Afilipi 3 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Afilipi 3:1-21

Osakhulupirira za Thupi

1Abale anga, ndikupitiriza kunena kuti, kondwani mwa Ambuye! Sizondivuta kuti ndilembenso mawu omwewo, ndipo zimenezi nʼzokuthandizani inuyo.

2Chenjerani ndi agalu amenewa, anthu ochita zoyipa, anthu amene amadula thupi lawo. 3Pakuti ochita mdulidwe weniweni ndife. Ife amene timatumikira Mulungu motsogozedwa ndi Mzimu. Ife amene timanyadira Khristu, ndipo sitidalira zinthu za thupi 4ngakhale kuti ineyo ndili ndi zifukwa zokwanira kudalira zinthu za thupizo.

Ngati pali winanso amene akuganiza kuti ali ndi zifukwa zokwanira kudalira zinthu za thupi, ineyo ndili ndi zifukwa zoposa pamenepo. 5Ndinachita mdulidwe pa tsiku lachisanu ndi chitatu nditangobadwa. Ndine wa mtundu wa Israeli, wa fuko la Benjamini, Mhebri wa Ahebri, kunena za malamulo, ndinali Mfarisi. 6Kunena za changu changa, ndinkazunza mpingo. Kunena za chilungamo chopezeka chifukwa chotsata malamulo, ineyo ndinali wopanda cholakwa.

7Koma zonse zimene ndinkaziyesa zaphindu, tsopano ndikuziona kuti nʼzosapindulitsa chifukwa cha Khristu. 8Kuwonjeza pamenepo, ndikuziona zonse kuti nʼzopanda phindu poyerekeza ndi phindu lopambana la kudziwa Khristu Yesu Ambuye anga. Nʼchifukwa cha Yesuyo ndataya zinthu zonse ndipo ndikuziyesa zinyalala kuti ndipindule Khristu 9ndi kuti ndipezeke mwa Iyeyo, osati ndi chilungamo changa chobwera chifukwa chotsata malamulo, koma chimene chimabwera chifukwa chokhulupirira Khristu. Chilungamochi nʼchochokera kwa Mulungu, timachilandira mwachikhulupiriro. 10Ine ndikufuna kudziwa Khristu, ndithu, kudziwa mphamvu zake za kuuka kwa akufa. Ndikufuna kuyanjana naye mʼmasautso ake, kufanana naye pa imfa yake 11kuti nanenso ndidzaukitsidwe kwa akufa.

Kuthamanga Mpaka Kumapeto pa Mpikisano wa Liwiro

12Sikuti ndazipeza kale zonsezi, kapena kuti ndakhala kale wangwiro, koma ndikuthamangabe ndi kuyesetsa kuti ndipeze chimene Khristu Yesu anandiyitanira. 13Abale, sindidziyesera ndekha kuti ndachipeza kale chimenechi. Koma chinthu chimodzi chimene ndimachita, nʼkuyiwala zamʼmbuyo ndi kuthamangira molimbika zinthu zimene zili mʼtsogolo mwanga. 14Ndikuthamangira kokathera mpikisanowo kuti ndikalandire mphotho imeneyi kumwamba, imene Mulungu anandiyitanira mwa Khristu Yesu.

Kutsanzira Paulo

15Choncho ife tonse amene tili okhwima pa moyo wauzimu, tikhale ndi maganizo omwewa. Ndipo ngati pena ndi pena muli ndi maganizo osiyana ndi amenewa, pameneponso Mulungu adzakuwunikirani. 16Tiyeni ife tizikhala mogwirizana ndi zimene tinapeza kale basi.

17Abale, nonsenu pamodzi mudzinditsanzira ine, ndipo monga inu muli ndi chitsanzo, phunzirani kwa amene akukhala moyo motsatira momwe timakhalira. 18Pakuti monga ndakhala ndikukuwuzani kawirikawiri mʼmbuyomu, ndipo tsopano ndikunenanso ndi misozi kuti, anthu ambiri akukhala monga adani a mtanda wa Khristu. 19Mapeto awo ndi chiwonongeko, mulungu wawo ndi mimba zawo, ndipo ulemerero wawo ndi manyazi awo. Mtima wawo uli pa zinthu za dziko lapansi. 20Koma ife ndife nzika za kumwamba ndipo tikudikirira mwachidwi Mpulumutsi wochokera kumeneko, Ambuye Yesu Khristu. 21Iyeyo, ndi mphamvu imene imamuthandiza kukhazikitsa zinthu zonse pansi pa ulamuliro wake, adzasintha matupi athu achabewa kuti akhale ofanana ndi thupi lake la ulemerero.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Филиппийцам 3:1-21

Предостережение против тех, кто надеется на свою праведность

1Наконец, братья, радуйтесь, будучи верующими в Повелителя! Мне не трудно писать об этом ещё и ещё раз, потому что для вас это будет надёжней.

2Берегитесь псов – людей, делающих зло, «членовредителей», требующих обрезания3:2 Это были лжеучители, которые проповедовали, что для спасения необходимо быть обрезанным.. 3Истинно обрезанные – это мы с вами, поклоняющиеся под руководством Духа Аллаха, хвалящиеся Исой аль-Масихом и не полагающиеся на внешнее, 4хотя я и могу полагаться на это. Если у кого-то и есть основания полагаться на внешнее, то тем более у меня. 5Я был обрезан на восьмой день от рождения3:5 Согласно Закону Аллаха иудеи обрезывают своих сыновей на восьмой день от рождения (см. Нач. 17:12)., происхожу из исраильского народа, из рода Вениамина. Я чистокровный еврей и по отношению к Закону – блюститель Закона3:5 Блюститель Закона (букв.: «фарисей») – член религиозной партии, которую отличало неукоснительное выполнение законов Таурата, следование обычаям предков и строгое соблюдение ритуальной чистоты.. 6Я ревностно преследовал верующих в Ису аль-Масиха и с точки зрения законнической праведности – беспорочен.

7Но всё, что я считал приобретением тогда, сейчас ради аль-Масиха считаю потерей. 8И не только это, но и всё прочее я считаю потерей в сравнении с бесценным познанием моего Повелителя Исы аль-Масиха. Ради Него всё остальное в мире я стал почитать за навоз, и я всё отбросил прочь ради приобретения аль-Масиха, 9ради того, чтобы быть с Ним не со своей уже праведностью от исполнения Закона, но с праведностью по вере в аль-Масиха, праведностью, приходящей от Аллаха через веру. 10Я хочу познать аль-Масиха и ту силу, что воскресила Его, я хочу разделить с Ним Его страдания и стать как Он в Его смерти. 11Тогда, надеюсь, я достигну и воскресения из мёртвых.

12Не то, чтобы я уже приобрёл это или уже стал совершенным, но я стремлюсь приобрести, потому что меня приобрёл Иса аль-Масих. 13Братья, я не считаю, что я уже достиг этого, а лишь забывая всё, что осталось позади, иду к тому, что впереди. 14Я стремительно бегу к финишу, чтобы получить небесную награду, к которой призвал нас Аллах через Ису аль-Масиха.

15Нам всем, духовно зрелым людям, следовало бы так смотреть на вещи. Если же вы в чём-то мыслите иначе, то и это Аллах вам откроет. 16Но давайте будем жить согласно тому, чего мы уже достигли.

Наша Родина на небесах

17Подражайте мне, братья, и возьмите за образец тех, кто уже следует примеру, который вы имеете в нас. 18Потому что многие, о которых я вам говорил раньше и сейчас говорю со слезами на глазах, живут как враги искупительной смерти аль-Масиха на кресте. 19Их конец – погибель, их бог – это их желудок, и то, чем они хвалятся, позорит их; их мысли направлены на земное. 20Наша же Родина на небесах, и оттуда мы ожидаем Спасителя Ису аль-Масиха. 21Ему дана сила покорить Себе всё, и действием этой силы Он изменит наши униженные тела так, что они будут подобны Его славному телу.