu wamtendere adzakhala nanu.

Kuthokoza Chifukwa cha Mphatso

10Ndikukondwa kwambiri mwa Ambuye kuti patapita nthawi tsopano mwayambanso kuonetsa kuti mumandiganizira. Zoonadi, mwakhala mukundikumbukira, koma munalibe mpata woti muonetsere zimenezi. 11Sindikunena izi chifukwa choti ndikusowa thandizo, poti ine ndaphunzira kukhala wokwaniritsidwa ndi zimene ndili nazo. 12Ndimadziwa kusauka nʼkutani, ndipo ndimadziwa kulemera nʼkutani. Ndaphunzira chinsinsi chokhala wokhutitsidwa mwa njira ina iliyonse, kaya nʼkudya bwino kapena kukhala ndi njala, kaya kukhala ndi chuma kapena umphawi. 13Ndikhoza kuchita zonse kudzera mwa Iye amene amandipatsa mphamvu.

14Komatu munachita bwino kundithandiza mʼmavuto anga. 15Ndipo inu Afilipi mukudziwa kuti masiku oyambirira olalikira Uthenga Wabwino, nditachoka ku Makedoniya, panalibe mpingo ndi umodzi omwe umene unagwirizana nane pa nkhani yopereka ndi kulandira, kupatula inu. 16Pakuti ngakhale pamene ndinali ku Tesalonika, munanditumizira kangapo zondithandiza pa zosowa zanga. 17Osati ndikufuna mphatso zanu, koma ndikufuna kuti pa zimene muli nazo pawonjezerekepo phindu. 18Ndalandira zonse ndipo ndili nazo zokwanira zoposa zosowa zanga popeza ndalandira kwa Epafrodito mphatso zochuluka zimene munatumiza. Ndizo zopereka za fungo labwino, nsembe zolandiridwa zokondweretsa Mulungu. 19Ndipo Mulungu wanga adzakwaniritsa zosowa zanu monga mwa chuma chake chaulemerero mwa Khristu Yesu.

20Kwa Mulungu ndi Atate athu, kukhale ulemerero mpaka muyaya. Ameni.

Malonje Otsiriza

21Perekani moni kwa oyera mtima onse mwa Khristu Yesu. Abale amene ali ndi ine akupereka moni wawo. 22Oyera mtima onse akupereka moni, makamaka iwo a ku nyumba ya Kaisara.

23Chisomo cha Ambuye Yesu Khristu chikhale ndi mzimu wanu. Ameni.

La Bible du Semeur

Philippiens 4:1-23

1Ainsi donc, mes frères et sœurs bien-aimés, vous que je désire tant revoir, vous qui êtes ma joie et ma couronne, c’est de cette manière, mes chers amis, que vous devez tenir ferme, en restant attachés au Seigneur.

Recommandations

2Je recommande à Evodie et à Syntyche4.2 Deux anciennes collaboratrices de Paul opposées maintenant par un différend suffisamment grave pour qu’il soit parvenu aux oreilles de l’apôtre. de vivre en parfaite harmonie, l’une avec l’autre, selon le Seigneur ; je les y invite instamment.

3Toi, mon fidèle collègue4.3 Paul s’adresse sans doute à l’un des responsables de l’Eglise. Peut-être le mot susugos traduit par collègue est-il le nom d’un responsable. L’apôtre jouerait ainsi sur le sens de ce nom (comme il l’a fait dans Phm 11)., je te le demande : viens-leur en aide, car elles ont combattu à mes côtés pour la cause de l’Evangile, tout comme Clément et mes autres collaborateurs dont les noms sont inscrits dans le livre de vie4.3 Voir Ap 3.5..

4Réjouissez-vous en tout temps de tout ce que le Seigneur est pour vous. Oui, je le répète, soyez dans la joie. 5Faites-vous connaître par votre amabilité envers tous les hommes. Le Seigneur est proche. 6Ne vous mettez en souci pour rien, mais, en toute chose, exposez vos demandes à Dieu en lui adressant vos prières et vos supplications, tout en lui exprimant votre reconnaissance.

7Alors la paix de Dieu, qui surpasse tout ce qu’on peut concevoir, gardera votre cœur et votre pensée sous la protection de Jésus-Christ.

8Enfin, frères et sœurs, nourrissez vos pensées4.8 Autre traduction : tenez compte de. de tout ce qui est vrai, noble, juste, pur, digne d’amour ou d’approbation, de tout ce qui est vertueux et mérite louange.

9Ce que vous avez appris et reçu de moi, ce que vous m’avez entendu dire et vu faire, mettez-le en pratique. Alors le Dieu qui donne la paix sera avec vous.

Reconnaissance de Paul

10Je me suis profondément réjoui, dans le Seigneur, en voyant que votre intérêt pour moi a pu finalement porter de nouveaux fruits. Car cette sollicitude à mon égard, vous l’éprouviez toujours, mais vous n’aviez pas eu l’occasion de la manifester.

11Ce n’est pas le besoin qui me fait parler ainsi, car j’ai appris en toutes circonstances à être content avec ce que j’ai. 12Je sais vivre dans le dénuement, je sais aussi vivre dans l’abondance. C’est le secret que j’ai appris : m’accommoder à toutes les situations et toutes les circonstances, que je sois rassasié ou que j’aie faim, que je connaisse l’abondance ou que je sois dans le besoin. 13Je peux tout, grâce à celui qui me fortifie.

14Pourtant, vous avez bien fait de prendre part à ma détresse. 15Comme vous le savez, Philippiens, dans les premiers temps de mon activité pour la cause de l’Evangile, lorsque j’ai quitté la Macédoine4.15 Voir note 2 Co 1.16., aucune autre Eglise n’est entrée avec moi dans un échange réciproque de dons matériels et spirituels4.15 Paul utilise une expression du langage commercial désignant un compte de profits et pertes.. Vous seuls l’avez fait.

16Pendant mon séjour à Thessalonique, vous m’avez envoyé, par deux fois, des dons pour subvenir à mes besoins.

17Ce n’est pas que je tienne à recevoir des dons ; ce qui m’intéresse, c’est qu’un plus grand nombre de fruits soit porté à votre actif.

18J’atteste par cette lettre avoir reçu tous vos dons, et je suis dans l’abondance. Depuis qu’Epaphrodite me les a remis, je suis comblé. Ils ont été pour moi comme le doux parfum d’une offrande agréée par Dieu et qui lui fait plaisir.

19Aussi, mon Dieu subviendra pleinement à tous vos besoins ; il le fera, selon sa glorieuse richesse qui se manifeste en Jésus-Christ. 20A notre Dieu et Père soit la gloire dans tous les siècles ! Amen !

Salutations

21Saluez tous ceux qui, par leur union avec Jésus-Christ, font partie du peuple saint.

Les frères qui sont ici avec moi vous saluent. 22Tous les membres du peuple saint vous adressent leurs salutations, et en particulier ceux qui sont au service de l’empereur.

23Que la grâce du Seigneur Jésus-Christ soit avec vous.